Nyimbo ya Solomoni 4 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 4:1-16

Mwamuna

1Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga!

Ndithudi, ndiwe wokongola!

Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu.

Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi

zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.

2Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene,

zochokera kozisambitsa kumene.

Iliyonse ili ndi ana amapasa;

palibe imene ili yokha.

3Milomo yako ili ngati mbota yofiira;

pakamwa pako ndi pokongola kwambiri.

Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba

kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.

4Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide,

yomangidwa bwino ndi yosalala;

pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000,

zishango zonsezo za anthu ankhondo.

5Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala,

ngati ana amapasa a nswala

amene akudya pakati pa maluwa okongola.

6Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira

ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,

ndidzapita ku phiri la mure

ndi ku chitunda cha lubani.

7Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga;

palibe chilema pa iwe.

8Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga,

tiye tichoke ku Lebanoni,

utsikepo pa msonga ya Amana,

kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni,

kuchoka ku mapanga a mikango

ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.

9Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima,

iwe wanditenga mtima

ndi kapenyedwe ka maso ako,

ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.

10Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa!

Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo,

ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!

11Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi;

pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi.

Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.

12Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa;

ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.

13Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza;

muli zipatso zokoma kwambiri,

muli hena ndi nadi,

14nadi ndi safiro,

kalamusi ndi sinamoni,

komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino.

Mulinso mure ndi aloe

ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.

15Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda,

chitsime cha madzi oyenda,

mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.

Mkazi

16Dzuka, iwe mphepo yakumpoto,

ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera!

Uzira pa munda wanga,

kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse.

Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake

ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Cantares 4:1-16

El amado

1¡Cuán bella eres, amada mía!

¡Cuán bella eres!

Tus ojos, tras el velo, son dos palomas.

Tus cabellos son como los rebaños de cabras

que retozan en los montes de Galaad.

2Tus dientes son como ovejas recién trasquiladas,

que ascienden después de haber sido bañadas.

Cada una de ellas tiene su pareja;

ninguna de ellas está sola.

3Tus labios son cual cinta escarlata;

tus palabras me tienen hechizado.

Tus mejillas, tras el velo,

parecen dos mitades de granadas.

4Tu cuello se asemeja a la torre de David,

construida con piedras labradas;

de ella penden mil escudos,

escudos de guerreros todos ellos.

5Tus pechos parecen dos cervatillos,

dos crías mellizas de gacela

que pastan entre azucenas.

6Antes de que el día despunte

y se desvanezcan las sombras,

subiré a la montaña de la mirra,

a la colina del incienso.

7Toda tú eres bella, amada mía;

no hay en ti defecto alguno.

8Desciende del Líbano conmigo, novia mía;

desciende del Líbano conmigo.

Baja de la cumbre del Amaná,

de la cima del Senir y del Hermón.

Baja de las guaridas de los leones,

de los montes donde habitan los leopardos.

9Cautivaste mi corazón,

hermana y novia mía,

con una mirada de tus ojos;

con una vuelta de tu collar

cautivaste mi corazón.

10¡Cuán delicioso es tu amor,

hermana y novia mía!

¡Más agradable que el vino es tu amor,

y más que toda especia

la fragancia de tu perfume!

11Tus labios, novia mía, destilan miel;

leche y miel escondes bajo la lengua.

Cual fragancia del Líbano

es la fragancia de tus vestidos.

12Jardín cerrado eres tú,

hermana y novia mía;

¡jardín cerrado, sellado manantial!

13Tus pechos4:13 Tus pechos. Lit. Tus brotes. son un huerto de granadas

con frutos exquisitos,

con flores de nardo y azahar;

14con toda clase de árbol resinoso,4:14 resinoso. Lit. de incienso.

con nardo y azafrán,

con cálamo y canela,

con mirra y áloe,

y con las más finas especias.

15Eres fuente de los jardines,

manantial de aguas vivas,

¡arroyo que del Líbano desciende!

La amada

16¡Viento del norte, despierta!

¡Viento del sur, ven acá!

Soplad en mi jardín;

¡esparcid vuestra fragancia!

Que venga mi amado a su jardín

y pruebe sus frutos exquisitos.