Nyimbo ya Solomoni 1 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 1:1-17

1Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.

Mkazi

2Undipsompsone ndi milomo yako

chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.

3Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino;

dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa.

Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!

4Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire!

Mfumu indilowetse mʼchipinda chake.

Abwenzi

Ife timasangalala ndi kukondwera nawe,

tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo.

Mkazi

Amachita bwinotu potamanda iwe!

5Ndine wakuda, komatu ndine wokongola,

inu akazi a ku Yerusalemu,

ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara,

ngati makatani a tenti ya Solomoni.

6Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda,

ndine wakuda chifukwa cha dzuwa.

Alongo anga anandikwiyira

ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa;

munda wangawanga sindinawusamalire.

7Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako

ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana.

Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere

pambali pa ziweto za abwenzi ako?

Abwenzi

8Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena,

ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa

ndipo udyetse ana ambuzi

pambali pa matenti a abusa.

Mwamuna

9Iwe bwenzi langa,

uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.

10Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo,

khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.

11Tidzakupangira ndolo zagolide

zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.

Mkazi

12Pamene mfumu inali pa malo ake odyera,

mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.

13Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine,

kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.

14Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira,

ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.

Mwamuna

15Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi!

Ndithu, ndiwe chiphadzuwa,

maso ako ali ngati nkhunda.

Mkazi

16Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi!

Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri!

Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.

Mwamuna

17Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza,

phaso lake ndi la mtengo wa payini.