Nyimbo ya Solomoni 7 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 7:1-13

1Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola

mu nsapato wavalazo!

Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali,

ntchito ya manja ya mmisiri waluso.

2Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino

chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo.

Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu

utazunguliridwa ndi maluwa okongola.

3Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala,

ngati mphoyo zamapasa.

4Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu.

Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni,

amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu.

Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni,

yoyangʼana ku Damasiko.

5Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli.

Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu;

mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.

6Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa,

iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!

7Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa,

ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.

8Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa;

ndidzathyola zipatso zake.”

Mawere ako ali ngati maphava a mphesa,

fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,

9ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri.

Mkazi

Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga,

ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.

10Wokondedwayo ine ndine wake,

ndipo chilakolako chake chili pa ine.

11Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi,

tikagone ku midzi.

12Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa,

tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira,

ngati maluwa ake ayamba kuoneka,

komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa.

Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.

13Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino,

ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma,

zatsopano ndi zakale zomwe,

zimene ndakusungira wokondedwa wanga.

Het Boek

Hooglied 7:1-13

1Och, prinses, wat loop je sierlijk! De welvingen van je lichaam lijken door een meesterbeeldhouwer ontworpen.

2Je navel lijkt op een sierlijke kelk, waar een heerlijke wijn in hoort. Je buik lijkt op een schoof tarwe, versierd met lelies.

3Je borsten zijn zo mooi als twee jongen van de gazellen.

4Je hals rijst als een ivoren toren op en je ogen lijken op de diepglanzende vijvers van Chesbon die bij de poort Bath-Rabbim liggen. Je neus is zo fraai als de toren van de Libanon die over de stad Damascus uitziet.

5Je hoofd steekt fier omhoog als de berg Karmel en je haar glanst koperrood. De koning kijkt er geboeid naar.

6Wat is de liefde heerlijk! Heerlijker dan alle andere dingen waarnaar men kan verlangen.

7Je slanke lichaam lijkt op een dadelpalm waaraan de borsten als dadeltrossen bloeien.

8Ik zei dat ik die palmboom wilde beklimmen en de trossen ervan plukken wilde. Je borsten lijken op rijpe druiventrossen. De geur van je adem doet mij denken aan de geur van appels.

9Je gehemelte is heerlijker dan de beste wijn…

…laat die wijn naar mijn liefste toevloeien, zodat hij hem slapend kan drinken.

10Ik behoor toe aan mijn liefste, ik verlang naar hem.

11Kom, mijn liefste, laten wij samen het veld ingaan en overnachten in een van de dorpen.

12Of laten wij heel vroeg de wijngaard ingaan en kijken of de wijnstokken al uitlopen, of de knoppen al openspringen en de granaatappelbomen al bloeien. Daar zal ik mij aan je geven.

13Ik ruik de geur van de liefdesappels en overal groeien de heerlijkste vruchten. Mijn liefste, ik heb ze voor jou bewaard.