Oweruza 15 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 15:1-20

Samsoni Abwezera Afilisti

1Patapita nthawi, mu nyengo yodula tirigu, Samsoni anatenga kamwana kambuzi ndipo anapita kukacheza kwa mkazi wake. Iye anati, “Ndikufuna kukalowa ku chipinda cha mkazi wanga.” Koma abambo a mkaziyo anamuletsa kutero.

2Abambo a mkaziyo anati, “Ine ndimaganiza kuti umamuda kwambiri nʼchifukwa chake ndinamupereka kwa mnzako. Kodi mngʼono wake uja sindiye wokongola kupambana iye? Ingotengani ameneyo mʼmalo mwake.”

3Samsoni anawawuza kuti, “Pano sindikhala wochimwa ndikawachita choyipa chachikulu Afilistiwa.” 4Choncho Samsoni anapita nakagwira nkhandwe 300 nazimangirira michira ziwiriziwiri ndipo pa fundo iliyonse ya michirayo anamangirira nsakali. 5Anayatsa nsakalizo kenaka ndi kuzitayira nkhandwe zija mʼminda ya tirigu ya Afilisti, ndipo zinatentha milu ya tirigu, ndi wosadula yemwe pamodzi ndi mitengo ya mpesa ndi ya olivi.

6Tsono Afilisti anayamba kufunsana kuti, “Ndani wachita izi?” Ena anati, “Ndi Samsoni mkamwini wa munthu wa ku Timna uja chifukwa Mtimunayo anatenga mkazi wake ndi kumupereka kwa mnzake.”

Choncho Afilisti anapita kukatentha mtsikanayo pamodzi ndi abambo ake. 7Samsoni anawawuza kuti, “Ngati mumachita zangati zimenezi, ndiye ine sindileka mpaka nditakulipsirani.” 8Choncho Samsoni anamenyana nawo koopsa ndipo anapha ambiri a iwo. Kenaka anakalowa mʼphanga la Etamu, nakhala momwemo.

9Pambuyo pake Afilisti anakamanga misasa ya nkhondo mʼdziko la Yuda, ndi kuthira nkhondo mʼdera la Lehi. 10Anthu a fuko la Yuda anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwabwera kudzamenyana nafe?”

Iwo anayankha kuti, “Tabwera kudzamanga Samsoni ndi kuti timuchite zofanana ndi zimene anatichita.”

11Ndipo anthu 3,000 a ku Yuda anapita ku phanga la Etamu, ndi kukamufunsa Samsoni kuti, “Kodi iwe sudziwa kuti ife amatilamulira ndi Afilisti? Tsono ndi chiyani chimene watichitachi?”

Iye anayankha kuti, “Ine ndinachita zomwe iwo anandichita.”

12Iwo anati kwa iye, “Ife tabwera kuti tikumange ndi kukupereka kwa Afilisti.”

Ndipo Samsoni anati, “Lonjezani mwa lumbiro kuti simundipha ndinu.”

13Iwo anamuyankha kuti, “Ayi, ife sitikupha. Koma tingokumanga ndi kukupereka mʼmanja mwa Afilisti.” Choncho anamumanga ndi zingwe ziwiri zatsopano namutulutsa mʼphanga muja. 14Samsoni anafika ku Lehi, ndipo Afilisti anamuchingamira akufuwula. Nthawi yomweyo Mzimu wa Yehova unatsika pa iye mwamphamvu ndipo zingwe zimene anamumanga nazo zinasanduka ngati thonje lopsa mʼmoto, zinachita ngati zasungunuka nʼkuchoka mʼmanja mwake. 15Anapeza chibwano cha bulu amene anali atangofa kumene. Anachitola ndi kuphera nacho anthu 1,000.

16Ndipo Samsoni anati,

“Ndi chibwano cha bulu,

milu ndi milu ya anthu.

Ndi chibwano cha bulu,

ndapha anthu 1,000.”

17Atatsiriza kuyankhula, anataya chibwanocho, ndipo malowo anawatcha Ramati-Lehi.

18Pambuyo pake anamva ludzu kwambiri ndipo anayitana Yehova mopempha kuti, “Inu mwapatsa mtumiki wanu chipulumutso chachikulu chotere. Kodi tsopano ndife ndi ludzu ndi kugwidwa ndi anthu osachita mdulidwewa?” 19Pamenepo Mulungu anangʼamba nthaka ku Lehi, ndipo madzi anatuluka mʼdzenjemo. Samsoni anamwa madziwo, ndipo mphamvu zake zinabwerera nakhalanso monga analili. Choncho chitsimecho chinatchedwa Eni-Hakore, ndipo chilipobe ku Lehiko mpaka lero.

20Samsoni anatsogolera Israeli pa nthawi ya Afilisti kwa zaka makumi awiri.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

士师记 15:1-20

参孙向非利士人报仇

1过了些日子,在割麦的时候,参孙带着一只山羊羔去探望他妻子。他说:“我要进内室见我妻子。”他岳父却不让他进去, 2并对他说:“我以为你非常恨她,所以我把她改嫁给你的伴郎了。她妹子不是比她更美丽吗?你可以娶来代替她。”

3参孙说:“这次我要加害非利士人,可不能怪我了。”

4于是,他出去捉了三百只狐狸,把它们的尾巴一对一对绑起来,将火把绑在两条尾巴中间, 5然后点燃火把,把狐狸放进非利士人的麦田里,将割好的麦捆和未割的麦子、葡萄园和橄榄园都烧毁了。 6非利士人问:“这是谁干的?”有人回答说:“是亭拿人的女婿参孙干的,因为他岳父把他的妻子嫁给了他的伴郎。”非利士人就去放火烧死了参孙的妻子和岳父。 7参孙说:“你们既然这样做,我不向你们报仇誓不罢休。” 8参孙大肆击杀他们,杀死了很多人。事后,他下到以坦,住在那里的岩洞里。

9非利士人进犯犹大,在利希一带扎营。 10犹大人问他们:“你们为什么来攻打我们?”非利士人回答说:“我们来捉拿参孙,向他以报还报。” 11于是,有三千犹大人去以坦的岩洞找参孙,对他说:“难道你不知道非利士人是我们的统治者吗?你为什么连累我们?”参孙回答说:“我只是以牙还牙。” 12犹大人说:“我们来是要捉拿你,把你交给非利士人。”参孙说:“你们要保证你们不会亲手杀我。” 13他们说:“我们不会杀你,只将你绑起来交给非利士人。”于是,他们用两根新绳子把参孙捆绑起来带出岩洞。

14非利士人看见参孙来到利希,就呐喊着迎了上去。耶和华的灵降在参孙身上,绑在他手臂上的绳子就像被火烧的麻线一样脱落下来。 15他看到一块还没有干的驴腮骨,就捡起来用它杀了一千个非利士人。 16参孙说:

“用这驴腮骨,我杀人成堆;

用这驴腮骨,我杀戮千人。”

17说完,他扔掉了手中的驴腮骨。因此,那地方叫拉末·利希15:17 拉末·利希”意思是“腮骨岗”。

18参孙觉得非常口渴,便向耶和华呼求说:“你既然借着仆人的手大败敌人,难道你会让我渴死、落在这些未受割礼的人手中吗?” 19于是,上帝使利希的一处洼地裂开,涌出水来。参孙喝后恢复了精神。因此,那水泉叫隐哈·歌利15:19 隐哈·歌利”意思是“呼求者的泉”。。那水泉今天还在利希20非利士人统治期间,参孙以色列的士师二十年。