Oweruza 21 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 21:1-25

Akazi a Abenjamini

1Aisraeli anali atalumbira ku Mizipa kuti, “Palibe mmodzi wa ife adzapereke mwana wake wamkazi kuti akwatiwe ndi mwamuna wa fuko la Benjamini.”

2Anthu anapita ku Beteli kumene anakakhala pansi pamaso pa Mulungu mpaka madzulo. Iwo anakweza mawu nalira kwambiri. 3Iwo ankanena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli, nʼchifukwa chiyani izi zachitika mʼdziko la Israeli kuti lero fuko limodzi lisowe mu Israeli?”

4Mmawa mwake anthu anadzuka namanga guwa lansembe ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano.

5Kenaka Aisraeli anafunsa kuti, “Kodi ndani pakati pa mafuko a Israeli sanafike ku msonkhano wa Yehova?” Anatero chifukwa anachita malumbiro aakulu okhudza munthu amene alephere kupita ku Mizipa ndi kuti woteroyo ayenera kuphedwa.

6Tsono Aisraeli anamva chisoni chifukwa cha abale awo, Abenjamini. Iwo anati, “Lero fuko limodzi lachotsedwa mu Israeli. 7Kodi tingawapezere bwanji anthu otsalawa akazi woti awakwatire? Paja ife tinalumbira kwa Yehova kuti sitidzapereka ana anthu aakazi kuti awakwatire. 8Kenaka anafunsa kuti, ‘Kodi mu fuko la Israeli ndani amene sanabwere pamaso pa Yehova ku Mizipa?’ ” Tsono panapezeka kuti panalibe ndi mmodzi yemwe wochokera ku Yabesi Giliyadi amene anapita ku msonkhano ku misasa kuja. 9Pamene anthu anawerengana anangoona kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi palibe.

10Choncho msonkhano unatumiza anthu ankhondo 12,000 ndi kuwalamula kuti, “Mukaphe anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi, kuphatikizapo akazi ndi ana.” 11Izi ndi zimene mukachite. “Mukaphe mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense amene anadziwapo mwamuna.” 12Iwo anapeza atsikana 400 pakati pa anthu okhala mu Yabesi Giliyadi amene anali asanadziwepo mwamuna ndipo anabwera nawo ku misasa ku Silo mʼdziko la Kanaani.

13Kenaka msonkhano wonse unatumiza uthenga kwa Abenjamini amene ankakhala ku thanthwe la Rimoni kuwawuza kuti nkhondo yatha. 14Choncho Abenjamini anabwera nthawi imeneyo ndipo Aisraeli anawapatsa akazi a ku Yabesi Giliyadi amene sanaphedwe. Koma sanapezeke owakwanira.

15Aisraeli anamvera chisoni Abenjamini, chifukwa Yehova anachita ngati waligwerula dzino fuko la Israeli. 16Choncho akuluakulu a msonkhano anati, “Kodi tikawapezera kuti akazi anthu otsalirawa kuti awakwatire popeza kuti akazi a fuko la Benjamini anaphedwa?” 17Iwo anati, “Abenjamini amene anapulumukawa ayenera kukhala ndi zidzukulu, kuti mtundu wa Israeli usafafanizike. 18Ife sitingathe kuwapatsa ana anthu aakazi kuti akwatire. Paja tinalumbira kuti, ‘Akhale wotembereredwa aliyense amene adzapereka mwana wake wamkazi kwa mwamuna wa fuko la Benjamini kuti akwatire.’ 19Ndipo anati, ‘Paja ku Silo kuli chikondwerero cha chaka ndi chaka cholemekeza Yehova. Tsono Silo ali kumpoto kwa Beteli, kummawa kwa msewu wochokera ku Beteli kupita ku Sekemu, ndiponso kummwera kwa Lebona.’ ”

20Choncho anawalamulira Abenjamini aja kuti, “Pitani mukabisale mʼminda ya mpesa 21ndipo mukakhale tcheru. Ana aakazi a ku Silo akadzatulukira kudzavina nawo magule, pomwepo inu mutuluke minda ya mpesa ndi kukawagwira aliyense wake ndi kupita nawo ku dziko la Benjamini. 22Ngati abambo awo kapena alongo awo adzabwera kudzadandaula kwa ife, tidzawawuza kuti, ‘Chonde, tikomereni mtima powalola kuti atenga ana anu aakaziwo popeza kuti ife sitinawapezere akazi pomenya nkhondo. Inunso simunachite kuwapatsa. Mukanatero ndiye mukanapalamula.’ ”

23Abenjamini anachitadi zimenezi. Mwa akazi amene ankavina aja anagwirapo ena, malingana ndi chiwerengero chawo, nawatenga kuti akhale akazi awo. Kenaka ananyamuka kubwerera ku dziko la kwawo, nakamanganso mizinda yawo ndi kumakhalamo.

