Nyimbo ya Solomoni 8 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 8:1-14

1Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga,

amene anayamwa mawere a amayi anga!

Ndikanakumana nawe pa njira,

ndikanakupsompsona,

ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.

2Ndikanakutenga

ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,

amayi amene anandiphunzitsa,

ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe,

zotsekemera za makangadza.

3Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

4Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani:

musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

Abwenzi

5Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo,

atatsamira wokondedwa wakeyo?

Mkazi

Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi,

pamenepo ndi pamene amayi anachirira,

pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.

6Undiyike pamtima pako ngati chidindo,

ngati chidindo cha pa dzanja lako;

pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa,

nsanje ndiyaliwuma ngati manda.

Chikondi chimachita kuti lawilawi

ngati malawi a moto wamphamvu.

7Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,

mitsinje singachikokolole chikondicho.

Ngati wina apereka chuma chonse

cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi,

adzangonyozeka nazo kotheratu.

Abwenzi

8Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono,

koma alibe mawere,

kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu

pa tsiku limene adzamufunsire?

9Ngati iye ndi khoma,

tidzamumangira nsanja ya siliva.

Ngati iye ndi chitseko,

tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.

Mkazi

10Ine ndili ngati khoma,

ndipo mawere anga ndi nsanja zake.

Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa

ndine wobweretsa mtendere.

11Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni;

iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi,

aliyense mwa iwo ankayenera kupereka

ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.

12Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha.

Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000

ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.

Mwamuna

13Iwe amene umakhala mʼminda

uli pamodzi ndi anzako,

ndilole kuti ndimve liwu lako!

Mkazi

14Fulumira wokondedwa wanga,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena mwana wa mbawala

wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.

New Russian Translation

Книга Песнь Песней 8:1-14

1О, если бы ты был мне братом,

которого моя мать вскормила грудью!

Тогда я, встретив тебя на улице,

целовала бы тебя,

и меня бы не осудили.

2Я бы повела тебя

и привела в дом матери моей –

той, что учила меня8:2 Или: « … матери моей; там ты учил бы меня»..

Я дала бы тебе выпить пряного вина

и сок моих гранатов.

3Его левая рука под моей головой,

а правая обнимает меня.

4Дочери Иерусалима, заклинаю вас:

не будите и не возбуждайте любви,

пока она сама того не пожелает.

Молодые женщины:

5– Кто это восходит от пустыни,

прижавшись к своему возлюбленному?

Она:

– Под яблоней я разбудила тебя:

там, где зачала тебя мать твоя,

там, где она тебя родила.

6Положи меня, как печать, на сердце твое,

как перстень, на руку свою,

потому что любовь крепка, как смерть,

жар ее свиреп, как преисподняя8:6 Евр.: «шеол». Шеол – место, где пребывают души умерших..

Она горит ярким огнем,

она подобна бушующему пламени.

7Множество вод не потушит любви,

и реки не смоют ее.

Если бы кто и отдавал все богатство своего дома за любовь,

он был бы отвергнут с презрением.

Братья:

8– Есть у нас младшая сестра,

у которой груди еще не выросли.

Что мы будем делать с сестрой нашей

в день, когда будут сватать ее?

9Если она – стена,

то мы воздвигнем на ней серебряные башни.

Если она – дверь,

то мы запрем ее за кедровыми досками.

Она:

10– Я – стена, и груди мои, словно башни,

поэтому я нашла благоволение в его глазах8:10 Или: «поэтому он смотрит на меня, как на достигшую зрелости»..

11У Соломона был виноградник в Баал-Гамоне8:11 Местонахождение Баал-Гамона неизвестно. Значение этого названия – «богатый господин».;

он сдал его арендаторам.

Каждый должен был приносить за плоды его

тысячу серебряных монет.

12А мой виноградник в моем распоряжении!

Тысяча серебряных монет – пусть тебе, Соломон,

а двести – взращивающим плоды.

Он:

13– Жительница садов!

Друзья внимают голосу твоему,

позволь и мне услышать его.

Она:

14– Спеши, возлюбленный мой,

скачи, словно газель

или как молодой олень

в горах, где произрастают пряности.