Numeri 6 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 6:1-27

Za Mnaziri

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri, 3sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma. 4Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’

5“ ‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’ 6Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo. 7Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake. 8Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.

9“Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri. 10Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano. 11Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake. 12Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.

13“Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano. 14Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano, 15ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.

16“Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza. 17Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.

18“Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.

19“Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija. 20Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.

21“Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”

Kupereka Mdalitso

22Yehova anawuza Mose kuti, 23“Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,

24“ ‘Yehova akudalitse

ndi kukusunga;

25Yehova awalitse nkhope yake pa iwe,

nakuchitira chisomo;

26Yehova akweze nkhope yake pa iwe,

nakupatse mtendere.’ ”

27Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.

Bibelen på hverdagsdansk

4. Mosebog 6:1-27

Forskrifter for naziræerne

1Herren sagde til Moses: 2„Sig til Israels folk, at hvis en mand eller en kvinde aflægger naziræerløftet og således indvier sig til Herren på en særlig måde, 3-4må de, så længe de er bundet af deres løfte, hverken drikke øl eller vin—ikke engang druesaft—og de må heller ikke spise druer eller rosiner. De må ikke nyde noget, der har med vindruer at gøre—ikke engang kernerne eller skrællerne.

5I den periode løftet gælder, må de ikke lade deres hår klippe, for de er helliget og indviet til Herren. Derfor skal de lade håret vokse.

6-7I den periode løftet gælder, må de ikke komme i nærheden af lig—heller ikke, hvis det drejer sig om deres forældre eller søskende, for de er indviet til Gud på en særlig måde— 8de er naziræere og helliget Herren. 9Men hvis nogen falder død om, så de ikke kan undgå at røre ved den døde, så de bliver urene, skal de være urene i syv dage og derefter lade deres hår klippe af. Da vil de være renset for deres urenhed. 10Næste dag skal de så bringe to turtelduer eller to unge duer til præsten ved åbenbaringsteltets indgang, 11og præsten skal ofre den ene due som syndoffer og den anden som brændoffer, så der skaffes soning for deres urenhed. Først da kan de aflægge løfte på ny og lade håret vokse igen. 12Den del af løftet, som blev opfyldt, før de blev urene, tæller ikke længere. Nej, de må begynde forfra og aflægge et nyt løfte. Samtidig skal de ofre et etårs vædderlam som skyldoffer.

13Når de har opfyldt deres naziræerløfte, og indvielsestiden er udløbet, skal de gå hen til åbenbaringsteltets indgang 14og ofre et etårs vædderlam uden skavanker som brændoffer til Herren. De skal desuden ofre et tilsvarende gimmerlam som syndoffer, et takoffer bestående af en vædder uden skavanker, 15en kurv med usyrnede brød, dels ringbrød lavet af fint mel blandet med olivenolie, dels fladbrød penslet med olivenolie, samt de sædvanlige afgrøde- og drikofre. 16Da skal præsten bringe ofrene til Herren i denne rækkefølge: syndofferet først, så brændofferet 17og takoffervædderen sammen med de usyrnede brød—og endelig afgrødeofferet og drikofferet.

18Derefter skal naziræerne ved åbenbaringsteltets indgang klippe deres hår, for det lange hår var tegnet på, at de havde indviet sig på en særlig måde til Herren, og de skal ofre håret på alteret sammen med takofferet. 19Efter at de har klippet håret af, skal præsten tage vædderens kogte bov, et usyrnet ringbrød og et usyrnet fladbrød fra kurven og lægge disse ting i deres hænder. 20Så skal præsten svinge det foran Herrens alter som et offer til Herren. Denne del af offeret tilfalder præsten sammen med bryststykket og låret, der blev svunget foran Herrens alter. Derefter kan naziræerne drikke vin igen, for de er løst fra deres løfte.

21Det er forskrifterne for naziræerløftet og de påkrævede ofre, efter at løftet er opfyldt. Ud over disse ofre skal de naturligvis bringe de ofre, de eventuelt måtte have lovet Herren, da de aflagde deres naziræerløfte.”

Den aronitiske velsignelse

22Herren sagde til Moses: 23„Sig til Aron og hans sønner, at de skal velsigne Israels folk på følgende måde: 24-26Herren velsigne dig og bevare dig. Herren våge over dig og være dig nådig. Herren være dig nær og give dig fred. 27Aron og hans sønner skal med denne velsignelse stemple mit navn på Israels folk—og jeg vil velsigne dem.”