1Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
Mkazi
2Undipsompsone ndi milomo yako
chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
3Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino;
dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa.
Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
4Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire!
Mfumu indilowetse mʼchipinda chake.
Abwenzi
Ife timasangalala ndi kukondwera nawe,
tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo.
Mkazi
Amachita bwinotu potamanda iwe!
5Ndine wakuda, komatu ndine wokongola,
inu akazi a ku Yerusalemu,
ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara,
ngati makatani a tenti ya Solomoni.
6Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda,
ndine wakuda chifukwa cha dzuwa.
Alongo anga anandikwiyira
ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa;
munda wangawanga sindinawusamalire.
7Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako
ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana.
Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere
pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Abwenzi
8Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena,
ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa
ndipo udyetse ana ambuzi
pambali pa matenti a abusa.
Mwamuna
9Iwe bwenzi langa,
uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo,
khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11Tidzakupangira ndolo zagolide
zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Mkazi
12Pamene mfumu inali pa malo ake odyera,
mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine,
kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira,
ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
Mwamuna
15Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi!
Ndithu, ndiwe chiphadzuwa,
maso ako ali ngati nkhunda.
Mkazi
16Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi!
Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri!
Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Mwamuna
17Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza,
phaso lake ndi la mtengo wa payini.