Rute 4 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Rute 4:1-22

Bowazi Akwatira Rute

1Nthawi yomweyo Bowazi anapita ku chipata cha mzinda ndi kukhala pansi kumeneko pabwalo losonkhanira. Tsono anangoona wachibale woyenera kulowa chokolo uja akufika. Ndipo Bowazi anati, “Patukirani kuno, bwenzi langa. Mubwere mudzakhale apa.” Choncho anapatuka nakakhala pansi.

2Bowazi anayitananso akuluakulu khumi a mu mzindamo nati, “Dzakhaleni pansi apa,” ndipo anadzakhala pansi.

3Kenaka anamuwuza oyenera kulowa chokolo uja kuti, “Naomi amene wabwera kuchoka ku Mowabu akugulitsa malo amene anali a malemu Elimeleki, mʼbale wathu uja. 4Choncho ndinaganiza zokuwuza zimenezi kuti ugule mundawu pamaso pa anthu amene ali panowa, ndi pamaso pa akuluakulu mwa abale athu. Ngati ukufuna kuwuwombola, uwombole. Koma ngati sukufuna, undiwuze kuti ndidziwe, pakuti palibe wina angawuwombole koma iweyo, ndipo pambuyo pa iwe pali ine.” Iye anati, “Ine ndidzawuwombola.”

5Tsono Bowazi anati, “Tsiku limene ukagule mundawo kwa Naomi, udzatenganso Rute Mmowabu, mkazi wamasiye uja, kuti dzina la malemu lisungike pa cholowa chake.”

6Pamenepo wachibaleyo anati, “Sindingathe kuwuwombola mundawu kuti ukhale wanga, kuopa kuti kutaya cholowa changa. Mugule ndinu. Ine sindingathe.”

7(Kale mu Israeli zinkatere ngati munthu afuna kuwombola kanthu kapena kusinthana kanthu ndi mnzake kuti chikhale chakechake. Iye ankavula nsapato imodzi namupatsa mnzakeyo. Imeneyo ndiyo inali njira yochitira umboni mu Israeli).

8Choncho wachibale uja atawuza Bowazi kuti, “Gulani ndinu mundawu.” Iye anavula nsapato yake namupatsa Bowazi.

9Ndipo Bowazi anawuza akuluakuluwo ndi anthu onse aja kuti, “Nonsenu ndinu mboni lero, kuti ine ndagula kwa Naomi zonse zimene zinali za malemu Elimeleki, zonse zimene zinali za malemu Kiliyoni ndiponso za malemu Maloni. 10Ndatenganso Rute Mmowabu uja mkazi wa malemu Maloni, kuti akhale mkazi wanga, kuti dzina la malemu Maloni lisungike pa cholowa chake, ndipo lisafafanizike pakati pa abale ake ngakhalenso mʼmudzi mwake. Nonsenu ndinu mboni lero lino.”

11Ndipo akuluakulu aja ndi anthu onse amene anali pa chipata anati, “Ife ndife mboni, ndipo Yehova amusandutsa mkazi amene akudzalowa mʼnyumba yakoyu kuti akhale ngati Rakele ndi Leya, amene anamanga banja la Israeli. Ukhale munthu wosasowa kanthu mu Efurata ndi munthu wotchuka mu Betelehemu. 12Ana amene Yehova adzakupatsa mwa mkaziyu adzamange banja lako kukhala la Perezi, amene Tamara anamubalira Yuda.”

Makolo a Davide

13Choncho Bowazi anakwatira Rute. Yehova anamudalitsa nakhala ndi pakati, ndipo anabereka mwana wamwamuna.

14Ndipo amayi osiyanasiyana anati kwa Naomi. “Alemekezeke Yehova, amene lero lino sanakusiyeni nokha wopanda wachibale. Mwanayu dzina lake likhale lotchuka mu Israeli. 15Mwanayo adzakupatseni moyo watsopano ndi kukuthandizani pa ukalamba wanu. Inde, mpongozi wanu amene amakukondani, amenenso waonetsa kuti ali wopambana kwa inu kuposa ana aamuna asanu ndi awiri, ndiye wakubalirani mwanayu.”

16Kenaka Naomi anatenga mwanayo namufukata ndipo anakhala mlezi.

17Amayi achinansi ake anati, “Naomi ali ndi mwana wamwamuna.” Ndipo anamutcha dzina lake Obedi. Iye anali abambo a Yese abambo ake a Davide.

18Izi tsono ndizo zidzukulu za Perezi:

Perezi anali abambo a Hezironi.

