Oweruza 9 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 9:1-57

Abimeleki

1Abimeleki mwana wa Yeru-Baala anapita ku Sekemu kwa abale a amayi ake ndi kukawawuza iwowo ndi fuko lonse la banja la abambo a amayi ake kuti, 2“Funsani nzika zonse za ku Sekemu kuno, ‘Chabwino ndi chiyani kwa inu kuti ana onse makumi asanu ndi awiri a Yeru-Baala azikulamulirani, kapena kuti azikulamulirani ndi munthu mmodzi basi?’ Kumbukirani kuti ine ndine mʼbale wanu weniweni.”

3Abale a amayi akewo anamuyankhulira mawu amenewa kwa nzika zonse za ku Sekemu, ndipo mitima ya anthu onse inali pa Abimeleki chifukwa anati, “Uyu ndi mʼbale wathu,” 4Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira. 5Anapita ku Ofiri ku mudzi kwa abambo ake ndipo anapha abale ake makumi asanu ndi awiri, ana a Yeru-Baala pa mwala umodzi. Koma Yotamu yemwe anali wamngʼono mwa onsewo anapulumuka chifukwa anabisala. 6Tsono nzika za ku Sekemu ndi za ku Beti-Milo zinapita kukasonkhana ku mtengo wa thundu pafupi ndi chipilala cha ku Sekemu kuti akalonge Abimeleki ufumu.

7Yotamu atamva izi anapita kukayima pamwamba pa phiri la Gerizimu ndipo anafuwula nati, “Tandimverani inu anthu a ku Sekemu, kuti Mulungu akumvereninso. 8Tsiku lina mitengo inapita kukadzoza mfumu yawo. Tsono mitengoyo inati kwa mtengo wa olivi, ‘Iwe ukhale mfumu yathu.’ ”

9“Koma mtengo wa olivi uja unayankha kuti, ‘Kodi ndisiye mafuta angawa amene amalemekezera nawo milungu ndi anthu omwe, kuti ndizikalamulira mitengo?’ ”

10Apo mitengo inawuza mtengo wa mkuyu kuti, “Bwera ndiwe ukhale mfumu yathu.”

11Koma mtengo wa mkuyu unayankha kuti, “Kodi ndisiye chipatso changa chokoma ndi chozunachi kuti ndizikalamulira mitengo?”

12Kenaka mitengo ija inawuza mtengo wamphesa kuti, “Bwera ndiwe kuti ukhale mfumu yathu.”

13Koma mtengo wamphesa unayankha kuti, “Kodi ine ndisiye vinyo wangayu, amene amasangalatsa milungu ndi anthu omwe kuti ndizikalamulira mitengo?”

14Pomaliza mitengo yonse inawuza mkandankhuku kuti, “Bwera ndipo ukhale mfumu yathu.”

15Mkandankhuku uja unayankha kuti, “Ngati mukufunadi kuti mudzoze ine kuti ndikhale mfumu yanu, bwerani mudzabisale mu mthunzi mwangamu, koma ngati simutero, moto utuluka kwa ine ndi kupsereza mikungudza ya ku Lebanoni.”

16Yotamu anatinso, “Kodi mukuti munaonetsadi kuona mtima ndi kukhulupirika podzoza Abimeleki kukhala mfumu? Kodi mukuti munachitira ulemu Yeru-Baala ndi banja lake poganizira ntchito zimene anachita? 17Kodi suja abambo anga anakumenyerani nkhondo ndi kuyika moyo wawo pa chiswe kuti akupulumutseni mʼmanja mwa Amidiyani? 18Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu. 19Tsono ngati mukuti zimene mwachitira Yeru-Baala ndi banja lake mwazichita moona mtima ndiponso mokhulupirika, ndiye mukondwere ndi Abimeleki, nayenso akondwere nanu! 20Koma ngati sichoncho moto utuluke mwa Abimeleki ndi kupsereza anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndipo moto utulukenso mwa anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndi kupsereza Abimeleki!”

21Kenaka Yotamu anathawira ku Beeri nakakhala komweko chifukwa ankaopa Abimeleki mʼbale wake.

22Abimeleki atalamulira Israeli zaka zitatu, 23Mulungu anayika chidani pakati pa Abimelekiyo ndi anthu a ku Sekemu, motero kuti anthu a ku Sekemu anawukira Abimeleki. 24Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo. 25Choncho anthu a ku Sekemu anayika anthu omubisalira pamwamba pa mapiri. Tsono iwo ankalanda anthu odutsa mʼnjira imeneyo zinthu zawo ndipo Abimeleki anamva zimenezi.

