Oweruza 17 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 17:1-13

Mafuno a Mika

1Munthu wina dzina lake Mika wochokera ku dziko la mapiri la Efereimu anawuza amayi ake kuti 2“Ndinamva inu mukutemberera munthu amene anaba ndalama zanu zasiliva 1,100. Ndalamazo zili ndi ine, ndinatenga ndine.”

Pamenepo amayi akewo anati, “Yehova akudalitse mwana wanga!”

3Choncho Mika anabweza ndalama 1,100 za siliva kwa amayi ake, ndipo amayi akewo anati, “Ine ndapatulira Yehova ndalama za silivazi kuti mwana wanga aseme fano ndi kulikuta ndi siliva. Ndiye tsopano ndikubwezera ndalamazo.”

4Tsono Mika atabweza ndalama zija kwa amayi ake, iwo anatengapo ndalama za siliva 200 namupatsa mmisiri wosula siliva. Iye anakonza fano, nasungunula siliva uja ndi kulikutira fano lija. Ndipo Mika anayika fanolo mʼnyumba mwake.

5Mikayu anali ndi kachisi, ndipo anapanga efodi ndi mafano otchedwa terafimu. Anapatula mwana wake mmodzi kuti akhale wansembe. 6Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense amachita zomwe zinamukomera.

7Ku Betelehemu mʼdziko la Yuda kunali mnyamata wina amene anali wa fuko la Levi. 8Iyeyu anachoka mu mzinda wa Betelehemu uja ku Yuda kukafuna malo ena okhala. Akuyenda, anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ku nyumba ya Mika.

9Tsono Mika anamufunsa kuti, “Mukuchokera kuti?”

Ndipo iye anayakha kuti, “Ndine Mlevi wochokera ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Ndikufunafuna malo okhala.”

10Tsono Mika anati kwa iye, “Khalani ndi ine. Mukhale ngati mlangizi wanga ndi wansembe, ndipo ine ndizikupatsani ndalama za siliva khumi pa chaka komanso zovala ndi zakudya.” 11Choncho Mleviyo anavomera kuti azikhala naye, ndipo mnyamatayo anakhala ngati mmodzi mwa ana ake aamuna. 12Pambuyo pake Mika anapatula Mleviyo ndipo mnyamatayu anakhala wansembe. Tsono ankakhala mʼnyumba ya Mika. 13Ndipo Mika anati, “Tsopano ndadziwa kuti Yehova adzandikomera mtima chifukwa Mleviyu ndiye wakhala wansembe wanga.”

Bibelen på hverdagsdansk

Dommerbogen 17:1-13

Mikas afgudsbilleder

1I Efraims højland boede der en mand ved navn Mika. 2En dag sagde han til sin mor: „Jeg hørte, hvordan du forbandede den tyv, der stjal 1100 sølvstykker fra dig. Her er de. Det var mig, der tog dem!” „Må Herren velsigne dig, fordi du sagde det, min søn,” svarede moderen. 3Så gav Mika pengene tilbage til hende.

Da sagde moderen: „De her sølvstykker vil jeg indvi til Herren. Jeg vil få lavet et afgudsbillede af dem og en støbt statuette, som du skal have, min søn.”

4Så tog hun 200 sølvstykker og gav dem til sølvsmeden, som lavede et gudebillede og en gudestatuette. Da de var færdige, blev de overdraget til Mika. 5Han fik lavet et gudehus til sine afgudsbilleder. Han lavede også nogle små husguder af træ og en efod, hvorefter han indviede en af sine sønner til at være præst. 6På den tid var der ingen konge i Israel, og folk gjorde, hvad de fandt for godt.

7-8En dag kom en ung levit til Mikas hus i Efraims højland. Han havde boet som fremmed i Betlehem i Judastammens område og var nu på udkig efter et nyt sted at slå sig ned.

9„Hvor kommer du fra?” spurgte Mika. „Jeg er levit og kommer fra Betlehem i Juda,” svarede den unge mand. „Jeg er ved at se mig om efter et nyt sted at bo.” 10„Hvis du vil blive her, kan du blive vejleder og præst hos mig,” foreslog Mika. „Jeg vil give dig ti sølvstykker om året plus tøj og kost og logi.”

11Den unge mand tog imod tilbuddet og boede derefter hos Mika, der behandlede ham som sin egen søn. 12Desuden indsatte Mika ham til at være sin personlige præst. 13„Nu er jeg sikker på, at Herren vil velsigne mig!” udbrød Mika. „For jeg har jo en rigtig levit som præst ved mit gudehus!”