Numeri 5 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 5:1-31

Ukhondo wa pa Msasa

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa. 3Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.” 4Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.

Kukonza Zolakwika

5Yehova anati kwa Mose, 6“Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo 7ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo. 8Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake. 9Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo. 10Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’ ”

Mkazi Wosakhulupirika

11Kenaka Yehova anawuza Mose kuti, 12“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, 13nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita), 14mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse, 15apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’ ”

16“ ‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova. 17Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano. 18Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’ 19Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke. 20Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’ 21pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako. 22Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’ ”

“Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’ ”

23“ ‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja. 24Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa. 25Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe. 26Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja. 27Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake. 28Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.

29“ ‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake, 30kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo. 31Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’ ”

New International Reader’s Version

Numbers 5:1-31

Making the Camp Pure

1The Lord spoke to Moses. He said, 2“Tell the Israelites that certain people must be sent away from the camp. Command them to send away anyone who has a skin disease. They must send away all those who have liquid waste coming from their bodies. And they must send away those who are ‘unclean’ because they have touched a dead body. 3That applies to men and women alike. Send them out of the camp. They must not make their camp ‘unclean.’ That is where I live among them.” 4So the Israelites did what the Lord commanded. They sent out of the camp those who were “unclean.” They did just as the Lord had directed Moses.

Sins Against Others Must Be Paid For

5The Lord said to Moses, 6“Speak to the Israelites. Say to them, ‘Suppose a man or woman does something wrong to someone else. Then that person is not being faithful to the Lord. People like that are guilty. 7They must admit they have committed a sin. They must pay in full for what they did wrong. And they must add a fifth of the value to it. Then they must give all of it to the person they have sinned against. 8But suppose that person has died. And suppose that person does not have a close relative who can be paid for the sin that was committed. Then what is paid belongs to the Lord. It must be given to the priest. A ram must be given along with it. The ram must be sacrificed to the Lord to pay for the sin. 9All the sacred gifts the Israelites bring to a priest will belong to him. 10Sacred gifts belong to their owners. But what they give to the priest will belong to the priest.’ ”

The Test for an Unfaithful Wife

11Then the Lord spoke to Moses again. He said, 12“Speak to the Israelites. Say to them, ‘Suppose a man’s wife goes astray. And suppose she is not faithful to her husband. 13Suppose another man has sex with her. And suppose this is hidden from her husband. No one knows she is not “clean.” So there is no witness against her. And she has not been caught in the act. 14Suppose her husband becomes jealous. He does not trust his wife, and she is really “unclean.” Or suppose he does not trust her even though she is “clean.” 15Then he must take his wife to the priest. He must also bring an offering. It must be eight cups of barley flour. The offering is for his wife. He must not pour olive oil on it. And he must not put incense on it. It is a grain offering for being jealous. It calls attention to the wrong thing a person has done.

16“ ‘The priest must have her stand in front of the Lord. 17He must pour some holy water into a clay jar. He must get some dust from the floor of the holy tent. And he must put it into the water. 18The priest must have the woman stand in front of the Lord. Then he must untie her hair. He must place in her hands the offering that calls attention to the wrong thing a person has done. It is the grain offering for being jealous. The priest must keep the bitter water with him. It is the water that brings a curse. 19Then the priest must have the woman give her word. He must say to her, “Suppose no other man has had sex with you. And suppose you haven’t gone astray. You have kept yourself pure while you are married to your husband. Then may the bitter water that brings a curse not harm you. 20But suppose you have gone astray while you are married to your husband. You have made yourself ‘unclean.’ You have had sex with a man who isn’t your husband.” 21At that point the priest must put the woman under the curse that will come if she breaks her word. He must say, “May the Lord cause you to become a curse among your people. You will become a curse when the Lord makes your body unable to have children. 22May this water that brings a curse enter your body. May it make your body unable to have children.”

“ ‘Then the woman must say, “Amen. Let it happen.”

23“ ‘The priest must write the curses on a scroll. He must wash them off in the bitter water. 24It is the water he will make the woman drink. It is bitter water that brings a curse. It will enter her body. And it will cause her to suffer bitterly. 25The priest must take from her hands the grain offering for being jealous. He must lift it up and wave it in front of the Lord. He must bring it to the altar. 26Then the priest must take a handful of the grain offering. It is the offering that calls attention to the wrong thing a person has done. The priest must burn it on the altar. After that, he must have the woman drink the water. 27Suppose she has made herself “unclean.” She has not been faithful to her husband. And she has drunk the water that brings a curse. Then it will go into her body. It will cause her to suffer bitterly. It will make her body unable to have children. She will become a curse. 28Suppose the woman has not made herself “unclean.” But suppose she is “clean.” Then she will be free of guilt. And she will be able to have children.

29“ ‘This is the law about being jealous. It applies to a woman who has gone astray. She has made herself “unclean” while she is married to her husband. 30And it applies to a man who becomes jealous. He has doubts about his wife. The priest must have her stand in front of the Lord. He must apply the entire law to her. 31The husband will not be guilty of doing anything wrong. But the woman will be punished for her sin.’ ”