Oweruza 5 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 5:1-31

Nyimbo ya Debora

1“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:

2“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli;

ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu,

tamandani Yehova:

3“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu!

Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova,

Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.

4“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri,

pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu,

dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka

nigwetsa madzi.

5Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova,

Mulungu wa Israeli.

6“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati,

pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa;

alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.

7Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi

mpaka pamene iwe Debora unafika;

unafika ngati mayi ku Israeli.

8Pamene anasankha milungu ina,

nkhondo inabwera ku zipata za mzinda,

ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke

pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.

9Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli,

uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu.

Tamandani Yehova!

10“Inu okwera pa abulu oyera,

okhala pa zishalo,

ndi inu oyenda pa msewu,

yankhulani. 11Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta;

kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana;

akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli.

“Choncho anthu a Yehova

anasonkhana ku zipata za mzinda.

12Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera;

tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo.

Iwe Baraki! nyamuka

Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’

13“Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo;

anthu a Yehova anapita

kukamenyera Yehova nkhondo

kulimbana ndi adani amphamvu.

14Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu;

akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako.

Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri,

ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.

15Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora;

inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki,

ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira.

Koma pakati pa mafuko a Rubeni

panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.

16Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera

zitoliro zoyitanira nkhosa?

Pakati pa anthu a fuko la Rubeni

panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.

17Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani.

Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi?

Aseri anali pa gombe la Nyanja;

anangokhala mʼmadooko mwawo.

18Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa.

Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.

19“Mafumu anabwera, anachita nkhondo;

mafumu Akanaani anachita nkhondo

ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido,

koma sanatengeko zofunkha zasiliva.

20Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo,

zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.

21Mtsinje wa Kisoni unawakokolola,

chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola.

Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!

22Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu,

akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.

23Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’

‘Tembererani nzika zake mwaukali,

chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova,

kulimbana ndi adani ake amphamvu.’

24“Akhale wodala kupambana akazi onse,

Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni;

inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.

25Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka;

anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.

26Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake,

anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja.

Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake,

ndi kumubowola mu litsipa mwake.

27Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa,

anagwa; iye anagona pamenepo.

Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa;

pamene anagwera, pamenepo anaferapo.

28“Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera;

nafuwula mokweza kuti,

‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika?

Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’

29Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha,

ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,

30‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane;

akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri.

Sisera akumupatsa zofunkha:

zovala zonyikidwa mu utoto,

zoti ndizivala mʼkhosi

zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’

31“Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke,

koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa

pamene lituluka ndi mphamvu zake.”

Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.

Thai New Contemporary Bible

ผู้วินิจฉัย 5:1-31

บทเพลงของเดโบราห์

1ในวันนั้นเดโบราห์กับบาราคบุตรอาบีโนอัมร้องเพลงบทนี้ว่า

2“สรรเสริญองค์พระผู้เป็นเจ้า!

เมื่อเหล่าเจ้านายในอิสราเอลนำหน้า

เมื่อเหล่าประชากรเต็มใจอุทิศตน

3“ฟังเถิด กษัตริย์ทั้งหลาย! ฟังเถิด บรรดาเจ้านาย!

ข้าพเจ้าจะร้องเพลงสดุดีแด่5:3 หรือขององค์พระผู้เป็นเจ้าข้าพเจ้าจะขับร้อง

จะบรรเลงเพลงถวาย5:3 หรือข้าพเจ้าจะร้องเพลงสรรเสริญถวายแด่พระยาห์เวห์พระเจ้าแห่งอิสราเอล

4“ข้าแต่องค์พระผู้เป็นเจ้าเมื่อพระองค์เสด็จออกมาจากเสอีร์

เมื่อทรงยาตราจากดินแดนเอโดม

โลกก็สั่นสะท้าน ท้องฟ้าหลั่งริน

เมฆเทฝนลงมา

5ภูเขาสะเทือนเลื่อนลั่นต่อหน้าองค์พระผู้เป็นเจ้า

แม้แต่ภูเขาซีนายก็สั่นคลอนต่อหน้าพระยาห์เวห์พระเจ้าแห่งอิสราเอล

6“ในยุคของชัมการ์บุตรอานาท

ในสมัยของยาเอลถนนหนทางถูกทิ้งร้าง

ผู้สัญจรไปมาใช้เส้นทางคดเคี้ยว

7วิถีชาวบ้าน5:7 หรือนักรบในอิสราเอลก็หยุดลง

หยุดจนกระทั่งข้าพเจ้า5:7 หรือท่านเดโบราห์ขึ้นมา

ดั่งมารดาคนหนึ่งของอิสราเอล

8เมื่อพวกเขาเลือกพระอื่นๆ

สงครามก็มาประชิดประตูเมือง

และไม่มีโล่ไม่มีหอกให้เห็นเลย

ท่ามกลางชายฉกรรจ์สี่หมื่นคนในอิสราเอล

9จิตใจของข้าพเจ้าชื่นชมบรรดาเจ้านายของอิสราเอล

และเหล่าอาสาสมัครในหมู่ประชาชน

สรรเสริญองค์พระผู้เป็นเจ้า!

10“ท่านผู้ขี่ลาสีขาว

นั่งอยู่บนอานพรม

และท่านผู้เดินตามถนน

จงใคร่ครวญ 11เสียงของเหล่านักร้อง5:11 หรือนักธนูในภาษาฮีบรูคำนี้มีความหมายไม่ชัดเจนที่แหล่งน้ำ

เขาเล่าขานถึงพระราชกิจอันชอบธรรมขององค์พระผู้เป็นเจ้า

ถึงพันธกิจอันชอบธรรมของนักรบ5:11 หรือชาวบ้านของพระองค์ในอิสราเอล

“แล้วชนชาติขององค์พระผู้เป็นเจ้า

ลงมาที่ประตูเมือง

12‘ตื่นเถิดเดโบราห์เอ๋ย ตื่นขึ้นเถิด!

