Nyimbo ya Solomoni 6 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 6:1-13

Abwenzi

1Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,

kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti?

Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti

kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?

Mkazi

2Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake,

ku timinda ta zokometsera zakudya,

akukadyetsa ziweto zake ku minda,

ndiponso akuthyola maluwa okongola.

3Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga;

amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.

Mwamuna

4Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza,

wokongola kwambiri ngati Yerusalemu,

ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.

5Usandipenyetsetse;

pakuti maso ako amanditenga mtima.

Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi

zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.

6Mano ako ali ngati gulu la nkhosa

zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa,

iliyonse ili ndi ana amapasa,

palibe imene ili yokha.

7Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu,

masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.

8Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60,

ndi azikazi 80,

ndi anamwali osawerengeka;

9koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense;

mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake,

mwana wapamtima wa amene anamubereka.

Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala;

akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.

Abwenzi

10Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha,

wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa,

wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?

Mwamuna

11Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi

kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa,

kukaona ngati mpesa waphukira

kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.

12Ndisanazindikire kanthu,

ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.

Abwenzi

13Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami;

bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe!

Mwamuna

Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami,

pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Cantares 6:1-13

El coro

1¿A dónde se ha ido tu amado,

tú, bella entre las bellas?

¿Hacia dónde se ha encaminado?

¡Iremos contigo a buscarlo!

La amada

2Mi amado ha bajado a su jardín,

a los lechos de bálsamo,

para retozar en los jardines

y recoger azucenas.

3Yo soy de mi amado, y mi amado es mío;

él apacienta su rebaño entre azucenas.

Quinto Canto

El amado

4Tú, amada mía, eres bella como Tirsá,

encantadora como Jerusalén,

majestuosa como las estrellas del cielo.

5Aparta de mí la mirada,

que tus ojos me tienen fascinado.

Tus cabellos son como los rebaños de cabras

que retozan en Galaad.

6Tus dientes son como rebaños de cabritas

recién salidas del baño.

Cada una de ellas tiene su pareja,

ninguna de ellas va sola.

7Tus mejillas, tras el velo,

parecen dos mitades de granadas.

8Pueden ser sesenta las reinas,

ochenta las concubinas

e innumerables las vírgenes,

9pero una sola es mi palomita preciosa,

la hija consentida de su madre,

la favorita de quien le dio la vida.

Las mujeres la ven y la bendicen;

las reinas y las concubinas la alaban.

El coro

10¿Quién es esta, admirable como la aurora?

¡Es bella como la luna,

radiante como el sol,

majestuosa como las estrellas del cielo!

El amado

11Descendí al huerto de los nogales

para admirar los nuevos brotes en el valle,

para admirar los retoños de las vides

y los granados en flor.

12Sin darme cuenta, mi pasión me puso

entre las carrozas reales de mi pueblo.6:12 entre … mi pueblo. Alt. entre los carros de Aminadab.

Los amigos

13Vuelve, Sulamita, vuelve;

vuélvete a nosotros,

¡queremos contemplarte!

El amado

¿Y por qué han de contemplar a la Sulamita,

como en las danzas de los campamentos?