Numeri 34 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 34:1-29

Malire a Dziko la Kanaani

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:

3“ ‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere. 4Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni, 5kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.

6“ ‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.

7“ ‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori 8ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi, 9ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.

10“ ‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu. 11Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti. 12Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere.

“ ‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’ ”

13Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka, 14chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo. 15Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”

16Yehova anawuza Mose kuti, 17“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni. 18Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo. 19Mayina awo ndi awa:

Kalebe mwana wa Yefune,

wochokera ku fuko la Yuda,

20Semueli mwana wa Amihudi,

wochokera ku fuko la Simeoni;

21Elidadi mwana wa Kisiloni,

wochokera ku fuko la Benjamini;

22Buki mwana wa Yogili,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;

23Hanieli mwana wa Efodi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;

24Kemueli mwana wa Sifitani,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.

25Elizafani mwana wa Parinaki,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;

26Palitieli mwana wa Azani,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,

27Ahihudi mwana wa Selomi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;

28Pedaheli mwana wa Amihudi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”

29Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.

New Russian Translation

Числа 34:1-29

Границы Ханаана

1Господь сказал Моисею:

2– Дай израильтянам повеление и скажи им: «Когда вы войдете в Ханаан, то у земли, которая будет дана вам в удел, будут такие границы.

3Южная сторона у вас будет простираться от пустыни Цин вдоль границы Эдома. На востоке ваша южная граница будет начинаться от края Соленого моря34:3 То есть Мертвого моря; также в ст. 12., 4проходить на юг к Скорпионовой возвышенности, тянуться через Цин и идти на юг в направлении Кадеш-Барнеа. Оттуда она пойдет к Хацар-Аддару и пройдет к Ацмоне, 5где повернет к речке на границе Египта и закончится у моря34:5 То есть Средиземного моря; также в ст. 6..

6Вашей западной границей будет побережье Великого моря34:6 Букв.: «Великое море и побережье».. Это ваша граница на западе.

7Для северной границы проведите рубеж от Великого моря до горы Ор, 8а от горы Ор – до Лево-Хамата34:8 Или: «до перевала в Хамат».. Оттуда граница пойдет к Цедаду, 9продолжится к Зифрону и закончится в Хацар-Енане. Это ваша граница на севере.

10Для восточной границы проведите рубеж от Хацар-Енана до Шефама. 11Граница пойдет от Шефама к Ривле на восточной стороне Аина и продолжится по склонам к востоку от озера Киннерет34:11 То есть Галилейского озера.. 12Затем граница спустится по Иордану и дойдет до Соленого моря. Это ваша земля, с ее границами на каждой стороне».

13Моисей повелел израильтянам:

– Это та земля, которую вы получите в удел по жребию. Господь повелел отдать ее девяти с половиной родам, 14потому что семьи родов Рувима, Гада и половина рода Манассии уже получили надел. 15Эти два с половиной рода получили надел на восточной стороне Иордана, напротив Иерихона.

Ответственные за раздел земли

16Господь сказал Моисею:

17– Вот имена тех, кто разделит землю вам в удел: священник Элеазар и Иисус, сын Навин. 18Назначьте по одному вождю от каждого рода, чтобы помочь делить землю. 19Вот их имена:

Халев, сын Иефонниин, от рода Иуды;

20Самуил, сын Аммиуда, от рода Симеона;

21Элидад, сын Кислона, от рода Вениамина;

22Буккий, сын Иоглии, вождь от рода Дана;

23Ханниил, сын Эфода, вождь от рода Манассии, сына Иосифа;

24Кемуил, сын Шифтана, вождь от рода Ефрема, сына Иосифа;

25Элицафан, сын Фарнака, вождь от рода Завулона;

26Фалтиил, сын Аззана, вождь от рода Иссахара;

27Ахиуд, сын Шеломия, вождь от рода Асира;

28Педаил, сын Аммиуда, вождь от рода Неффалима.

29Это те, кому Господь велел назначить израильтянам наделы в земле Ханаана.