Numeri 4 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 4:1-49

Akohati

1Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni: 2“Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo. 3Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.

4“Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri. 5Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni. 6Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.

7“Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse. 8Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.

9“Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta. 10Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.

11“Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.

12“Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.

13“Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake. 14Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.

15“Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.

16“Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”

17Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti, 18“Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi. 19Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula. 20Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”

Ageresoni

21Yehova anawuza Mose kuti, 22“Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo. 23Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.

24“Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi: 25Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano, 26makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi. 27Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira. 28Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.

Amerari

29“Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo. 30Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano. 31Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde, 32ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita. 33Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”

Chiwerengero cha Fuko la Levi

34Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 35Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano, 36atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750. 37Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.

38Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 39Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano, 40atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630. 41Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.

42Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 43Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano, 44atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200. 45Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.

46Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 47Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano 48analipo 8,580. 49Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose.

Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.

Священное Писание

Числа 4:1-49

Обязанности каафитов

1Вечный сказал Мусе и Харуну:

2– Сделай перепись каафитской ветви левитов по кланам и семьям. 3Исчисли всех мужчин от тридцати до пятидесяти лет, которые смогут работать при шатре встречи.

4Вот служба каафитов при шатре встречи: пусть они заботятся о самой священной утвари. 5Когда лагерю нужно будет трогаться в путь, пусть Харун и его сыновья войдут, снимут закрывающую завесу и покроют ею сундук соглашения. 6Пусть они положат на завесу кожу дюгоней4:6 Дюгонь – водное млекопитающее отряда сирен, обитающее в Красном море., расстелют сверху развёрнутое голубое покрывало и вложат шесты.

7Пусть они расстелют над столом для священного хлеба голубое покрывало и положат на него тарелки, блюда, чаши и кувшины для жертвенных возлияний. Хлеб, который постоянно лежит там, пусть там и остаётся. 8Над ними пусть они расстелют алое покрывало, покроют его кожей дюгоней и вложат шесты.

9Пусть они возьмут голубое покрывало и покроют светильник с его лампадами, щипцами для фитилей, лотками для нагара и всеми сосудами для масла, из которых его заправляют. 10Пусть они завернут его со всей утварью в покров из кожи дюгоней и положат на носилки.

11Над золотым жертвенником пусть они расстелют голубое покрывало, покроют его кожей дюгоней и вложат шесты.

12Пусть они возьмут всю утварь, которой пользуются для служения в святилище, завернут её в голубое покрывало, покроют кожей дюгоней и положат на носилки.

13Пусть они сметут пепел с бронзового жертвенника, расстелют на жертвеннике пурпурное покрывало 14и положат на него всю утварь, которой пользуются для служения при жертвеннике: противни, вилки для мяса, лопатки и кропильные чаши. Пусть они расстелют над ним покров из кожи дюгоней и вложат шесты.

15Когда лагерю нужно будет трогаться в путь, после того как Харун и его сыновья закончат покрывать святилище и его утварь, пусть каафиты придут, чтобы нести всё это. Им нельзя прикасаться к самим священным вещам, иначе они умрут. Это утварь шатра встречи, которую будут носить каафиты.

16Пусть Элеазар, сын священнослужителя Харуна, заботится о масле для посвящения, благовониях, постоянном хлебном приношении и масле для помазания. Пусть он заботится о священном шатре и обо всём, что в нём: о святилище и его утвари.

17Вечный сказал Мусе и Харуну:

18– Не дайте погибнуть левитскому клану каафитов. 19Чтобы они жили и не умерли, приближаясь к великим святыням, сделайте для них вот что: пусть Харун и его сыновья входят в святилище и назначают каждому его службу и что ему нести. 20Но сами они пусть не входят, чтобы посмотреть на святыни даже на миг, иначе они умрут.

Обязанности гершонитов

21Вечный сказал Мусе:

22– Ещё сделай перепись гершонитов по семьям и кланам. 23Исчисли всех мужчин от тридцати до пятидесяти лет, которые могут служить при шатре встречи.

24Вот служба гершонитских кланов, когда они трудятся и носят тяжести: 25пусть несут покрывала священного шатра – шатра встречи, – его покрытие и внешнее покрытие из кож дюгоней, завесы к входу в шатёр встречи, 26завесы двора вокруг священного шатра и жертвенника, завесу к входу, верёвки и все принадлежности к ним. Пусть они делают всё то, что с этим положено делать. 27Вся их служба – переноска или другая работа – пусть совершается под руководством Харуна и его сыновей. Доверьте их заботе всё, что они должны нести. 28Такова служба гершонитских кланов при шатре встречи. Пусть они исполняют свои обязанности под началом Итамара, сына священнослужителя Харуна.

Обязанности мераритов

29Исчисли мераритов по кланам и семьям. 30Исчисли всех мужчин от тридцати до пятидесяти лет, которые могут служить при шатре встречи. 31Вот их обязанность по службе при шатре встречи: пусть несут брусья священного шатра, его поперечины, столбы и основания, 32а ещё столбы окружающего двора с их основаниями, колья священного шатра, верёвки, все принадлежности к ним и оснастку. Определи каждому, что именно ему нести. 33Такова служба мераритских кланов, которую они должны исполнять при шатре встречи под началом Итамара, сына священнослужителя Харуна.

Исчисление левитских кланов

34Муса, Харун и вожди народа исчислили каафитов по кланам и семьям. 35Всех мужчин от тридцати до пятидесяти лет, годных служить при шатре встречи, 36которых исчислили по кланам, было две тысячи семьсот пятьдесят человек. 37Это общее число всех, кто в каафитских кланах служил при шатре встречи. Муса и Харун исчислили их по повелению Вечного, данному через Мусу.

38Гершониты были исчислены по кланам и семьям. 39Всех мужчин от тридцати до пятидесяти лет, годных служить при шатре встречи, 40которых исчислили по кланам и семьям, было две тысячи шестьсот тридцать человек. 41Это общее число всех, кто в гершонитских кланах служил при шатре встречи. Муса и Харун исчислили их по повелению Вечного.

42Мерариты были исчислены по кланам и семьям. 43Всех мужчин от тридцати до пятидесяти лет, годных служить при шатре встречи, 44которых исчислили по кланам, было три тысячи двести человек. 45Это их общее число в мераритских кланах. Муса и Харун исчислили их по повелению Вечного, данному через Мусу.

46Муса, Харун и вожди Исраила исчислили всех левитов по кланам и семьям. 47Всех мужчин от тридцати до пятидесяти лет, годных совершать служение при шатре встречи и нести его, 48было восемь тысяч пятьсот восемьдесят человек. 49По повелению Вечного, данному через Мусу, каждому из них назначили его службу и сказали, что нести.

Они были исчислены, как повелел через Мусу Вечный.