Nyimbo ya Solomoni 1 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 1:1-17

1Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.

Mkazi

2Undipsompsone ndi milomo yako

chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.

3Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino;

dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa.

Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!

4Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire!

Mfumu indilowetse mʼchipinda chake.

Abwenzi

Ife timasangalala ndi kukondwera nawe,

tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo.

Mkazi

Amachita bwinotu potamanda iwe!

5Ndine wakuda, komatu ndine wokongola,

inu akazi a ku Yerusalemu,

ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara,

ngati makatani a tenti ya Solomoni.

6Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda,

ndine wakuda chifukwa cha dzuwa.

Alongo anga anandikwiyira

ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa;

munda wangawanga sindinawusamalire.

7Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako

ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana.

Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere

pambali pa ziweto za abwenzi ako?

Abwenzi

8Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena,

ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa

ndipo udyetse ana ambuzi

pambali pa matenti a abusa.

Mwamuna

9Iwe bwenzi langa,

uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.

10Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo,

khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.

11Tidzakupangira ndolo zagolide

zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.

Mkazi

12Pamene mfumu inali pa malo ake odyera,

mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.

13Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine,

kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.

14Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira,

ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.

Mwamuna

15Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi!

Ndithu, ndiwe chiphadzuwa,

maso ako ali ngati nkhunda.

Mkazi

16Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi!

Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri!

Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.

Mwamuna

17Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza,

phaso lake ndi la mtengo wa payini.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Песнь Сулеймана 1:1-16

1Лучшая из песен Сулеймана.

Она:

– Целуй меня, целуй устами своими,

ведь любовь твоя отрадней вина,

2приятней аромата благовоний твоих.

Имя твоё подобно разлитому благовонию,

поэтому девушки любят тебя.

3Веди меня за собой – давай убежим!

О мой царь, введи меня в чертоги свои!

Молодые женщины:

– Будем радоваться и восхищаться тобой,

превыше вина вознесём мы любовь твою.

Она:

– По праву девушки любят тебя!

4Дочери Иерусалима,

Я черна, как шатры Кедара,

но прекрасна, словно завесы Сулеймана.

5Не смотрите, что я так смугла,

ведь солнце опалило меня.

Мои братья разгневались на меня

и заставили меня ухаживать за виноградниками;

своим виноградником я пренебрегла.

6Скажи мне, возлюбленный, где пасёшь ты стадо своё

и где покоишь ты овец своих в полдень?

Зачем мне искать тебя, бродя, как блудница1:6 Букв.: «Зачем мне быть как бы покрытой (покрывалом)». Эти слова можно понять двояко: молодая женщина, разыскивая своего жениха, боится показаться блудницей (ср. Нач. 38:14-15), или, что в разлуке со своим возлюбленным женщина покроет свою голову в знак сильной печали (ср. 2 Цар. 15:30).,

среди стад твоих друзей?

Молодые женщины:

7– Если ты не знаешь, прекраснейшая из женщин,

то иди по следам овец

и паси козлят своих

у шатров пастушеских.

Он:

8– Милая моя, я уподобил тебя кобылице,

запряжённой в колесницу фараона.

9Прекрасны щёки твои под украшениями,

и шея твоя в ожерельях.

10Мы сделаем тебе украшения из золота,

оправленные серебром.

Она:

11– Пока царь был за столом своим,

благовония мои источали свой аромат.

12Мой возлюбленный, как мешочек мирры1:12 Мирра (смирна) – приятно пахнущая смола растущего в Аравии растения.,

покоится между грудей моих.

13Мой возлюбленный словно кисть киперовых1:13 Кипер – растение семейства дербенниковых, белые цветы которого источают сильный аромат. Из этого растения и по сей день изготовляют хну. Также в 4:13. цветов

в виноградниках Ен-Геди.

Он:

14– Как прекрасна ты, милая моя,

как прекрасна!

Глаза твои словно голуби.

Она:

15– Как красив ты, милый мой,

как красив!

И ложе наше – зелёный покров.

Он:

16– Брусья дома нашего – кедры,

навес наш – кипарисы.