Oweruza 8 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 8:1-35

Zeba ndi Zalimuna

1Aefereimu anafunsa Gideoni kuti, “Nʼchifukwa chiyani watichita zimenezi? Bwanji sunatiyitane pamene umakamenyana ndi Amidiyani?” Iwo anamudzudzula kwambiri.

2Koma iye anawayankha kuti, “Nʼchiyani ndachita kuyerekeza ndi zimene mwachita inu? Kodi zimene mwachita inu Aefereimu si zazikulu kuposa zimene fuko langa la Abiezeri lachita? 3Mulungu wapereka mafumu a Midiyani, Orebu ndi Zeebu mʼmanja mwanu. Ndachita chiyani kuyerekeza ndi zimene mwachita inu?” Atanena izi, anthuwo mitima yawo inatsika.

4Gideoni anafika ndi kuwoloka mtsinje wa Yorodani pamodzi ndi anthu 300 amene anali naye. Ngakhale kuti anali otopa anapirikitsabe adani awo. 5Atafika ku Sukoti anapempha anthu a kumeneko kuti, “Chonde apatseniko buledi ankhondo angawa pakuti atopa. Koma ine ndikupirikitsa Zeba ndi Zalimuna, mafumu a Midiyani.”

6Koma atsogoleri a Sukoti anayankha kuti, “Kodi Zeba ndi Zalimuna mwawagonjetsa kale kuti tipatse buledi ankhondo akowa?”

7Gideoni anayankha kuti, “Mwatero! Yehova akapereka Zeba ndi Zalimuna mʼdzanja langa, ndidzakukwapulani ndi matsatsa a minga ya mʼchipululu.”

8Atachoka pamenepo anapita ku Penueli ndipo anapemphanso buledi kwa anthu a kumeneko, koma iwo anamuyankha monga anayankhira anthu a ku Sukoti aja. 9Gideoni anawawuzanso kuti, “Ndikamadzabwerera nditawagonjetsa, ndidzagwetsa nsanja iyi.”

10Nthawi iyi nʼkuti Zeba ndi Zalimuna ali ku Karikori ndi ankhondo pafupifupi 15,000. Amenewa ndiwo anatsalako mwa ankhondo a anthu akummawa; pakuti anafa ankhondo 120,000. 11Gideoni anadzera njira ya anthu a matenti kummawa kwa Noba ndi Yogibeha ndipo anawathira nkhondo popeza ankhondo awo anali osakonzekera. 12Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri a Amidiyani anathawa koma Gideoni anawathamangitsa mpaka kuwagwira. Koma ankhondo awo onse anathawa ndi mantha.

13Ndipo Gideoni mwana wa Yowasi, pobwera kuchokera ku nkhondo anadzera njira ya ku chikweza cha Heresi. 14Kumeneko iye anagwira mnyamata wa ku Sukoti ndipo atamufunsa, mnyamatayo anamulembera mayina a akuluakulu ndi atsogoleri 77 a ku Sukoti. 15Kenaka Gideoni anabwera kwa anthu a ku Sukoti ndi kunena kuti, “Awa ndi Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri munkandinena nawo aja kuti, ‘Kodi Zeba ndi Zalimuna wawagonjetsa kale mmene ukuti tiwapatse buledi anthu ako otopawa?’ ” 16Tsono Gideoni anatenga akuluakulu a mu mzindawo ndipo anagwira matsatsa a minga za mʼchipululu ndi kuwakwapula nawo. 17Anagwetsa nsanja ya ku Penueli ndi kupha amuna onse a mu mzindawo.

18Kenaka anafunsa Zeba ndi Zalimuna kuti, “Kodi anthu a ku Tabori amene munawapha aja anali a maonekedwe otani?” Iwo anayankha kuti, “Anali anthu a maonekedwe ngati inu. Aliyense ankaoneka ngati mwana wa mfumu?”

Iwo anayankha kuti, “Anthu ngati inu, aliyense wooneka ngati mwana wa mfumu.”

19Ndipo Gideoni anayankha kuti, “Ndikulumbira pa Mulungu, mukanapanda kuwapha nanenso sindikanakuphani. Ndi abale anga amenewo, ana a amayi anga enieni.” 20Tsono anawuza Yetero, mwana wake wachisamba kuti, “Tiye, ipha anthu amenewa!” Koma chifukwa Yeteri anali wamngʼono sanasolole lupanga lake, popeza anachita mantha.

