Oweruza 17 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 17:1-13

Mafuno a Mika

1Munthu wina dzina lake Mika wochokera ku dziko la mapiri la Efereimu anawuza amayi ake kuti 2“Ndinamva inu mukutemberera munthu amene anaba ndalama zanu zasiliva 1,100. Ndalamazo zili ndi ine, ndinatenga ndine.”

Pamenepo amayi akewo anati, “Yehova akudalitse mwana wanga!”

3Choncho Mika anabweza ndalama 1,100 za siliva kwa amayi ake, ndipo amayi akewo anati, “Ine ndapatulira Yehova ndalama za silivazi kuti mwana wanga aseme fano ndi kulikuta ndi siliva. Ndiye tsopano ndikubwezera ndalamazo.”

4Tsono Mika atabweza ndalama zija kwa amayi ake, iwo anatengapo ndalama za siliva 200 namupatsa mmisiri wosula siliva. Iye anakonza fano, nasungunula siliva uja ndi kulikutira fano lija. Ndipo Mika anayika fanolo mʼnyumba mwake.

5Mikayu anali ndi kachisi, ndipo anapanga efodi ndi mafano otchedwa terafimu. Anapatula mwana wake mmodzi kuti akhale wansembe. 6Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense amachita zomwe zinamukomera.

7Ku Betelehemu mʼdziko la Yuda kunali mnyamata wina amene anali wa fuko la Levi. 8Iyeyu anachoka mu mzinda wa Betelehemu uja ku Yuda kukafuna malo ena okhala. Akuyenda, anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ku nyumba ya Mika.

9Tsono Mika anamufunsa kuti, “Mukuchokera kuti?”

Ndipo iye anayakha kuti, “Ndine Mlevi wochokera ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Ndikufunafuna malo okhala.”

10Tsono Mika anati kwa iye, “Khalani ndi ine. Mukhale ngati mlangizi wanga ndi wansembe, ndipo ine ndizikupatsani ndalama za siliva khumi pa chaka komanso zovala ndi zakudya.” 11Choncho Mleviyo anavomera kuti azikhala naye, ndipo mnyamatayo anakhala ngati mmodzi mwa ana ake aamuna. 12Pambuyo pake Mika anapatula Mleviyo ndipo mnyamatayu anakhala wansembe. Tsono ankakhala mʼnyumba ya Mika. 13Ndipo Mika anati, “Tsopano ndadziwa kuti Yehova adzandikomera mtima chifukwa Mleviyu ndiye wakhala wansembe wanga.”

Nueva Versión Internacional

Jueces 17:1-13

Los ídolos de Micaías

1En la región montañosa de Efraín había un hombre llamado Micaías, 2quien dijo a su madre:

—Con respecto a los mil siclos17:2 Es decir, aprox. 12.6 kg; también en v. 3. de plata que te robaron y sobre los cuales te oí pronunciar una maldición, yo tengo esa plata; yo te la robé.

Su madre dijo:

—¡Que el Señor te bendiga, hijo mío!

3Cuando Micaías devolvió a su madre los mil siclos de plata, ella dijo:

—Solemnemente consagro mi plata al Señor para que mi hijo haga una imagen tallada y un ídolo de fundición.17:3 una … fundición. Alt. una imagen tallada revestida de metal fundido; también en v. 4 y 18:14. Ahora pues, te la devuelvo.

4Cuando él le devolvió la plata a su madre, ella tomó doscientos siclos17:4 Es decir, aprox. 2.3 kg. de plata y se los dio a un platero, quien hizo con eso una imagen tallada y un ídolo de fundición, que fueron puestos en la casa de Micaías.

5Este Micaías tenía un santuario. Hizo un efod y algunos ídolos familiares,17:5 ídolos familiares. Lit. terafines. y consagró a uno de sus hijos como sacerdote. 6En aquella época no había rey en Israel; cada uno hacía lo que le parecía mejor.

7Un joven levita, que vivía como extranjero en Belén de Judá, 8salió de aquella ciudad en busca de algún otro lugar donde vivir. En el curso de su viaje17:8 En el curso de su viaje. Alt. Para ejercer su oficio. llegó a la casa de Micaías en la región montañosa de Efraín.

9—¿De dónde vienes? —preguntó Micaías.

—Soy levita, de Belén de Judá —contestó él—, y estoy buscando un lugar donde vivir.

10—Vive conmigo —le propuso Micaías—, y sé mi padre y sacerdote; yo te daré diez siclos17:10 Es decir, aprox. 115 g. de plata al año, además de ropa y comida.

11El joven levita aceptó quedarse a vivir con él y fue para Micaías como uno de sus hijos. 12Luego Micaías invistió al levita, y así el joven se convirtió en su sacerdote y vivió en su casa. 13Y Micaías dijo: «Ahora sé que el Señor me hará prosperar, porque tengo a un levita como sacerdote».