Numeri 36 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 36:1-13

Cholowa cha Ana Aakazi a Zelofehadi

1Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli. 2Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi. 3Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa. 4Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”

5Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona. 6Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo 7kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake. 8Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake. 9Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”

10Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose. 11Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo. 12Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.

13Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.

O Livro

Números 36:1-13

A herança das filhas de Zelofeade

(Nm 27.1-11)

1Então os principais responsáveis de agregado de Gileade, do subgrupo de Maquir, da tribo de Manassés, um dos filhos de José, veio ter com Moisés e os demais chefes de Israel, com esta petição: 2“O Senhor deu-vos instruções para repartirem a terra pelo povo de Israel, por sorteio, e dar a parte do nosso familiar Zelofeade às suas filhas. 3Mas se elas casarem dentro de outra tribo, a terra delas irá com elas para ser incorporada na tribo dentro da qual casarem, 4incorporação que ficará definitiva com o ano de jubileu. Desta forma, a área total da nossa tribo ficará reduzida.”

5Então Moisés respondeu diante de toda a gente, e deu as seguintes instruções da parte do Senhor: “Os homens da tribo de José apresentam um requerimento justo. 6Isto é, portanto, o que o Senhor disse mais quanto ao caso das filhas de Zelofeade: que elas casem com quem quiserem, mas que seja sempre dentro da sua própria tribo. 7Desta forma, nenhuma fração de terra de uma tribo passará para outra tribo, visto que a herança recebida por cada tribo deverá ficar inalterada, como foi originalmente distribuída. 8Portanto, toda a rapariga, sendo ela a herdeira, deverá casar na sua própria tribo, para que a terra que lhe pertence não venha a agregar-se a outra tribo. 9Desta forma as heranças não passarão duma tribo para outra e as tribos israelitas poderão continuar sempre ligadas cada uma à sua herança.”

10As filhas de Zelofeade fizeram como o Senhor ordenara a Moisés. 11Estas raparigas, Mala, Tirza, Hogla, Milca e Noa, casaram-se com seus primos, filhos de tios paternos, 12da descendência de Manassés, filho de José, de forma que a herança dessa tribo não foi alterada.

13Estes são os mandamentos e os regulamentos que o Senhor deu ao povo de Israel através de Moisés, enquanto estavam acampados nas planícies de Moabe, nas margens do rio Jordão, em frente de Jericó.