21Tsono Zeba ndi Zalimuna anawuza Gideoni kuti, “Bwera utiphe ndiwe chifukwa uli ndi mphamvu za munthu wamkulu.” Choncho Gideoni anapita nawapha natenganso zokongoletsera zimene zinali pa makosi a ngamira zawo.

Efodi ya Gideoni

22Aisraeli anati kwa Gideoni, “Inu muzitilamulira, mwana wanu ndi zidzukulu zanu, chifukwa mwatipulumutsa mʼmanja mwa Amidiyani.”

23Koma Gideoni anawawuza kuti, “Sindidzakulamulirani, mwana wanganso sadzakulamulirani. Koma Yehova ndiye adzakulamulirani.” 24Gideoni anatinso, “Ine ndikupemphani chinthu chimodzi. Aliyense wa inu andipatse ndolo zomwe anafunkha ku nkhondo.” (Adani aja anali ndi ndolo zagolide popeza anali Aismaeli).

25Iwo anayankha kuti, “Ife tikupatsani ndithu ndolozi.” Choncho anayala chinsalu, ndipo aliyense anaponyapo ndolo zimene anafunkha. 26Tsono kulemera kwa ndolo zagolide zimene anapereka kunali makilogalamu makumi awiri, osawerengera kulemera kwa mphande, mkanda wamʼkhosi, zovala zapepo za mafumu a Midiyani ndiponso malamba azitsulo za mʼmakosi a ngamira zawo. 27Gideoni anagwiritsa ntchito golide uja kupanga efodi, ndipo anakamuyika ku mzinda wake ku Ofura. Tsono Aisraeli onse anasiya kupembedza Yehova nayamba kupembedza efodiyo kumeneko. Ichi chinasanduka msampha kwa Gideoni ndi banja lake lonse.

Imfa ya Gideoni

28Choncho Amidiyani anagonjetsedwa ndi Aisraeli ndipo sanayeserenso kuwawukira. Ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 40 pamene Gideoni anali ndi moyo.

29Yeru-Baala mwana wa Yowasi anapita kukakhala kwawo. 30Ana a Gideoni anali 70 popeza anali ndi akazi ambiri. 31Mdzakazi wake amene anali ku Sekemu, anabereka naye mwana wamwamuna, amene anamutcha Abimeleki. 32Gideoni mwana wa Yowasi anamwalira atakalamba ndipo anayikidwa mʼmanda a abambo ake, Yowasi ku Ofura mzinda wa Mwabiezeri.

33Atangomwalira Gideoni, Aisraeli anayambanso kupembedza Abaala. Iwo anasandutsa Baala-Beriti kukhala mulungu wawo. 34Aisraeli sanakumbukirenso Yehova Mulungu wawo amene anawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo mbali zonse. 35Ndiponso sanachite zinthu zokomera banja la Yeru-Baala (ndiye kuti Gideoni) chifukwa cha zabwino zonse zimene iye anawachitira.

Bibelen på hverdagsdansk

Dommerbogen 8:1-35

1De efraimitiske ledere var imidlertid utilfredse og rettede en skarp kritik mod Gideon. „Hvorfor ventede du med at sende bud efter os, til midjanitterne var besejret?” spurgte de.

2Gideon svarede: „Den smule, jeg og min klan har gjort, er ikke noget i sammenligning med jeres heltedåd! 3Lod Gud jer ikke fange de to midjanitiske hærførere Oreb og Ze’eb? Hvad I opnåede mod slagets afslutning, har langt større betydning, end hvad vi foretog os i begyndelsen.” Da efraimitterne hørte det, var de ikke vrede længere.

4Derpå satte Gideon over Jordanfloden med sine 300 mand, som ikke havde opgivet at forfølge fjenden, selv om de var trætte og udmattede. 5Da de nåede Sukkot, sagde Gideon til byens ledere: „Giv venligst mine krigere noget at spise. Vi er udmattede af at jagte midjanitterkongerne Zeba og Salmunna.”

6Men byens ledere svarede: „Fang først Zeba og Salmunna. Så skal vi nok give jer noget at spise.”