19Hezironi anali abambo a Ramu,

Ramu anali abambo a Aminadabu,

20Aminadabu abambo a Naasoni,

Naasoni anali abambo a Salimoni,

21Salimoni abambo a Bowazi,

Bowazi abambo a Obedi.

22Obedi anali abambo a Yese,

ndipo Yese anali abambo a Davide.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Рут 4:1-22

Боаз женится на Рут

1А Боаз тем временем направился к городским воротам4:1 Ворота города были центром всей общественной жизни, около них проходили и судебные разбирательства. и сел там. Когда родственник, о котором он говорил, проходил мимо, Боаз сказал:

– Сверни сюда, мой друг, и присядь.

Тот свернул и сел.

2Боаз взял десять человек из старейшин города и сказал им:

– Сядьте здесь. – И они сели.

3После этого он сказал тому родственнику:

– Наоми, которая вернулась из Моава, продаёт участок земли, что принадлежал нашему родичу Эли-Малику. 4Я подумал, что должен довести это до твоего сведения и предложить тебе купить его в присутствии тех, кто сидит здесь, и в присутствии старейшин моего народа. Но если ты не купишь, скажи мне, чтобы я знал. Ведь у тебя первоочередное право сделать это, а я – за тобой.

– Я выкуплю его, – сказал он.

5Тогда Боаз сказал:

– В тот день, когда купишь землю у Наоми, ты также должен будешь жениться на моавитянке Рут, вдове покойного, чтобы, когда у вас родится сын, земля осталась за семьёй покойного.

6Но родственник сказал:

– В таком случае я не могу выкупить этот участок, потому что я подвергну опасности своё собственное имение. Выкупай лучше сам, а я не могу этого сделать.

7(В прежние времена в Исроиле, чтобы выкупить или передать права на собственность, один из участников сделки снимал свою сандалию и отдавал её другому. Такой в Исроиле был обычай узаконивать сделку.)

8Родственник сказал Боазу:

– Покупай сам. – И снял свою сандалию.

9Тогда Боаз объявил старейшинам и всему народу:

– Сегодня вы свидетели того, что я купил у Наоми всё, что принадлежало Эли-Малику, Килеону и Махлону. 10Ещё я приобрёл моавитянку Рут, вдову Махлона, себе в жёны, чтобы сохранить землю за семьёй покойного, чтобы его имя не исчезло среди его родичей и не было забыто в стенах его родного города. Вы сегодня свидетели этого!

11Тогда старейшины и все, кто был у ворот, сказали:

– Мы свидетели. Пусть Вечный сделает плодовитой женщину, которая входит в твой дом, подобно Рахиле и Лии, которые вместе возвели дом Исроила4:11 См. Нач. 29:31–30:24; 35:16-20.. Приобретай богатство в Ефрафе и славься в Вифлееме. 12Пусть через потомство, которое Вечный даст тебе от этой молодой женщины, твой род уподобится роду Фареца, которого Фамарь родила Иуде4:12 История рождения Фареца могла быть здесь упомянута по трём причинам: 1) он появился на свет, как наследник умершего Ира, сына Иуды (см. Нач. 38); 2) Боаз был прямым потомком Фареца (см. 4:18-21); 3) потомки Фареца поселились в Вифлееме (см. 1 Лет. 2:5, 18-19, 50-54)..

Родословие царя Довуда

(1 Лет. 2:5-15; Мат. 1:3-6; Лк. 3:31-33)

13Так Боаз взял Рут, и она стала его женой. Он лёг с ней, и Вечный дал ей зачать, и она родила сына.

14Женщины говорили Наоми:

– Хвала Вечному! Он не оставил тебя сегодня без наследника, который будет заботиться о тебе. Пусть мальчик прославится в Исроиле! 15Он обновит твою жизнь и обеспечит тебя в старости. Ведь его родила твоя сноха, которая любит тебя, и которая для тебя лучше семи сыновей.

16И Наоми взяла младенца, носила его в объятиях и нянчила его. 17Женщины, которые жили там, говорили:

– У Наоми родился сын.

Они назвали его Овид. Он стал отцом Есея, отца Довуда.

18И вот родословие Фареца:

Фарец был отцом Хецрона,

19Хецрон – отцом Рама,

Рам – отцом Аминадава,

20Аминадав – отцом Нахшона,

Нахшон – отцом Салмона,

21Салмон – отцом Боаза,

Боаз – отцом Овида,

22Овид – отцом Есея,

а Есей – отцом Довуда.