Nyimbo ya Solomoni 3 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 3:1-11

1Usiku wonse ndili pa bedi langa

ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda;

ndinamufunafuna koma osamupeza.

2Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda,

mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake;

ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda.

Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.

3Alonda anandipeza

pamene ankayendera mzinda.

“Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”

4Nditawapitirira pangʼono

ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda.

Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke

mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,

mʼchipinda cha amene anandibereka.

5Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani

pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:

Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

6Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu

ngati utsi watolotolo,

wonunkhira mure ndi lubani,

zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?

7Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni,

choperekezedwa ndi asilikali 60,

anthu amphamvu a ku Israeli,

8onse atanyamula lupanga,

onse odziwa bwino nkhondo,

aliyense ali ndi lupanga pambali pake,

kukonzekera zoopsa za usiku.

9Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi;

anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.

10Milongoti yake anayipanga yasiliva,

kumbuyo kwake kwa golide.

Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo,

anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi

cha akazi a ku Yerusalemu.

11Tukulani inu akazi a ku Ziyoni

ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu,

chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka

pa tsiku la ukwati wake,

tsiku limene mtima wake unasangalala.

King James Version

Song of Solomon 3:1-11

1By night on my bed I sought him whom my soul loveth: I sought him, but I found him not. 2I will rise now, and go about the city in the streets, and in the broad ways I will seek him whom my soul loveth: I sought him, but I found him not. 3The watchmen that go about the city found me: to whom I said, Saw ye him whom my soul loveth? 4It was but a little that I passed from them, but I found him whom my soul loveth: I held him, and would not let him go, until I had brought him into my mother’s house, and into the chamber of her that conceived me. 5I charge you, O ye daughters of Jerusalem, by the roes, and by the hinds of the field, that ye stir not up, nor awake my love, till he please.

6¶ Who is this that cometh out of the wilderness like pillars of smoke, perfumed with myrrh and frankincense, with all powders of the merchant?

7Behold his bed, which is Solomon’s; threescore valiant men are about it, of the valiant of Israel. 8They all hold swords, being expert in war: every man hath his sword upon his thigh because of fear in the night. 9King Solomon made himself a chariot of the wood of Lebanon.3.9 a chariot: or, a bed 10He made the pillars thereof of silver, the bottom thereof of gold, the covering of it of purple, the midst thereof being paved with love, for the daughters of Jerusalem. 11Go forth, O ye daughters of Zion, and behold king Solomon with the crown wherewith his mother crowned him in the day of his espousals, and in the day of the gladness of his heart.