ตื่นเถิด ตื่นขึ้น เปล่งเสียงร้องเพลง!

บาราคเอ๋ย ลุกขึ้นเถิด!

บุตรแห่งอาบีโนอัมเอ๋ย จงนำเชลยของท่านไป’

13“ครั้งนั้นบรรดาผู้ที่เหลืออยู่

ลงมาต่อสู้เหล่าเจ้านาย

ประชากรขององค์พระผู้เป็นเจ้า

มาร่วมกับข้าพเจ้าต่อสู้ผู้เกรียงไกร

14บางคนมาจากเอฟราอิมซึ่งเคยเป็นดินแดนของชาวอามาเลข

เบนยามินอยู่กับเหล่าประชากรที่ติดตามท่าน

เหล่าแม่ทัพลงมาจากมาคีร์

บรรดาผู้ถือคทาของแม่ทัพมาจากเศบูลุน

15เจ้านายแห่งอิสสาคาร์ไปกับเดโบราห์

อิสสาคาร์สมทบกับบาราค

เร่งรุดติดตามเขาเข้าสู่หุบเขา

แต่ในแว่นแคว้นแห่งรูเบน

พากันใคร่ครวญอย่างหนัก

16ทำไมท่านจึงพำนักอยู่รอบกองไฟ5:16 หรือถุงสัมภาระ

เพื่อฟังเสียงผิวปากเรียกฝูงแกะ?

แต่ในแว่นแคว้นแห่งรูเบน

พากันใคร่ครวญอย่างหนัก

17กิเลอาดอยู่ฟากข้างโน้นของแม่น้ำจอร์แดน

และดานทำไมยังมัวอ้อยอิ่งอยู่ข้างๆ เรือ?

อาเชอร์เอ้อระเหยอยู่ที่ชายฝั่ง

นั่งเฉยอยู่ริมทะเล

18ประชากรของเศบูลุนเสี่ยงชีวิตของตน

นัฟทาลีก็อยู่ในสมรภูมิ5:18 ภาษาฮีบรูว่าบนที่สูงแห่งท้องทุ่งเช่นเดียวกัน

19“เหล่ากษัตริย์มาสู้รบกัน

เหล่ากษัตริย์แห่งคานาอันได้สู้รบกัน

ที่ทาอานาค ใกล้ห้วงน้ำแห่งเมกิดโด

แต่ไม่ได้ริบเงินริบข้าวของใดๆ เลย

20ดวงดาวจากฟ้าสวรรค์

ออกจากวงโคจรมาต่อสู้สิเสรา

21แม่น้ำคีโชน แม่น้ำสายโบราณ

กวาดล้างพวกเขาออกไป

จิตวิญญาณของข้าพเจ้าเอ๋ย จงเดินหน้าต่อไป จงเข้มแข็งเถิด!

22และแล้วเสียงเกือกม้าก็ดังกระหึ่ม

ม้าศึกของเขาควบห้อออกไป

23ทูตขององค์พระผู้เป็นเจ้ากล่าวว่า ‘จงสาปแช่งเมโรส

สาปแช่งชาวเมืองนั้นอย่างหนัก

เพราะเขาไม่ได้มาช่วยองค์พระผู้เป็นเจ้า

ช่วยองค์พระผู้เป็นเจ้าต่อสู้ผู้เกรียงไกร’

24“หญิงผู้น่ายกย่องมากที่สุดคือยาเอล

ภรรยาของเฮเบอร์ชาวเคไนต์

เป็นผู้ที่น่าชมเชยที่สุดของบรรดาหญิงที่อาศัยอยู่ในเต็นท์

25เขาร้องขอน้ำ นางก็ให้น้ำนม

นางนำนมข้นใส่ชามที่ใช้กับเหล่าเจ้านายมาให้เขา

26นางเอื้อมมือหยิบหลักหมุดเต็นท์

มือขวาคว้าค้อนของช่างไม้

ตอกทะลุขมับของสิเสรา หัวเขาแหลกเหลว

นางตอกหลักหมุดทะลุขมับของเขา

27เขาทรุดลงที่เท้าของนาง

เขาล้มลงตรงที่เขานอนอยู่

เขาฟุบลงแทบเท้าของนาง

เขาล้มลงตายตรงนั้น

28“มารดาของสิเสรา

เฝ้ามองลอดลูกกรงหน้าต่างและร่ำร้องว่า

‘ทำไมรถรบของเขาจึงมาช้า?

ทำไมล้อของรถม้าศึกของเขาแล่นช้านัก?’

29ผู้ฉลาดที่สุดในหมู่สตรีของนางก็ตอบนาง

อันที่จริงนางเฝ้าบอกตัวเองว่า

30‘พวกเขายังหาและแบ่งของเชลยกันไม่เสร็จหรือไร?

แต่ละคนได้หญิงสาวหนึ่งคนบ้าง สองคนบ้าง

สิเสราริบได้เสื้อผ้า

ปักสีสดสวย

ผ้าพันคอปักลวดลายสำหรับฉัน

ทั้งหมดนี้เป็นของที่ริบมา’

31“ข้าแต่องค์พระผู้เป็นเจ้า! ขอให้ศัตรูทั้งปวงของพระองค์พินาศไปเช่นนั้น

แต่ขอให้บรรดาผู้ที่รักพระองค์เป็นเช่นดวงอาทิตย์

ที่โผล่ขึ้นด้วยพลัง”

แล้วแผ่นดินก็สงบสุขอยู่ตลอดสี่สิบปี