Nyimbo ya Solomoni 4 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 4:1-16

Mwamuna

1Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga!

Ndithudi, ndiwe wokongola!

Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu.

Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi

zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.

2Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene,

zochokera kozisambitsa kumene.

Iliyonse ili ndi ana amapasa;

palibe imene ili yokha.

3Milomo yako ili ngati mbota yofiira;

pakamwa pako ndi pokongola kwambiri.

Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba

kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.

4Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide,

yomangidwa bwino ndi yosalala;

pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000,

zishango zonsezo za anthu ankhondo.

5Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala,

ngati ana amapasa a nswala

amene akudya pakati pa maluwa okongola.

6Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira

ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,

ndidzapita ku phiri la mure

ndi ku chitunda cha lubani.

7Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga;

palibe chilema pa iwe.

8Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga,

tiye tichoke ku Lebanoni,

utsikepo pa msonga ya Amana,

kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni,

kuchoka ku mapanga a mikango

ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.

9Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima,

iwe wanditenga mtima

ndi kapenyedwe ka maso ako,

ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.

10Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa!

Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo,

ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!

11Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi;

pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi.

Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.

12Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa;

ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.

13Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza;

muli zipatso zokoma kwambiri,

muli hena ndi nadi,

14nadi ndi safiro,

kalamusi ndi sinamoni,

komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino.

Mulinso mure ndi aloe

ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.

15Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda,

chitsime cha madzi oyenda,

mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.

Mkazi

16Dzuka, iwe mphepo yakumpoto,

ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera!

Uzira pa munda wanga,

kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse.

Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake

ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.

Nova Versão Internacional

Cântico dos Cânticos 4:1-16

O Amado

1Como você é linda, minha querida!

Ah, como é linda!

Seus olhos, por trás do véu, são pombas.

Seu cabelo é como um rebanho de cabras

que vêm descendo do monte Gileade.

2Seus dentes são como um rebanho de ovelhas

recém-tosquiadas que vão subindo do lavadouro.

Cada uma tem o seu par;

não há nenhuma sem crias.

3Seus lábios são como um fio vermelho;

sua boca é belíssima.

Suas faces, por trás do véu,

são como as metades de uma romã.

4Seu pescoço é como a torre de Davi,

construída como arsenal.

Nela estão pendurados mil escudos,

todos eles escudos de heroicos guerreiros.

5Seus dois seios são como filhotes de cervo,

como filhotes gêmeos de uma gazela

que repousam entre os lírios.

6Enquanto não raia o dia

e as sombras não fogem,

irei à montanha da mirra

e à colina do incenso.

7Você é toda linda, minha querida;

em você não há defeito algum.

8Venha do Líbano comigo, minha noiva,

venha do Líbano comigo.

Desça do alto do Amana,

do topo do Senir, do alto do Hermom,

das covas dos leões

e das tocas dos leopardos nas montanhas.

9Você fez disparar o meu coração,

minha irmã, minha noiva;

fez disparar o meu coração

com um simples olhar,

com uma simples joia dos seus colares.

10Quão deliciosas são as suas carícias,

minha irmã, minha noiva!

Suas carícias são mais agradáveis que o vinho,

e a fragrância do seu perfume

supera o de qualquer especiaria!

11Os seus lábios gotejam a doçura

dos favos de mel, minha noiva;

leite e mel estão debaixo da sua língua.

A fragrância das suas vestes

é como a fragrância do Líbano.

12Você é um jardim fechado,

minha irmã, minha noiva;

você é uma nascente fechada,

uma fonte selada.

13De você brota um pomar de romãs

com frutos seletos,

com flores de hena e nardo,

14nardo e açafrão, cálamo e canela,

com todas as madeiras aromáticas,

mirra e aloés e as mais finas especiarias.

15Você é4.15 Ou Eu sou (na voz da Amada) uma fonte de jardim,

um poço de águas vivas,

que descem do Líbano.

A Amada

16Acorde, vento norte!

Venha, vento sul!

Soprem em meu jardim,

para que a sua fragrância

se espalhe ao seu redor.

Que o meu amado entre em seu jardim

e saboreie os seus deliciosos frutos.