26Gaali mwana wa Ebedi anasamukira ku Sekemu ndi abale ake, ndipo anthu a ku Sekemuko anamukhulupirira iye. 27Anthuwo anapita ku munda kukathyola mphesa ndi kuzifinya, ndipo anachita chikondwerero mʼnyumba ya milungu yawo. Anthuwo akudya ndi kumwa, ankatemberera Abimeleki. 28Ndipo Gaali mwana wa Ebedi anati “Kodi Abimeleki ndi ndani, ndipo nʼchifukwa chiyani akutilamulira ife Asekemu? Kodi iyeyu si mwana wa Yeru-Baala ndipo womuthandiza wake si Zebuli? Tiyeni titumikire anthu a ku Hamori, kholo la fuko la Sekemu! Nanga nʼchifukwa chiyani tikutumikira Abimeleki? 29Anthu a mu mzindawo akanakhala pansi pa ulamuliro wanga, ndikanamuchotsa Abimelekiyu. Ndikanamuwuza Abimeleki kuti, ‘Wonjeza ankhondo ako ndipo ubwere tidzamenyane!’ ”

30Zebuli amene ankalamulira mzindawo atamva zimene Gaali mwana wa Ebadi ananena, anakwiya kwambiri. 31Anatumiza amithenga kwa Abimeleki, kukanena kuti, “Gaali mwana wa Ebedi ndi abale ake abwera ku Sekemu ndipo akuwutsa mitima ya anthu a mu mzindawo kuti akuwukireni inu. 32Nʼchifukwa chake usiku womwe uno inu ndi anthu anu mupite, mukabisale mʼminda. 33Mmawa dzuwa likutuluka, mudzuke ndi kukathira nkhondo mzindawo. Gaali ndi anthu amene ali naye akamadzabwera kuti alimbane ndi inu, inu mudzathane nawo monga mmene mungachitire.”

34Choncho Abimeleki ndi ankhondo ake onse anadzuka usiku nakabisalira mzinda wa Sekemu mʼmagulu anayi. 35Gaali mwana wa Ebedi anatuluka nakayima pa khomo pa chipata cha mzinda pamene Abimeleki ndi ankhondo ake anatuluka ku malo kumene anabisala kuja.

36Gaaliyo atawaona, anawuza Zebuli kuti, “Taona anthu akutsika kuchoka pamwamba pa mapiri.”

Koma Zebuli anayankha kuti, “Zimene mukuonazo ndi zithunzi za mapiri chabe osati anthu.”

37Koma Gaaliyo anayankhulanso kuti, “Taona anthu akutsika kuchokera pakati pa phiri, ndipo gulu lina likubwera kuchokera ku mtengo wa thundu wa owombeza mawula.”

38Ndipo Zebuli anamufunsa iye kuti, “Pakamwa pako paja pali kuti tsopano, iwe amene umanena kuti, Abimeleki ndaninso kuti ife timutumikire? Kodi amenewa si anthu aja umawanyozawa? Tsopano tuluka ukamenyane nawo.”

39Choncho Gaaliyo anatuluka akutsogolera anthu a ku Sekemu kukamenyana ndi Abimeleki. 40Koma Abimeleki anamuthamangitsa ndipo Gaala anathawa. Ambiri a ankhondo ake anagwa napwetekeka njira yonse mpaka ku chipata cha mzinda. 41Abimeleki anakhala ku Aruma, ndipo Zebuli anathamangitsa Gaali pamodzi ndi abale ake, kuwatulutsa mu Sekemu.

42Mmawa mwake anthu a ku Sekemu anapangana zopita ku minda, ndipo Abimeleki anamva zimenezi. 43Tsono Abimeleki anatenga anthu ake, nawagawa magulu atatu ndi kukabisala mʼminda. Ataona anthu akutuluka mu mzindawo, iye anapita kukalimbana nawo ndipo onsewo anawapha. 44Abimeleki pamodzi ndi magulu ake anathamangira kutsogolo nakawakhalira pa chipata cha mzinda. Ndipo magulu awiri ena aja anathamangira anthu amene anali mʼminda ndi kuwapha onse. 45Abimeleki anawuthira nkhondo mzindawo tsiku lonse. Kenaka anawulanda ndi kupha nzika zonse za mu mzindamo. Anawuwonongeratu mzindawo nawuwaza mchere.

46Anthu a mu nsanja ya Sekemu atamva zimenezi, anakalowa mu linga la nyumba yopembedzeramo Baala-Beriti. 47Abimeleki anamva kuti anthu ena asonkhana kumeneko. 48Choncho Abimeleki pamodzi ndi anthu ake onse anapita ku phiri la Zalimoni. Kumeneko anatenga nkhwangwa nadula nthambi za mitengo. Ananyamula nthambi zija pa phewa pake. Tsono anawuza anthu aja kuti, “Zimene mwaona ine ndikuchita, inunso mufulumire kuchita monga ndachitiramu.” 49Tsono aliyense anadula nthambi zake, natsatira Abimeleki. Anakawunjika nthambi zija pa linga paja, kenaka ndi kuliyatsa moto. Choncho anthu onse a ku nsanja ya Sekemu anafa. Analipo anthu pafupifupi 1,000, amuna ndi akazi.

