Nyimbo ya Solomoni 2 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 2:1-17

Mkazi

1Ine ndine duwa la ku Saroni,

duwa lokongola la ku zigwa.

Mwamuna

2Monga duwa lokongola pakati pa minga

ndi momwe alili wokondedwa wanga pakati pa atsikana.

Mkazi

3Monga mtengo wa apulosi pakati pa mitengo ya mʼnkhalango

ndi momwe alili bwenzi langa pakati pa anyamata.

Ndimakondwera kukhala pansi pa mthunzi wako,

ndipo chipatso chake ndi chokoma mʼkamwa mwanga.

4Iye wanditengera ku nyumba yaphwando,

ndipo mbendera yake yozika pa ine ndi chikondi.

5Undidyetse keke ya mphesa zowuma,

unditsitsimutse ndi ma apulosi,

pakuti chikondi chandifowoketsa.

6Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere,

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

7Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani

pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:

Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

8Tamverani bwenzi langa!

Taonani! Uyu akubwera apayu,

akulumphalumpha pa mapiri,

akujowajowa pa zitunda.

9Bwenzi langa ali ngati gwape kapena mwana wa mbawala.

Taonani! Uyo wayima kuseri kwa khoma lathulo,

akusuzumira mʼmazenera,

akuyangʼana pa mpata wa zenera.

10Bwenzi langa anayankha ndipo anati kwa ine,

“Dzuka bwenzi langa,

wokongola wanga, ndipo tiye tizipita.

11Ona, nyengo yozizira yatha;

mvula yatha ndipo yapitiratu.

12Maluwa ayamba kuoneka pa dziko lapansi;

nthawi yoyimba yafika,

kulira kwa njiwa kukumveka

mʼdziko lathu.

13Mtengo wankhuyu ukubereka zipatso zake zoyambirira;

mitengo ya mpesa ya maluwa ikutulutsa fungo lake.

Dzuka bwenzi langa, wokongola wanga

tiye tizipita.”

Mwamuna

14Nkhunda yanga yokhala mʼmingʼalu ya thanthwe,

mʼmalo obisala a mʼmbali mwa phiri,

onetsa nkhope yako,

nʼtamvako liwu lako;

pakuti liwu lako ndi lokoma,

ndipo nkhope yako ndi yokongola.

15Mutigwirire nkhandwe,

nkhandwe zingʼonozingʼono

zimene zikuwononga minda ya mpesa,

minda yathu ya mpesa imene yayamba maluwa.

Mkazi

16Bwenzi langa ndi wangadi ndipo ine ndine wake;

amadyetsa gulu lake la ziweto pakati pa maluwa okongola.

17Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira

ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,

unyamuke bwenzi langa,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena ngati mwana wa mbawala

pakati pa mapiri azigwembezigwembe.

Korean Living Bible

아가 2:1-17

1(여자) 나는 사론의 2:1 또는 ‘수선화’장미요 골짜기의 백합화라네.

2(남자) 내가 사랑하는 님을 다른 여자와 비교해 보니 가시나무 가운데 있는 백합화 같구나.

3(여자) 내가 사랑하는 사람을 다른 남자와 비교해 보니 숲속의 사과나무 같구나. 내가 그의 그늘에 앉아서 기뻐하며 그의 열매를 맛있게 먹는구나.

4그가 나를 데리고 연회장으로 들어가서 나에게 사랑의 기를 치켜올렸네.

5건포도로 내 힘을 회복시키고 사과로 나를 시원하게 해 다오. 내가 사랑 때문에 병이 들었단다.

6그가 나에게 그의 왼손을 베게 하고 오른손으로 나를 안는구나.

7예루살렘 여자들아, 내가 너희에게 2:7 원문에는 ‘노루와 들사슴으로’간절히 부탁한다. 제발 우리의 사랑을 방해하지 말아다오.

두 번째 노래

8(여자) 사랑하는 님의 목소리가 들리는구나. 그가 산을 넘고 들을 지나 달려온다.

9내 사랑하는 님은 노루와 어린 사슴 같구나. 그가 벽 뒤에 서서 창틈으로 들여다본다네.

10내 사랑하는 님이 말한다. (남자) 나의 사랑, 나의 님이여, 일어나 함께 갑시다.

11겨울도 지나고 비도 그쳤으며

12꽃이 피고 새가 노래하는 때가 되어 비둘기 소리가 들리고 있소.

13무화과가 맺히기 시작하고 포도나무가 꽃이 피어 향기를 날립니다. 나의 사랑, 나의 님이여, 일어나 함께 갑시다.

14바위 틈에 숨은 비둘기 같은 님이여, 그대의 사랑스런 얼굴을 보이고 그대의 아름다운 목소리를 들려 주오.

15여우를 잡아라. 포도원을 해치는 작은 여우를 잡아라. 우리의 포도원에 꽃이 피었다.

16(여자) 님은 나의 사랑, 나는 님의 사랑, 그가 백합화 가운데서 양떼를 먹이는구나.

17내 사랑하는 님이시여, 날이 새기 전, 어두움이 사라지기 전에 돌아와서 베델산의 노루와 어린 사슴처럼 되어 주세요.