Nyimbo ya Solomoni 5 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 5:1-16

Mwamuna

1Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga;

ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga.

Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe;

ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga.

Abwenzi

Idyani abwenzi anga, imwani;

Inu okondana, imwani kwambiri.

Mkazi

2Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso.

Tamverani, bwenzi langa akugogoda:

“Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa,

nkhunda yanga, wangwiro wanga.

Mutu wanga wanyowa ndi mame,

tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”

3Ndavula kale zovala zanga,

kodi ndizivalenso?

Ndasamba kale mapazi anga

kodi ndiwadetsenso?

4Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko;

mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.

5Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo,

ndipo manja anga anali noninoni ndi mure,

zala zanga zinali mure chuchuchu,

pa zogwirira za chotsekera.

6Ndinamutsekulira wachikondi wanga,

koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita.

Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake.

Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze.

Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.

7Alonda anandipeza

pamene ankayendera mzindawo.

Anandimenya ndipo anandipweteka;

iwo anandilanda mwinjiro wanga,

alonda a pa khoma aja!

8Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani,

mukapeza wokondedwa wangayo,

kodi mudzamuwuza chiyani?

Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.

Abwenzi

9Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,

kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji?

Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani

kuti uzichita kutipempha motere?

Mkazi

10Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi

pakati pa anthu 1,000.

11Mutu wake ndi golide woyengeka bwino;

tsitsi lake ndi lopotanapotana,

ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.

12Maso ake ali ngati nkhunda

mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,

ngati nkhunda zitasamba mu mkaka,

zitayima ngati miyala yamtengowapatali.

13Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya

zopatsa fungo lokoma.

Milomo yake ili ngati maluwa okongola

amene akuchucha mure.

14Manja ake ali ngati ndodo zagolide

zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali.

Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu

woyikamo miyala ya safiro.

15Miyendo yake ili ngati mizati yamwala,

yokhazikika pa maziko a golide.

Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni,

abwino kwambiri ngati mkungudza.

16Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri;

munthuyo ndi wokongola kwambiri!

Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa,

inu akazi a ku Yerusalemu.

New International Reader’s Version

Song of Songs 5:1-16

The king says

1“My bride, I have come into my garden.

My sister, I’ve gathered my myrrh and my spice.

I’ve eaten my honeycomb and my honey.

I’ve drunk my wine and my milk.”

The other women say to the Shulammite woman and to Solomon

“Friends, eat and drink.

Drink up all the love you want.”

The woman says

2“I slept, but my heart was awake.

Listen! The one who loves me is knocking.

He says, ‘My sister, I love you.

Open up so I can come in.

You are my dove.

You are perfect in every way.

My head is soaked with dew.

The night air has made my hair wet.’

3“But I’ve taken off my robe.

Must I put it on again?

I’ve washed my feet.

Must I get them dirty again?

4My love put his hand through the opening.

My heart began to pound for him.

5I got up to open the door for my love.

My hands dripped with myrrh.

It flowed from my fingers

onto the handles of the lock.

6I opened the door for my love.

But he had left and was gone.

My heart sank because he had left.

I looked for him but didn’t find him.

I called out to him, but he didn’t answer.

7Those on guard duty found me

as they were walking around in the city.

They beat me. They hurt me.

Those on guard duty at the walls

took my coat away from me.

8Women of Jerusalem, make me a promise.

If you find the one who loves me,

tell him our love has made me weak.”

The other women say

9“You are the most beautiful woman of all.

How is the one you love better than others?

How is he better than anyone else?

Why do you ask us to make you this promise?”

The woman says

10“The one who loves me is tanned and handsome.

He’s the finest man among 10,000.

11His head is like the purest gold.

His hair is wavy and as black as a raven.

12His eyes are like doves

by streams of water.

They look as if they’ve been washed in milk.

They are set like jewels in his head.

13His cheeks are like beds of spice

giving off perfume.

His lips are like lilies

dripping with myrrh.

14His arms are like rods of gold

set with topaz.

His body is like polished ivory

decorated with lapis lazuli.

15His legs are like pillars of marble

set on bases of pure gold.

He looks like the finest cedar tree

in the mountains of Lebanon.

16His mouth is very sweet.

Everything about him is delightful.

That’s what the one who loves me is like.

That’s what my friend is like, women of Jerusalem.”