50Kenaka Abimeleki anapita ku Tebezi. Anakawuzungulira mzindawo ndi kuwulanda. 51Koma mu mzindamo munali nsanja yolimba. Anthu onse a mu mzindamo amuna ndi akazi anathawira mu nsanjayo, nadzitsekera mʼkati. Ndipo anakwera ku denga la nsanjayo. 52Abimeleki anapita ku nsanjayo nathira nkhondo. Anafika pafupi ndi chitseko cha nsanja ija kuti ayitenthe. 53Koma mkazi wina anaponya mwala wa mphero pa mutu wa Abimeleki ndi kuswa chibade cha mutuwo.

54Mwamsanga Abimeleki anayitana mnyamata womunyamulira zida za nkhondo namuwuza kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuti anthu asadzanene kuti, ‘Mkazi ndiye anamupha.’ ” Choncho wantchito wake anamubayadi mpaka kutulukira kunja lupangalo ndipo anafa. 55Aisraeli ataona kuti Abimeleki wafa, anapita kwawo.

56Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja. 57Mulungu anawalanganso anthu a ku Sekemu chifukwa cha kuyipa kwawo konse. Ndipo matemberero a Yotamu mwana wa Yeru-Baala anawagweradi.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Судьи 9:1-57

Абималик

1Абималик, сын Иеруб-Баала, пришёл к братьям своей матери в Шахем и сказал им и всему клану своей матери:

2– Спросите всех жителей Шахема: «Что для вас лучше, чтобы вами правили все семьдесят сыновей Иеруб-Баала или всего лишь один?» Помните, что я ваша плоть и кровь.

3Когда братья его матери пересказали всё это жителям Шахема, те склонились на сторону Абималика, потому что говорили: «Он наш брат». 4Они дали ему восемьсот сорок граммов9:4 Букв.: «семьдесят шекелей». серебра из храма Баал-Берита, и Абималик нанял на них праздных и безрассудных людей, которые пошли за ним. 5Он пришёл в дом своего отца в Офре и убил семьдесят своих братьев, сыновей Иеруб-Баала, на одном камне. Но Иотам, самый младший сын Иеруб-Баала, спрятался и спасся. 6А все жители Шахема и Бет-Милло собрались у великого дерева в Шахеме и сделали Абималика царём.

7Когда об этом рассказали Иотаму, он поднялся на вершину горы Геризим и закричал им:

– Послушайте меня, жители Шахема, чтобы и Всевышний послушал вас! 8Решили однажды деревья поставить над собою царя. Они сказали оливе: «Царствуй над нами». 9Но олива ответила: «Бросить ли мне своё масло – им славят богов и людей, – чтобы править деревьями?» 10Деревья сказали инжиру: «Ты приди, царствуй над нами». 11Но инжир им ответил: «Бросить ли мне свой плод – такой хороший и вкусный, – чтобы править деревьями?» 12Деревья сказали виноградной лозе: «Ты приди, царствуй над нами». 13Но лоза им ответила: «Бросить ли мне своё вино – оно веселит богов и людей, – чтобы править деревьями?» 14Тогда деревья сказали терновнику: «Ты приди, царствуй над нами». 15И терновник ответил деревьям: «Если вы и вправду хотите поставить меня над собою царём, то приходите, покойтесь в моей тени. Но если нет, то пусть выйдет из терновника пламя и пожрёт ливанские кедры».

16Итак, честно ли и достойно ли вы поступили, сделав Абималика царём? По совести ли вы поступили с Иеруб-Баалом и его семьёй, так ли обошлись с ним, как он того заслуживает? 17Мой отец сражался за вас, рисковал жизнью, чтобы избавить вас от руки мадианитян, 18но сегодня вы восстали против семьи моего отца, убили семьдесят его сыновей на одном камне и сделали Абималика, сына его рабыни, царём над жителями Шахема, потому что он ваш брат. 19Если сегодня вы поступили с Иеруб-Баалом и его семьёй честно и достойно, то радуйтесь за Абималика, и пусть он радуется за вас! 20Но если нет, то пусть из Абималика выйдет пламя и пожрёт вас, жители Шахема и Бет-Милло, и пусть из вас, жители Шахема и Бет-Милло, выйдет пламя и пожрёт Абималика!

21И Иотам бежал и поселился в городе Беэре, потому что боялся своего брата Абималика.