7Da sagde Gideon: „Når Herren har udleveret Zeba og Salmunna til mig, vender jeg tilbage og slår jer alle sammen med ørkentjørne og tidsler.” 8Så fortsatte de videre til Penuel, men der gav man samme svar som i Sukkot, 9hvorpå Gideon sagde til dem: „Når vi har sejret, vender vi tilbage og river jeres vagttårn ned.”

10I mellemtiden var Zeba og Salmunna nået frem til Karkor med de 15.000 mand, der var tilbage af den forenede hær fra øst. 120.000 var faldet for sværdet. 11Men Gideon gik en omvej forbi teltlejrene øst for Noba og Jogbeha og overfaldt de intetanende midjanitter. 12De to konger flygtede, men Gideon fulgte efter dem og fangede dem, og hele deres hær blev grebet af rædsel.

13Derefter vendte Gideon tilbage gennem Herespasset. 14Dér tog han en ung mand fra Sukkot til fange og tvang ham til at skrive navnene ned på alle byens 77 ledere. 15Så gik Gideon til Sukkot og sagde til mændene i byen:

„Her er de to konger Zeba og Salmunna. I husker vist godt, at I sagde: Fang først Zeba og Salmunna. Så skal vi nok give jer noget at spise.”

16Så tog han de 77 ledere til fange og pryglede dem til døde med ørkentjørne og tidsler. 17Bagefter drog han til Penuel, hvor han rev byens vagttårn ned og dræbte samtlige mandlige indbyggere.

18Derpå spurgte han Zeba og Salmunna: „Hvordan så de mænd ud, som I dræbte ved Tabor?”

„De lignede dig, og de så begge to ud som kongesønner,” svarede de.

19„Så var det mine egne brødre!” udbrød Gideon. „Jeg sværger, at hvis I havde skånet dem, ville jeg have skånet jer.” 20Så sagde han til sin ældste søn Jeter: „Kom her hen og hug de to konger ned!” Men Jeter, der endnu kun var en stor dreng, havde ikke mod til det.

21„Gør det selv, Gideon,” sagde Zeba og Salmunna. „Det er ikke noget for et barn.” Så huggede Gideon dem ned og tog de kostbare ornamenter, som deres kameler havde om halsen.

Gideon afslår at blive konge

22Nu sagde israelitterne til Gideon: „Du og dine efterkommere skal regere over os, for du har reddet os fra midjanitterne!” 23Men Gideon svarede: „Hverken jeg eller min søn skal regere over jer. Herren skal være jeres Konge!” 24Så tilføjede han: „En enkelt ting vil jeg dog bede jer om: at I alle sammen giver mig en ørering fra jeres krigsbytte.” Midjanitterne gik nemlig med guldringe i ørerne, for de var dygtige handelsfolk.8,24 Ordret: „Ishmaelitter”, men det er her sikkert en titel på ørkenens handelsfolk.

25„Gerne,” svarede de og bredte et klæde ud på jorden, hvor de hver især lagde en ring fra deres krigsbytte. 26Vægten af ringene alene beløb sig til næsten 20 kilo.8,26 På hebraisk: 1700 shekel. 1 shekel = ca. 11,5 g. Dertil kom de kostbare kamelornamenter, andre smykker, kongernes purpurfarvede dragter og de kæder, som kamelerne havde haft om halsen. 27Af disse kostbarheder lavede Gideon en efod, som han anbragte i sin hjemby Ofra. Men israelitterne begyndte at tilbede efoden, som derfor blev årsag til fald for Gideon og hans familie.

28Midjanitterne var nu besejret og udgjorde ikke længere nogen trussel for Israel. De næste 40 år var der fred i landet, så længe Gideon levede.

29-30Efter sejren vendte Gideon tilbage til sin hjemegn, hvor han siden boede og fik 70 sønner, for han havde mange koner. 31Han fik også en søn med en slavepige fra Sikem, og han kom til at hedde Abimelek. 32Gideon døde som en meget gammel mand og blev begravet i familiegravstedet i Ofra, hvor Abiezers slægt kom fra.

33Kort efter Gideons død begyndte israelitterne igen at dyrke kana’anæernes afguder. De gjorde Ba’al-Berit til deres gud 34og glemte Herren, der havde frelst dem fra deres fjendtlige nabofolk. 35De viste heller ingen respekt for Gideons familie, på trods af hvad Gideon havde betydet for landet.