Oweruza 14 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 14:1-20

Ukwati wa Samsoni

1Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti. 2Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”

3Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?”

Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.” 4(Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli). 5Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye. 6Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo. 7Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.

8Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake. 9Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.

10Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata. 11Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.

12Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero. 13Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.”

Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”

14Iye anati,

“Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake;

ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.”

Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.

15Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”

16Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.”

Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?” 17Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.

18Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti,

“Chozuna nʼchiyani choposa uchi?

Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?”

Samsoni anawawuza kuti,

“Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono,

simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”

19Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu. 20Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Судьи 14:1-20

Женитьба Самсона

1Самсон пошёл в Тимну и встретил там молодую филистимлянку. 2Вернувшись, он сказал отцу и матери:

– Я видел в Тимне одну филистимлянку, возьмите мне её в жёны.

3Отец и мать ответили ему:

– Разве нет женщин среди твоих родичей или всего нашего народа? Неужели ты пойдёшь за женой к необрезанным филистимлянам?

Но Самсон сказал отцу:

– Возьми мне её. Она мне понравилась.

4(Его родители не знали, что Вечный использовал эту ситуацию, чтобы отомстить филистимлянам, которые в то время правили Исроилом.)

5И Самсон пошёл в Тимну вместе со своими родителями. Когда они подходили к виноградникам Тимны, внезапно навстречу Самсону, рыча, выскочил молодой лев. 6На Самсона сошёл Дух Вечного, и Самсон разорвал льва голыми руками, точно козлёнка. Но ни отцу, ни матери о сделанном он не рассказал. 7Затем он пришёл и поговорил с той женщиной, и она ему понравилась.

8Когда некоторое время спустя он возвращался, чтобы жениться на ней, он пошёл посмотреть на львиный труп. В нём оказался пчелиный рой и мёд. 9Он выскреб мёд руками и ел его по дороге. Придя к своим родителям, он дал мёда и им, и они тоже ели. Но он не сказал им о том, что взял мёд из львиного трупа14:9 Самсон как назорей не имел права прикасаться к мёртвому телу (см. Чис. 6:6)..

10И вот отец Самсона пришёл в дом к невесте. Самсон устроил там пир, как делают по обычаю женихи. 11Когда он показался там, ему выбрали тридцать брачных друзей, чтобы они были с ним.

12Самсон сказал им:

– Загадаю-ка я вам загадку. Если вы сможете разгадать её за семь дней пира, я дам вам тридцать одеяний из тонкого полотна и тридцать смен одежды. 13А если не сможете разгадать, вы сами дадите мне тридцать одеяний из тонкого полотна и тридцать смен одежды.

– Загадывай свою загадку, – сказали они, – послушаем.

14Он сказал:

– Из едока получилась еда,

из силача получилось сладкое.

И три дня они не могли разгадать эту загадку.

15На четвёртый14:15 В других рукописях: «седьмой», но см. ст. 14. день они сказали жене Самсона:

– Выведай разгадку у своего мужа, а не то мы сожжём тебя и дом твоего отца. Вы что, приглашали нас, чтобы обобрать?

16Жена Самсона стала плакать перед ним:

– Ты ненавидишь меня! Ты не любишь меня по-настоящему. Ты загадал моему народу загадку, а мне ответа не сказал.

– Я не открыл его даже отцу и матери, – ответил он. – Почему же я должен открывать его тебе?

17Она плакала перед ним все семь дней, пока у них продолжался пир. На седьмой день он наконец открыл ей, потому что она извела его. А она сказала ответ своему народу.

18В седьмой день, перед заходом солнца, жители города сказали ему:

– Что слаще мёда?

Что сильнее льва?

Самсон сказал им:

– Не пахали бы вы на моей тёлке –

не разгадали бы и моей загадки.

19Дух Вечного сошёл на него, и Самсон пошёл в Ашкелон, убил тридцать жителей города, забрал их пожитки и отдал их одежды тем, кто разгадал загадку. Кипя гневом, он ушёл в дом своего отца. 20А жену Самсона отдали тому, кто был у него дружкой на свадьбе.