Numeri 6 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 6:1-27

Za Mnaziri

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri, 3sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma. 4Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’

5“ ‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’ 6Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo. 7Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake. 8Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.

9“Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri. 10Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano. 11Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake. 12Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.

13“Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano. 14Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano, 15ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.

16“Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza. 17Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.

18“Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.

19“Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija. 20Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.

21“Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”

Kupereka Mdalitso

22Yehova anawuza Mose kuti, 23“Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,

24“ ‘Yehova akudalitse

ndi kukusunga;

25Yehova awalitse nkhope yake pa iwe,

nakuchitira chisomo;

26Yehova akweze nkhope yake pa iwe,

nakupatse mtendere.’ ”

27Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

民數記 6:1-27

拿細耳人的條例

1耶和華對摩西說: 2「你把以下條例告訴以色列人。

「無論男女,如果許願做拿細耳人,把自己獻給耶和華, 3就要禁戒淡酒和烈酒、淡酒或烈酒做的醋、葡萄汁、葡萄和葡萄乾。 4在做拿細耳人期間,葡萄樹所結的,包括葡萄核和葡萄皮,都不可吃。 5在許願做拿細耳人期間,不可用剃刀剃頭,要任由頭髮生長,要保持聖潔,一直到獻給耶和華的日期滿了。 6在獻給耶和華期間,不可挨近死屍, 7即使父母或是兄弟姊妹死了,也不可挨近,以免沾染不潔,因為他頭上有將自己奉獻給上帝的記號。 8在做拿細耳人期間,他是奉獻給耶和華的人。 9如果有人在他身邊暴斃,使他的頭髮沾染不潔,他要等到第七天潔淨的日子剃掉頭髮。 10第八天,他要帶兩隻斑鳩或雛鴿到會幕門口交給祭司。 11祭司要獻一隻作贖罪祭,另一隻作燔祭,為他碰過死屍贖罪。他要在當日使頭聖潔, 12重新開始過奉獻給耶和華的日子,還要帶一隻一歲的公羊羔作贖過祭。他以前做拿細耳人的日子無效,因為他沾染了不潔之物。

13「獻給耶和華的日子期滿後,拿細耳人要遵行以下條例。他要被帶到會幕門口, 14在那裡獻給耶和華一隻毫無殘疾、一歲的公羊羔作燔祭,一隻毫無殘疾、一歲母羊羔作贖罪祭,一隻毫無殘疾的公綿羊作平安祭, 15一籃調油的無酵細麵餅和塗油的無酵薄餅,以及素祭和奠祭。 16祭司要把這些祭物帶到耶和華面前,為他獻上贖罪祭和燔祭, 17然後把公綿羊和無酵餅獻給耶和華作平安祭,再獻上素祭和奠祭。 18拿細耳人要在會幕門口剃掉作為奉獻記號的頭髮,把頭髮放在平安祭的火裡燒掉。 19拿細耳人剃頭以後,祭司要取出一條煮好的公綿羊前腿,再從籃中拿出一塊無酵餅和一塊無酵薄餅,放在拿細耳人手中。 20然後,祭司要把這些祭物作為搖祭在耶和華面前搖一搖。這些祭物與作搖祭的胸肉和作舉祭的腿肉一樣,都是歸給祭司的聖物。此後,拿細耳人便可以喝酒。

21「以上是許願獻供物給耶和華的拿細耳人當守的條例和當獻的祭物。但如果他額外許願獻上力所能及之物,就必須還所許的願。」

祭司的祝福

22耶和華對摩西說: 23「你告訴亞倫父子們要這樣為以色列人祝福, 24『願耶和華賜福給你,保護你; 25願耶和華笑顏垂顧你,施恩給你; 26願耶和華恩待你,賜你平安。』 27他們要奉我的名為以色列人祝福,我必賜福給他們。」