22Абималик правил Исроилом три года. 23Но Всевышний наслал злого духа между Абималиком и жителями Шахема, и жители Шахема не стали покоряться Абималику. 24Это случилось, чтобы жестокость по отношению к семидесяти сыновьям Иеруб-Баала была наказана, и кровь их легла на их брата Абималика и на жителей Шахема, которые помогли ему убить своих братьев. 25Жители Шахема из вражды к нему устраивали засады на горных вершинах, чтобы грабить каждого, кто проходит мимо, и об этом было донесено Абималику.

26А в Шахем пришёл Гаал, сын Эведа, вместе со своими братьями, и жители Шахема доверились ему. 27Они вышли в поле, собирали виноград, давили его и праздновали. Они пошли в храм своего бога, ели и пили и проклинали Абималика.

28Гаал, сын Эведа, сказал:

– Кто такой Абималик и кто такие мы в Шахеме, чтобы подчиняться ему? Разве он не сын Иеруб-Баала и разве не Зевул его наместник? Служите людям Еммора, отца Шахема! Зачем нам служить Абималику? 29Если бы только эти люди были у меня под началом! Тогда я избавился бы от Абималика. Я бы сказал ему: «Собери своё войско и выходи!»

30Когда Зевул, правитель города, услышал слова Гаала, сына Эведа, он очень разгневался. 31Он тайно послал вестников к Абималику, чтобы сказать ему:

– Гаал, сын Эведа, и его братья пришли в Шахем и настраивают город против тебя. 32Итак, приходи ночью со своими воинами и устрой в поле засаду. 33А утром, на рассвете, напади на город. Когда Гаал и его воины выйдут против тебя, делай с ними всё, что хочешь.

34И Абималик вместе со всеми своими воинами отправился в путь, и они залегли в засаду у Шахема четырьмя отрядами. 35А Гаал, сын Эведа, вышел и стоял у входа в городские ворота как раз тогда, когда Абималик и его воины выходили из засады.

36Увидев их, Гаал сказал Зевулу:

– Смотри, с горных вершин спускаются люди!

Зевул ответил:

– Тени от гор кажутся тебе людьми.

37Но Гаал вновь сказал:

– Смотри, с горы9:37 Букв.: «Табур-Эрец», что переводится как «пуп земли». Возможно, это была гора Геризим. спускаются люди, и один отряд идёт со стороны дуба прорицателей9:37 Или: «из Елон-Меоненина»..

38Зевул сказал ему:

– Где твоя похвальба, ты, говоривший: «Кто такой Абималик, чтобы нам ему подчиняться?» Разве не этих людей ты высмеивал? Выходи же теперь и сразись с ними!

39И Гаал пошёл во главе жителей Шахема и сразился с Абималиком. 40Абималик погнался за ним, и Гаал побежал от него. Многие пали ранеными у самого входа в ворота. 41И Абималик расположился в Аруме, а Зевул выгнал Гаала и его братьев из Шахема.

42На следующий день жители Шахема вышли в поле, и об этом донесли Абималику. 43Он взял своих воинов, разделил их на три отряда и устроил в поле засаду. Увидев людей, которые выходили из города, он поднялся и напал на них. 44Абималик и отряд, который был с ним, поспешили занять место у входа в городские ворота, а два отряда ринулись на тех, кто был в поле, и стали убивать их. 45Весь день Абималик воевал с городом, пока не взял его и не перебил его жителей. После этого он сровнял город с землёй и засыпал это место солью.

46Услышав об этом, все жители, бывшие в Шахемской башне, вошли в убежище храма Баал-Берита9:46 Букв.: «Ил-Берит» – другое название Баал-Берита (см. ст. 4).. 47Когда Абималику донесли, что они собрались там, 48он вместе со всеми своими воинами поднялся на гору Цалмон. Он взял топор, срубил несколько веток и положил их на плечи. Затем он приказал воинам, которые были с ним:

– Быстро делайте то же, что и я.

49И все его воины нарубили веток и пошли за Абималиком. Они сложили их у убежища и подожгли его вместе с теми, кто в нём был. И все, кто был в Шахемской башне, около тысячи мужчин и женщин погибли.

50Затем Абималик пошёл к Тевецу, осадил его и захватил. 51Но в городе была крепкая башня, и туда бежали все мужчины и женщины – все жители города. Они заперлись изнутри и поднялись на крышу башни. 52Абималик пришёл к башне и напал на неё, но когда он приблизился к входу, чтобы поджечь её, 53одна женщина сбросила ему на голову обломок жёрнова и проломила ему череп.

54Он тотчас же подозвал своего оруженосца и сказал ему:

– Вытащи меч и убей меня, чтобы не говорили обо мне: «Его убила женщина».

Слуга пронзил его, и он умер. 55Увидев, что Абималик умер, исроильтяне разошлись по домам.

56Так Всевышний воздал за зло, которое Абималик сделал своему отцу, убив семьдесят своих братьев. 57Ещё Всевышний воздал за всё их зло жителям Шахема. Их постигло проклятие Иотама, сына Иеруб-Баала.