24Pambuyo pake Aisraeli anachoka kumeneko ndi kubwerera kwawo, ku mafuko ndi ku mabanja awo, aliyense ku dera la cholowa chake.

25Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense ankangochita zimene zomukomera yekha.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Судьи 21:1-25

Жёны для вениамитян

1Исраильтяне поклялись в Мицпе:

– Никто из нас не отдаст свою дочь замуж за вениамитянина.

2Люди пошли в Вефиль, где и сидели перед Аллахом до вечера, громко и горько плача.

3– О Вечный, Бог Исраила, – говорили они, – почему это случилось с Исраилом? Почему сегодня у Исраила недостаёт одного рода?

4На следующее утро, встав рано, народ построил там жертвенник и принёс на нём всесожжения и жертвы примирения.

5И исраильтяне спросили:

– Какой из всех родов Исраила не пришёл на собрание перед Вечным?

Они дали великую клятву, что всякий, кто не придёт на собрание перед Вечным в Мицпу, непременно будет предан смерти.

6Исраильтяне горевали о своих братьях вениамитянах.

– Сегодня от Исраила отсечён один род, – говорили они. – 7Где нам взять жён для тех, кто уцелел, раз мы поклялись Вечным не отдавать им в жёны наших дочерей?

8Затем они спросили:

– Какой из исраильских родов не пришёл на собрание перед Вечным в Мицпу?

Выяснилось, что в лагерь на собрание не пришёл никто из Иавеша, что в Галааде, 9и когда они пересчитали народ, там не оказалось ни одного из жителей Иавеша, что в Галааде.

10И тогда общество отправило туда двенадцать тысяч воинов, велев им:

– Идите, предайте мечу всех жителей Иавеша, что в Галааде, вместе с женщинами и детьми. 11Сделайте вот что: полностью истребите всех мужчин и всех женщин, кроме девственниц.

12Среди жителей Иавеша, что в Галааде, они нашли четыреста девушек-девственниц и увели их в лагерь в Шило, что в земле Ханаана.

13Всё общество послало вениамитянам к скале Риммон предложение заключить мир. 14Тогда вениамитяне вернулись, и им дали женщин Иавеша, что в Галааде, которых оставили в живых. Но на всех не хватило.

15Народ горевал о Вениамине, потому что Вечный не сохранил целостности родов Исраила. 16И старейшины народа сказали:

– Женщины Вениамина истреблены, как нам добыть жён для мужчин, которые уцелели? 17У уцелевших вениамитян должны быть наследники, – сказали они, – чтобы Исраил не потерял один из своих родов. 18Мы не можем дать им в жёны своих дочерей, ведь мы, исраильтяне, поклялись: «Проклят всякий, кто даст жену вениамитянину». 19Но послушайте, праздник Вечного21:19 Возможно, здесь говорится об одном из праздников, установленных в Таурате (см. Исх. 23:14-17 и таблицу «Праздники в Исраиле» на странице ##), или же о каком-то местном празднике урожая винограда. ежегодно отмечается в Шило, что на севере от Вефиля и на востоке от дороги, что ведёт от Вефиля в Шехем и на юг от Левоны.

20И они научили вениамитян, говоря:

– Идите, спрячьтесь в виноградниках 21и наблюдайте. Когда девушки Шило выйдут, чтобы кружиться в плясках, выбегайте из виноградников, хватайте каждый себе в жёны одну из девушек Шило и ступайте в землю Вениамина. 22Когда их отцы или братья станут жаловаться нам, мы им скажем:

– Будьте великодушны и оставьте их нам, потому что мы не взяли для них жён на войне, а раз не вы сами отдали их нам, то вы и не виновны.

23Так вениамитяне и поступили. Когда девушки плясали, каждый мужчина схватил по одной и унёс, чтобы она стала его женой. После этого они вернулись в свой надел, отстроили города и поселились в них. 24А исраильтяне тогда же покинули то место и пошли домой к своим родам и кланам, каждый – в свой надел.

25В те дни у Исраила не было царя, и каждый делал то, что считал правильным.