Rute 4 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Rute 4:1-22

Bowazi Akwatira Rute

1Nthawi yomweyo Bowazi anapita ku chipata cha mzinda ndi kukhala pansi kumeneko pabwalo losonkhanira. Tsono anangoona wachibale woyenera kulowa chokolo uja akufika. Ndipo Bowazi anati, “Patukirani kuno, bwenzi langa. Mubwere mudzakhale apa.” Choncho anapatuka nakakhala pansi.

2Bowazi anayitananso akuluakulu khumi a mu mzindamo nati, “Dzakhaleni pansi apa,” ndipo anadzakhala pansi.

3Kenaka anamuwuza oyenera kulowa chokolo uja kuti, “Naomi amene wabwera kuchoka ku Mowabu akugulitsa malo amene anali a malemu Elimeleki, mʼbale wathu uja. 4Choncho ndinaganiza zokuwuza zimenezi kuti ugule mundawu pamaso pa anthu amene ali panowa, ndi pamaso pa akuluakulu mwa abale athu. Ngati ukufuna kuwuwombola, uwombole. Koma ngati sukufuna, undiwuze kuti ndidziwe, pakuti palibe wina angawuwombole koma iweyo, ndipo pambuyo pa iwe pali ine.” Iye anati, “Ine ndidzawuwombola.”

5Tsono Bowazi anati, “Tsiku limene ukagule mundawo kwa Naomi, udzatenganso Rute Mmowabu, mkazi wamasiye uja, kuti dzina la malemu lisungike pa cholowa chake.”

6Pamenepo wachibaleyo anati, “Sindingathe kuwuwombola mundawu kuti ukhale wanga, kuopa kuti kutaya cholowa changa. Mugule ndinu. Ine sindingathe.”

7(Kale mu Israeli zinkatere ngati munthu afuna kuwombola kanthu kapena kusinthana kanthu ndi mnzake kuti chikhale chakechake. Iye ankavula nsapato imodzi namupatsa mnzakeyo. Imeneyo ndiyo inali njira yochitira umboni mu Israeli).

8Choncho wachibale uja atawuza Bowazi kuti, “Gulani ndinu mundawu.” Iye anavula nsapato yake namupatsa Bowazi.

9Ndipo Bowazi anawuza akuluakuluwo ndi anthu onse aja kuti, “Nonsenu ndinu mboni lero, kuti ine ndagula kwa Naomi zonse zimene zinali za malemu Elimeleki, zonse zimene zinali za malemu Kiliyoni ndiponso za malemu Maloni. 10Ndatenganso Rute Mmowabu uja mkazi wa malemu Maloni, kuti akhale mkazi wanga, kuti dzina la malemu Maloni lisungike pa cholowa chake, ndipo lisafafanizike pakati pa abale ake ngakhalenso mʼmudzi mwake. Nonsenu ndinu mboni lero lino.”

11Ndipo akuluakulu aja ndi anthu onse amene anali pa chipata anati, “Ife ndife mboni, ndipo Yehova amusandutsa mkazi amene akudzalowa mʼnyumba yakoyu kuti akhale ngati Rakele ndi Leya, amene anamanga banja la Israeli. Ukhale munthu wosasowa kanthu mu Efurata ndi munthu wotchuka mu Betelehemu. 12Ana amene Yehova adzakupatsa mwa mkaziyu adzamange banja lako kukhala la Perezi, amene Tamara anamubalira Yuda.”

Makolo a Davide

13Choncho Bowazi anakwatira Rute. Yehova anamudalitsa nakhala ndi pakati, ndipo anabereka mwana wamwamuna.

14Ndipo amayi osiyanasiyana anati kwa Naomi. “Alemekezeke Yehova, amene lero lino sanakusiyeni nokha wopanda wachibale. Mwanayu dzina lake likhale lotchuka mu Israeli. 15Mwanayo adzakupatseni moyo watsopano ndi kukuthandizani pa ukalamba wanu. Inde, mpongozi wanu amene amakukondani, amenenso waonetsa kuti ali wopambana kwa inu kuposa ana aamuna asanu ndi awiri, ndiye wakubalirani mwanayu.”

