Oweruza 5 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 5:1-31

Nyimbo ya Debora

1“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:

2“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli;

ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu,

tamandani Yehova:

3“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu!

Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova,

Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.

4“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri,

pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu,

dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka

nigwetsa madzi.

5Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova,

Mulungu wa Israeli.

6“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati,

pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa;

alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.

7Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi

mpaka pamene iwe Debora unafika;

unafika ngati mayi ku Israeli.

8Pamene anasankha milungu ina,

nkhondo inabwera ku zipata za mzinda,

ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke

pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.

9Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli,

uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu.

Tamandani Yehova!

10“Inu okwera pa abulu oyera,

okhala pa zishalo,

ndi inu oyenda pa msewu,

yankhulani. 11Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta;

kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana;

akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli.

“Choncho anthu a Yehova

anasonkhana ku zipata za mzinda.

12Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera;

tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo.

Iwe Baraki! nyamuka

Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’

13“Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo;

anthu a Yehova anapita

kukamenyera Yehova nkhondo

kulimbana ndi adani amphamvu.

14Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu;

akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako.

Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri,

ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.

15Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora;

inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki,

ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira.

Koma pakati pa mafuko a Rubeni

panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.

16Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera

zitoliro zoyitanira nkhosa?

Pakati pa anthu a fuko la Rubeni

panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.

17Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani.

Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi?

Aseri anali pa gombe la Nyanja;

anangokhala mʼmadooko mwawo.

18Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa.

Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.

19“Mafumu anabwera, anachita nkhondo;

mafumu Akanaani anachita nkhondo

ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido,

koma sanatengeko zofunkha zasiliva.

20Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo,

zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.

21Mtsinje wa Kisoni unawakokolola,

chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola.

Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!

22Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu,

akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.

23Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’

‘Tembererani nzika zake mwaukali,

chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova,

kulimbana ndi adani ake amphamvu.’

24“Akhale wodala kupambana akazi onse,

Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni;

inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.

25Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka;

anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.

26Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake,

anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja.

Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake,

ndi kumubowola mu litsipa mwake.

27Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa,

anagwa; iye anagona pamenepo.

Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa;

pamene anagwera, pamenepo anaferapo.

28“Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera;

nafuwula mokweza kuti,

‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika?

Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’

29Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha,

ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,

30‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane;

akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri.

Sisera akumupatsa zofunkha:

zovala zonyikidwa mu utoto,

zoti ndizivala mʼkhosi

zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’

31“Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke,

koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa

pamene lituluka ndi mphamvu zake.”

Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

士师记 5:1-31

底波拉和巴拉之歌

1那一天,底波拉巴拉高唱凯歌:

2以色列的首领身先士卒,

民众前仆后继,

你们要赞美耶和华!

3君王和首领啊,请留心细听!

我要向耶和华歌唱,

我要歌颂以色列的上帝耶和华。

4耶和华啊,当你从西珥出来,

走过以东时,

大地震动,

天上降雨。

5西奈山的耶和华面前,

以色列的上帝耶和华面前,

群山震动。

6亚拿的儿子珊迦雅亿的时代,

大路行人绝迹,

旅客绕道而行。

7底波拉以色列之母以前,

以色列的乡村人烟稀少。

8以色列人选择新的神明,

便战祸临门,

四万以色列人中找不到一矛一盾。

9我的心追随以色列的首领,

追随民中踊跃出征的人。

你们要赞美耶和华!

10“你们骑白驴的、坐绣花毯子的、步行的,

都要倾听。

11歌乐手聚集在井旁,

传扬耶和华和祂以色列子民的胜利。

耶和华的子民都来到城门口。

12底波拉啊,来吧,来吧,

歌唱吧!

亚比挪庵的儿子巴拉啊,来吧,

带走你的战俘吧!

13幸存的以色列人响应他们的首领,

耶和华的子民为我攻击勇士。

14他们有些来自原属亚玛力人的以法莲

有些来自便雅悯

统领出自玛吉

将官出自西布伦

15以萨迦的首领与底波拉同往,

以萨迦人随巴拉同去,

众人一起冲进山谷,

吕便人却犹豫不决。

16吕便人为什么坐在羊圈中听悠悠笛声?

他们举棋不定。

17基列人留在约旦河对岸。

人为什么停留在船上?

亚设人在海岸静坐,

在港口逗留。

18西布伦人和拿弗他利人却拼死鏖战沙场。

19迦南诸王来战,

来到米吉多河边的他纳交战,

却没有掠走金银。

20星辰从天上、从它们的轨道攻击西西拉

21古老的基顺河冲走了敌人。

我的心啊,要奋勇向前!

22蹄声隆隆,

骏马疾驰!

23“耶和华的天使说,

‘要咒诅米罗斯

要重重地咒诅米罗斯的居民,

因为他们没有帮助耶和华,

没有帮助耶和华攻击强敌。’

24基尼希百的妻子雅亿是妇人中最有福的,

是住帐篷的妇人中最有福的。

25西西拉求水,

雅亿给他奶喝,

用珍贵的碗盛上奶酪。

26雅亿左手拿起橛子,

右手拿起工匠的锤子,

猛击西西拉

打碎了他的头,

刺透了他的太阳穴。

27西西拉屈身倒下,

死在她脚前,

一动不动地躺在那里。

28“他母亲凭窗远眺,

隔着窗棂喊道,

‘为什么他的战车迟迟不回?

为什么还听不到车轮声?’

29聪明的宫女安慰她,

她却依然自言自语,

30‘莫非他们在搜索、瓜分战利品?

也许每人得到一两个少女,

西西拉也会分得从俘虏身上夺来的绣花彩巾。’

31耶和华啊,

愿你的敌人都像西西拉一样灭亡!

愿爱你的人如升起的太阳,

光辉熠熠!”

此后,以色列安享太平四十年。