Numeri 4 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 4:1-49

Akohati

1Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni: 2“Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo. 3Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.

4“Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri. 5Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni. 6Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.

7“Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse. 8Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.

9“Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta. 10Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.

11“Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.

12“Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.

13“Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake. 14Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.

15“Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.

16“Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”

17Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti, 18“Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi. 19Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula. 20Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”

Ageresoni

21Yehova anawuza Mose kuti, 22“Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo. 23Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.

24“Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi: 25Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano, 26makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi. 27Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira. 28Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.

Amerari

29“Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo. 30Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano. 31Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde, 32ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita. 33Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”

Chiwerengero cha Fuko la Levi

34Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 35Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano, 36atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750. 37Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.

38Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 39Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano, 40atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630. 41Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.

42Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 43Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano, 44atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200. 45Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.

46Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 47Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano 48analipo 8,580. 49Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose.

Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.

O Livro

Números 4:1-49

Os coatitas

1Então o Senhor disse a Moisés e a Aarão: 2“Tomem a soma do grupo familiar de Coate, da tribo de Levi. 3Serão contados todos os do sexo masculino, entre 30 e 50 anos, capazes de trabalharem na tenda do encontro.

4Estes são os seus deveres quanto às coisas santas: 5Quando o acampamento for chamado a deslocar-se, Aarão e os filhos entrarão primeiramente na tenda do encontro e descerão o véu, cobrindo a arca do testemunho com ele. 6Seguidamente, cobrirão o próprio véu com a coberta de peles de couro fino4.6 Acerca deste tipo de pele, o termo hebraico tem significado incerto. Pode significar couro à base de pele de um animal mamífero marinho, provavelmente o dugongo, ou significar um tipo fino e duradouro de couro à base de animais que foram domesticados. e, sobre esta, um pano azul. Porão ainda as varas na arca.

7Depois deverão estender igualmente um pano azul sobre a mesa, na qual está exposto o pão da Presença, e colocarão os pratos, as colheres, as taças, os jarros, e também o pão sobre esse tecido. Porão em cima disso tudo um pano carmesim; 8e finalmente uma coberta pele de couro fino. Então enfiarão as varas de transporte nos lados da mesa.

9Depois disso, cobrirão o candelabro com um pano azul, assim como as lâmpadas, os apagadores, os espevitadores e o reservatório de azeite. 10Todo este conjunto de objetos será depois coberto com peles de couro fino, feito o seu acondicionamento, será colocado sobre uma armação, para ser transportado.

11Deverão depois estender um pano azul sobre o altar de ouro, cobri-lo com uma pele de couro fino, e pôr as varas nos seus cantos.

12Todos os outros utensílios do tabernáculo deverão ser acondicionados num tecido azul, cobertos com pele de couro fino, e postos numa armação de transporte.

13Hão de ser tiradas as cinzas do altar e este será coberto com um pano de púrpura. 14Todos os utensílios do altar devem ficar sobre ele; braseiros, garfos, pás, bacias e outros recipientes, e uma coberta de peles de couro fino, estendida sobre eles. Finalmente, as varas de transporte serão enfiadas lateralmente, nos seus lugares.

15Quando Aarão e os seus filhos tiverem terminado esta tarefa, os homens de Coate chegar-se-ão e carregarão os embrulhos, levando-os para onde o acampamento se deslocar. Mas não deverão tocar nos objetos sagrados, senão morrerão. Esta é portanto a sagrada tarefa dos descendentes de Coate na tenda do encontro.

16Eleazar, filho de Aarão, terá a responsabilidade do azeite para a iluminação, do incenso aromático, da oferta diária de cereais, do azeite da unção; na realidade, terá até a supervisão de todo o tabernáculo; tudo ali estará à sua responsabilidade.”

17Então o Senhor disse a Moisés e a Aarão: 18“Atenção que as famílias dos coatitas não se destruam a si mesmas! 19Para que eles não morram quando transportam as coisas santas, farás o seguinte: Aarão e os seus filhos entrarão e indicarão a cada um o que deve transportar. 20No entanto, eles nunca deverão entrar no santuário, nem sequer por um momento, nem olhar para os objetos sagrados; senão morrerão.”

Os gersonitas

21Disse mais o Senhor a Moisés: 22“Toma o número dos gersonitas da tribo de Levi 23todos os homens entre 30 e 50 anos, capazes para o trabalho sagrado com a tenda do encontro. 24Serão estas as suas funções: 25levarão as cortinas do tabernáculo, mais propriamente o conjunto da tenda do encontro, com as cobertas, as peles de couro fino, a cortina da porta; 26e ainda as cortinas do pátio e as da entrada deste; também deverão transportar as suas cordas e todos os acessórios respetivos. 27São plenamente responsáveis por tudo isto que foi referido. Aarão ou os seus filhos deverão indicar-lhes as tarefas; 28mas os gersonitas serão diretamente responsáveis perante Itamar, sacerdote, filho de Aarão.

Os meraritas

29Agora, conta os homens do grupo das famílias descendentes de Merari, da tribo de Levi, 30entre 30 e 50 anos, capazes para o serviço da tenda do encontro. 31Quando a tenda do encontro tiver de ser deslocada, deverão transportar toda a armação, as bases, 32as tábuas, assim como a estrutura envolvente do pátio, com as suas bases, estacas, cordas, e tudo o resto que esteja relacionado com isso e que sirva para a sua conservação. Distribui as tarefas por cada homem, notando o seu nome. 33A divisão de Merari será igualmente responsável perante Itamar, filho de Aarão.”

As divisões de levitas são contadas

34Moisés, Aarão e os outros chefes tomaram o número dos homens da divisão de Coate, 35dos que tinham entre 30 e 50 anos, capazes para o serviço da tenda do encontro; 36e acharam que havia um total de 2750. 37Tudo isto foi feito para dar cumprimento às instruções do Senhor a Moisés.

38-48Idêntica contagem foi feita à divisão de Gerson, totalizando 2630 indivíduos. Quanto à de Merari, contaram-se 3200.

Moisés, Aarão e os chefes de Israel acharam que todos os levitas entre 30 e 50 anos, aptos para o serviço da tenda do encontro e para o seu transporte, constituíam um total de 8580 pessoas. 49Este censo foi realizado em resposta às ordens do Senhor a Moisés, o qual indicou para cada um a sua função e o que devia transportar.