Rute 4 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Rute 4:1-22

Bowazi Akwatira Rute

1Nthawi yomweyo Bowazi anapita ku chipata cha mzinda ndi kukhala pansi kumeneko pabwalo losonkhanira. Tsono anangoona wachibale woyenera kulowa chokolo uja akufika. Ndipo Bowazi anati, “Patukirani kuno, bwenzi langa. Mubwere mudzakhale apa.” Choncho anapatuka nakakhala pansi.

2Bowazi anayitananso akuluakulu khumi a mu mzindamo nati, “Dzakhaleni pansi apa,” ndipo anadzakhala pansi.

3Kenaka anamuwuza oyenera kulowa chokolo uja kuti, “Naomi amene wabwera kuchoka ku Mowabu akugulitsa malo amene anali a malemu Elimeleki, mʼbale wathu uja. 4Choncho ndinaganiza zokuwuza zimenezi kuti ugule mundawu pamaso pa anthu amene ali panowa, ndi pamaso pa akuluakulu mwa abale athu. Ngati ukufuna kuwuwombola, uwombole. Koma ngati sukufuna, undiwuze kuti ndidziwe, pakuti palibe wina angawuwombole koma iweyo, ndipo pambuyo pa iwe pali ine.” Iye anati, “Ine ndidzawuwombola.”

5Tsono Bowazi anati, “Tsiku limene ukagule mundawo kwa Naomi, udzatenganso Rute Mmowabu, mkazi wamasiye uja, kuti dzina la malemu lisungike pa cholowa chake.”

6Pamenepo wachibaleyo anati, “Sindingathe kuwuwombola mundawu kuti ukhale wanga, kuopa kuti kutaya cholowa changa. Mugule ndinu. Ine sindingathe.”

7(Kale mu Israeli zinkatere ngati munthu afuna kuwombola kanthu kapena kusinthana kanthu ndi mnzake kuti chikhale chakechake. Iye ankavula nsapato imodzi namupatsa mnzakeyo. Imeneyo ndiyo inali njira yochitira umboni mu Israeli).

8Choncho wachibale uja atawuza Bowazi kuti, “Gulani ndinu mundawu.” Iye anavula nsapato yake namupatsa Bowazi.

9Ndipo Bowazi anawuza akuluakuluwo ndi anthu onse aja kuti, “Nonsenu ndinu mboni lero, kuti ine ndagula kwa Naomi zonse zimene zinali za malemu Elimeleki, zonse zimene zinali za malemu Kiliyoni ndiponso za malemu Maloni. 10Ndatenganso Rute Mmowabu uja mkazi wa malemu Maloni, kuti akhale mkazi wanga, kuti dzina la malemu Maloni lisungike pa cholowa chake, ndipo lisafafanizike pakati pa abale ake ngakhalenso mʼmudzi mwake. Nonsenu ndinu mboni lero lino.”

11Ndipo akuluakulu aja ndi anthu onse amene anali pa chipata anati, “Ife ndife mboni, ndipo Yehova amusandutsa mkazi amene akudzalowa mʼnyumba yakoyu kuti akhale ngati Rakele ndi Leya, amene anamanga banja la Israeli. Ukhale munthu wosasowa kanthu mu Efurata ndi munthu wotchuka mu Betelehemu. 12Ana amene Yehova adzakupatsa mwa mkaziyu adzamange banja lako kukhala la Perezi, amene Tamara anamubalira Yuda.”

Makolo a Davide

13Choncho Bowazi anakwatira Rute. Yehova anamudalitsa nakhala ndi pakati, ndipo anabereka mwana wamwamuna.

14Ndipo amayi osiyanasiyana anati kwa Naomi. “Alemekezeke Yehova, amene lero lino sanakusiyeni nokha wopanda wachibale. Mwanayu dzina lake likhale lotchuka mu Israeli. 15Mwanayo adzakupatseni moyo watsopano ndi kukuthandizani pa ukalamba wanu. Inde, mpongozi wanu amene amakukondani, amenenso waonetsa kuti ali wopambana kwa inu kuposa ana aamuna asanu ndi awiri, ndiye wakubalirani mwanayu.”

16Kenaka Naomi anatenga mwanayo namufukata ndipo anakhala mlezi.

17Amayi achinansi ake anati, “Naomi ali ndi mwana wamwamuna.” Ndipo anamutcha dzina lake Obedi. Iye anali abambo a Yese abambo ake a Davide.

18Izi tsono ndizo zidzukulu za Perezi:

Perezi anali abambo a Hezironi.

19Hezironi anali abambo a Ramu,

Ramu anali abambo a Aminadabu,

20Aminadabu abambo a Naasoni,

Naasoni anali abambo a Salimoni,

21Salimoni abambo a Bowazi,

Bowazi abambo a Obedi.

22Obedi anali abambo a Yese,

ndipo Yese anali abambo a Davide.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

路得记 4:1-22

波阿斯娶路得

1波阿斯来到城门口,坐在那里,恰巧看见他所说的那位至亲经过,便招呼他说:“某人啊,请过来坐一坐。”那人便走过来坐下。 2波阿斯又邀请了城里的十位长老,对他们说:“请过来坐一坐。”他们都坐下以后, 3波阿斯便对那位至亲说:“拿俄米摩押回来了,现在要卖我们族兄以利米勒的那块地, 4我想应该让你知道这件事。你最有权赎那块地,其次才是我,此外再没有别人了。如果你愿意赎回那块地,希望你当着在座各位长老的面表明。如果不愿意,请你让我知道。”那人说:“我愿意赎。” 5波阿斯说:“那么,你从拿俄米手中买地的那天,也要娶已死之人的妻子摩押女子路得,好让死者继续在产业上留名。” 6那位至亲说:“那我就不能赎了,免得损害到我的产业。你来赎吧,我不能赎。”

7从前在以色列,买赎或交易有这样的规矩:一旦成交,一方要把鞋脱下来交给另一方,以色列人以此为成交的凭据。 8那位至亲对波阿斯说:“你自己买吧!”他就把鞋子脱了下来。 9波阿斯向长老和所有在场的人说:“请各位今天为我作证,所有属于以利米勒基连玛伦的产业,我都从拿俄米手上买了。 10同时,我要娶玛伦的遗孀摩押女子路得为妻,好使死者继续在产业上留名,免得他的名在本族本乡中消失。今天,请各位作证。” 11聚集在城门口的众人和长老都说:“我们愿意作证。愿耶和华使要进你家门的这女子,像建立以色列家的拉结利亚一样。愿你在以法他家业兴隆,在伯利恒声名远播。 12愿耶和华借着这年轻女子赐你后裔,使你家像先祖犹大她玛的儿子法勒斯家一样。”

13这样,波阿斯便娶了路得为妻,与她同房。耶和华使她怀孕生了一个儿子。 14妇女们对拿俄米说:“耶和华当受称颂!因为今日祂赐给你一位至亲,使你后继有人,愿这孩子在以色列得享盛名! 15他必让你的生命重新得力,奉养你,使你安度晚年,因为他是爱你的儿媳妇所生的。有这儿媳妇比有七个儿子还要好!” 16拿俄米接过婴孩抱在怀中,照顾他。 17邻居的妇女们喊着说:“拿俄米有孩子了!”她们给孩子取名叫俄备得,这俄备得就是耶西的父亲,耶西大卫的父亲。

18以下是法勒斯的家谱:法勒斯希斯仑19希斯仑亚米拿达20亚米拿达拿顺拿顺撒门21撒门波阿斯波阿斯俄备得22俄备得耶西耶西大卫