Nyimbo ya Solomoni 6 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 6:1-13

Abwenzi

1Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,

kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti?

Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti

kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?

Mkazi

2Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake,

ku timinda ta zokometsera zakudya,

akukadyetsa ziweto zake ku minda,

ndiponso akuthyola maluwa okongola.

3Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga;

amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.

Mwamuna

4Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza,

wokongola kwambiri ngati Yerusalemu,

ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.

5Usandipenyetsetse;

pakuti maso ako amanditenga mtima.

Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi

zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.

6Mano ako ali ngati gulu la nkhosa

zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa,

iliyonse ili ndi ana amapasa,

palibe imene ili yokha.

7Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu,

masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.

8Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60,

ndi azikazi 80,

ndi anamwali osawerengeka;

9koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense;

mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake,

mwana wapamtima wa amene anamubereka.

Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala;

akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.

Abwenzi

10Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha,

wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa,

wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?

Mwamuna

11Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi

kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa,

kukaona ngati mpesa waphukira

kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.

12Ndisanazindikire kanthu,

ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.

Abwenzi

13Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami;

bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe!

Mwamuna

Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami,

pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?

Bibelen på hverdagsdansk

Højsangen 6:1-12

Jerusalems unge piger:

1„Du smukkeste blandt kvinder, sig os,

hvor din elskede er gået hen,

så vi kan hjælpe dig med at finde ham!”

Den unge pige:

2„Min elskede er gået ned i sin have til bedene med krydderurter.

Der græsser han sin flok og plukker liljer.

3Min elskede er min, og jeg er hans.

Han græsser sin flok mellem liljerne.”

Femte sang: De nygiftes glæde over hinanden

Den unge mand:

4„Min elskede, du er yndig som kongebyen Tirtza,

bedårende som Jerusalem,

ærefrygtindgydende som en række bannere.6,4 Eller „som en marcherende hær.”

5Se ikke så direkte på mig,

for dine øjnes skønhed overvælder mig.

Dit hår bølger nedad som en flok sorte geder

på en bakkeskråning i Gilead.

6Dine tænder er hvide som en nyvasket fåreflok;

hver har sin tvilling, ingen står alene.

7Dine kinder bag sløret er røde

som to halve granatæbler.

8Om jeg så havde tres dronninger og firs medhustruer

foruden utallige tjenestepiger,

9ville du overgå dem alle i skønhed, min due—

du er fuldkommen!

Du er din mors eneste datter,

du er hendes yndling,

og hun har kun godt at sige om dig.

Byens piger priser din skønhed, når de ser dig,

dronninger og medhustruer lovpriser din charme og ynde.

10‚Hvem er skøn som morgenrøden,’ spørger de,

‚smuk som månen, strålende som solen,

og ærefrygtindgydende som en række bannere?’6,10 Eller „en hær under banner”.

11Jeg gik ned gennem nøddehegnet for at finde blomster i dalen,

for at se, om der var nye skud på vinrankerne

og blomsterknopper på granatæbletræerne.

12Jeg var ude af mig selv af kærlighed.

Giv mig dér din dejlige ‚myrra’, du fyrstedatter.”6,12 Teksten er uklar. Jf. 7,11-13.