16Kenaka Naomi anatenga mwanayo namufukata ndipo anakhala mlezi.

17Amayi achinansi ake anati, “Naomi ali ndi mwana wamwamuna.” Ndipo anamutcha dzina lake Obedi. Iye anali abambo a Yese abambo ake a Davide.

18Izi tsono ndizo zidzukulu za Perezi:

Perezi anali abambo a Hezironi.

19Hezironi anali abambo a Ramu,

Ramu anali abambo a Aminadabu,

20Aminadabu abambo a Naasoni,

Naasoni anali abambo a Salimoni,

21Salimoni abambo a Bowazi,

Bowazi abambo a Obedi.

22Obedi anali abambo a Yese,

ndipo Yese anali abambo a Davide.

New International Reader’s Version

Ruth 4:1-22

Boaz Marries Ruth

1Boaz went up to the town gate and sat down there. Right then, the family protector he had talked about came by. Then Boaz said, “Come over here, my friend. Sit down.” So the man went over and sat down.

2Boaz brought ten of the elders of the town together. He said, “Sit down here.” So they did. 3Then he spoke to the family protector. He said, “Naomi has come back from Moab. She’s selling the piece of land that belonged to our relative Elimelek. 4I thought I should bring the matter to your attention. I suggest that you buy the land. Buy it while those sitting here and the elders of my people are looking on as witnesses. If you are willing to buy it back, do it. But if you aren’t, tell me. Then I’ll know. No one has the right to buy it back except you. And I’m next in line.”

“I’ll buy it,” he said.

5Then Boaz said, “When you buy the property from Naomi, you must also marry Ruth. She is from Moab and is the dead man’s widow. So you must marry her. That’s because his property must continue to belong to his family.”

6When the family protector heard that, he said, “Then I can’t buy the land. If I did, I might put my own property in danger. So you buy it. I can’t do it.”

7In earlier times in Israel, there was a certain practice. It was used when family land was bought back and changed owners. The practice made the sale final. One person would take his sandal off and give it to the other. That was how people in Israel showed that a business matter had been settled.

8So the family protector said to Boaz, “Buy it yourself.” And he took his sandal off.

9Then Boaz said to the elders and all the people, “Today you are witnesses. You have seen that I have bought land from Naomi. I have bought all the property that had belonged to Elimelek, Kilion and Mahlon. 10I’ve also taken Ruth, who is from Moab, to become my wife. She is Mahlon’s widow. I’ve decided to marry her so the dead man’s name will stay with his property. Now his name won’t disappear from his family line or from his hometown. Today you are witnesses!”

11Then the elders and all the people at the gate said, “We are witnesses. The woman is coming into your home. May the Lord make her like Rachel and Leah. Together they built up the family of Israel. May you be an important person in Ephrathah. May you be famous in Bethlehem. 12The Lord will give you children through this young woman. May your family be like the family of Perez. He was the son Tamar had by Judah.”

Naomi Gains a Son

13So Boaz married Ruth. Then he slept with her. The Lord blessed her so that she became pregnant. And she had a son. 14The women said to Naomi, “We praise the Lord. Today he has provided a family protector for you. May this child become famous all over Israel! 15He will make your life new again. He’ll take care of you when you are old. He’s the son of your very own daughter-in-law. She loves you. She is better to you than seven sons.”

16Then Naomi took the child in her arms and took care of him. 17The women living there said, “Naomi has a son!” They named him Obed. He was the father of Jesse. Jesse was the father of David.

18Here is the family line of Perez.

Perez was the father of Hezron.

19Hezron was the father of Ram.

Ram was the father of Amminadab.

20Amminadab was the father of Nahshon.

Nahshon was the father of Salmon.

21Salmon was the father of Boaz.

Boaz was the father of Obed.

22Obed was the father of Jesse.

And Jesse was the father of David.