Nyimbo ya Solomoni 2 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 2:1-17

Mkazi

1Ine ndine duwa la ku Saroni,

duwa lokongola la ku zigwa.

Mwamuna

2Monga duwa lokongola pakati pa minga

ndi momwe alili wokondedwa wanga pakati pa atsikana.

Mkazi

3Monga mtengo wa apulosi pakati pa mitengo ya mʼnkhalango

ndi momwe alili bwenzi langa pakati pa anyamata.

Ndimakondwera kukhala pansi pa mthunzi wako,

ndipo chipatso chake ndi chokoma mʼkamwa mwanga.

4Iye wanditengera ku nyumba yaphwando,

ndipo mbendera yake yozika pa ine ndi chikondi.

5Undidyetse keke ya mphesa zowuma,

unditsitsimutse ndi ma apulosi,

pakuti chikondi chandifowoketsa.

6Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere,

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

7Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani

pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:

Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

8Tamverani bwenzi langa!

Taonani! Uyu akubwera apayu,

akulumphalumpha pa mapiri,

akujowajowa pa zitunda.

9Bwenzi langa ali ngati gwape kapena mwana wa mbawala.

Taonani! Uyo wayima kuseri kwa khoma lathulo,

akusuzumira mʼmazenera,

akuyangʼana pa mpata wa zenera.

10Bwenzi langa anayankha ndipo anati kwa ine,

“Dzuka bwenzi langa,

wokongola wanga, ndipo tiye tizipita.

11Ona, nyengo yozizira yatha;

mvula yatha ndipo yapitiratu.

12Maluwa ayamba kuoneka pa dziko lapansi;

nthawi yoyimba yafika,

kulira kwa njiwa kukumveka

mʼdziko lathu.

13Mtengo wankhuyu ukubereka zipatso zake zoyambirira;

mitengo ya mpesa ya maluwa ikutulutsa fungo lake.

Dzuka bwenzi langa, wokongola wanga

tiye tizipita.”

Mwamuna

14Nkhunda yanga yokhala mʼmingʼalu ya thanthwe,

mʼmalo obisala a mʼmbali mwa phiri,

onetsa nkhope yako,

nʼtamvako liwu lako;

pakuti liwu lako ndi lokoma,

ndipo nkhope yako ndi yokongola.

15Mutigwirire nkhandwe,

nkhandwe zingʼonozingʼono

zimene zikuwononga minda ya mpesa,

minda yathu ya mpesa imene yayamba maluwa.

Mkazi

16Bwenzi langa ndi wangadi ndipo ine ndine wake;

amadyetsa gulu lake la ziweto pakati pa maluwa okongola.

17Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira

ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,

unyamuke bwenzi langa,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena ngati mwana wa mbawala

pakati pa mapiri azigwembezigwembe.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Песнь Сулаймона 2:1-17

Она:

1– Я нарцисс Саронский,

лилия долин.

Он:

2– Как лилия между тёрнами,

так милая моя среди девушек.

Она:

3– Как яблоня среди лесных деревьев,

так возлюбленный мой среди юношей.

Сидеть в его тени мне наслаждение,

и плод его сладок для меня.

4Он привёл меня в дом пира,

и его знамя надо мной – любовь2:4 Или: «его желание ко мне – любовь»; или: «он посмотрел на меня с любовью»; или: «он поставил передо мной (на стол) любовь»..

5Подкрепи меня изюмом,

освежи меня яблоками,

ведь я изнемогаю от любви.

6Его левая рука под моей головой,

а правая обнимает меня.

7Дочери Иерусалима, заклинаю вас

газелями и полевыми ланями:

не будите и не возбуждайте любви,

пока она сама того не пожелает.

8Голос возлюбленного моего!

Вот идёт он,

перескакивая через горы,

перепрыгивая через холмы.

9Возлюбленный мой – как газель или молодой олень.

Вот стоит он за нашей стеной,

смотрит в окно,

заглядывает через решётку.

10Возлюбленный мой сказал мне:

«Вставай, любимая моя,

прекрасная моя, пойдём со мной!

11Смотри, зима уже прошла;

перестали лить дожди;

12появились цветы на земле;

настало время пения,

и раздаётся голос горлицы

в земле нашей;

13на инжире созревают плоды,

и цветущие виноградные лозы источают свой аромат.

Вставай, любимая моя,

прекрасная моя, пойдём со мной!»

Он:

14– Голубка моя далеко в ущелье скалы,

недосягаема, в пещере на склоне горы.

Позволь мне увидеть тебя

и услышать голос твой,

потому что сладок голос твой

и прекрасно лицо твоё.

15Поймайте нам лисиц,

лисят, которые портят виноградники,

а виноградники наши цветут.

Она:

16– Возлюбленный мой принадлежит мне, а я ему.

Среди лилий пасётся он2:16 Или: «пасёт он стадо своё»..

17Пока не наступил день

и не скрылись тени,

возвратись, возлюбленный мой,

скачи, словно газель

или молодой олень

на расселинах гор2:17 Или: «на горах Бетер»..