Nyimbo ya Solomoni 2 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 2:1-17

Mkazi

1Ine ndine duwa la ku Saroni,

duwa lokongola la ku zigwa.

Mwamuna

2Monga duwa lokongola pakati pa minga

ndi momwe alili wokondedwa wanga pakati pa atsikana.

Mkazi

3Monga mtengo wa apulosi pakati pa mitengo ya mʼnkhalango

ndi momwe alili bwenzi langa pakati pa anyamata.

Ndimakondwera kukhala pansi pa mthunzi wako,

ndipo chipatso chake ndi chokoma mʼkamwa mwanga.

4Iye wanditengera ku nyumba yaphwando,

ndipo mbendera yake yozika pa ine ndi chikondi.

5Undidyetse keke ya mphesa zowuma,

unditsitsimutse ndi ma apulosi,

pakuti chikondi chandifowoketsa.

6Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere,

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

7Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani

pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:

Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

8Tamverani bwenzi langa!

Taonani! Uyu akubwera apayu,

akulumphalumpha pa mapiri,

akujowajowa pa zitunda.

9Bwenzi langa ali ngati gwape kapena mwana wa mbawala.

Taonani! Uyo wayima kuseri kwa khoma lathulo,

akusuzumira mʼmazenera,

akuyangʼana pa mpata wa zenera.

10Bwenzi langa anayankha ndipo anati kwa ine,

“Dzuka bwenzi langa,

wokongola wanga, ndipo tiye tizipita.

11Ona, nyengo yozizira yatha;

mvula yatha ndipo yapitiratu.

12Maluwa ayamba kuoneka pa dziko lapansi;

nthawi yoyimba yafika,

kulira kwa njiwa kukumveka

mʼdziko lathu.

13Mtengo wankhuyu ukubereka zipatso zake zoyambirira;

mitengo ya mpesa ya maluwa ikutulutsa fungo lake.

Dzuka bwenzi langa, wokongola wanga

tiye tizipita.”

Mwamuna

14Nkhunda yanga yokhala mʼmingʼalu ya thanthwe,

mʼmalo obisala a mʼmbali mwa phiri,

onetsa nkhope yako,

nʼtamvako liwu lako;

pakuti liwu lako ndi lokoma,

ndipo nkhope yako ndi yokongola.

15Mutigwirire nkhandwe,

nkhandwe zingʼonozingʼono

zimene zikuwononga minda ya mpesa,

minda yathu ya mpesa imene yayamba maluwa.

Mkazi

16Bwenzi langa ndi wangadi ndipo ine ndine wake;

amadyetsa gulu lake la ziweto pakati pa maluwa okongola.

17Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira

ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,

unyamuke bwenzi langa,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena ngati mwana wa mbawala

pakati pa mapiri azigwembezigwembe.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

雅歌 2:1-17

女子:

1我是沙仑平原的玫瑰花,

是谷中的百合花。

男子:

2我的爱人在众少女中,

就像荆棘中的一朵百合花。

女子:

3我的良人在众男子中,

好像林中的一棵苹果树。

我欢欢喜喜地坐在他的树荫下,

轻尝他香甜无比的果子。

4他带我走进宴席大厅,

众人都看见他对我充满柔情爱意。

5请用葡萄干来补充我的力气,

用苹果来提振我的精神,

因为我思爱成病。

6他的左手扶着我的头,

他的右手紧抱着我。

7耶路撒冷的少女啊!

我指着羚羊和田野的母鹿2:7 羚羊和田野的母鹿”在希伯来文中与“万军之全能上帝”发音相似。吩咐你们,

不要叫醒或惊动爱情,

等它自发吧。

8听啊!是我良人的声音,

他攀过高岗,跃过山丘,

终于来了!

9我的良人好像羚羊和幼鹿。

看啊,他就在墙外,

正从窗户往里观看,

从窗棂间往里窥视。

10他对我说:

“我的爱人,起来吧!

我的佳偶,跟我来!

11你看!冬天过去了,

雨水止住了。

12大地百花盛开,

百鸟争鸣的季节已经来临,

田野也传来斑鸠的叫声。

13无花果快成熟了,

葡萄树也开满了花,

散发着阵阵芬芳。

我的爱人,起来吧;

我的佳偶,跟我来。”

男子:

14我的鸽子啊,

你在岩石缝中,

在悬崖的隐秘处。

让我看看你的脸,

听听你的声音吧,

因为你的声音温柔,

你的脸庞秀丽。

15为我们抓住那些狐狸,

抓住那些破坏葡萄园的小狐狸吧,

因为我们的葡萄树正在开花。

女子:

16我的良人属于我,我也属于他。

他在百合花间牧放羊群。

17我的良人啊,

凉风吹起、日影飞逝的时候,

但愿你像比特山的羚羊和小鹿一样快快回来。