Numeri 34 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 34:1-29

Malire a Dziko la Kanaani

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:

3“ ‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere. 4Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni, 5kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.

6“ ‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.

7“ ‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori 8ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi, 9ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.

10“ ‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu. 11Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti. 12Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere.

“ ‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’ ”

13Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka, 14chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo. 15Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”

16Yehova anawuza Mose kuti, 17“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni. 18Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo. 19Mayina awo ndi awa:

Kalebe mwana wa Yefune,

wochokera ku fuko la Yuda,

20Semueli mwana wa Amihudi,

wochokera ku fuko la Simeoni;

21Elidadi mwana wa Kisiloni,

wochokera ku fuko la Benjamini;

22Buki mwana wa Yogili,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;

23Hanieli mwana wa Efodi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;

24Kemueli mwana wa Sifitani,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.

25Elizafani mwana wa Parinaki,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;

26Palitieli mwana wa Azani,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,

27Ahihudi mwana wa Selomi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;

28Pedaheli mwana wa Amihudi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”

29Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.

King James Version

Numbers 34:1-29

1And the LORD spake unto Moses, saying, 2Command the children of Israel, and say unto them, When ye come into the land of Canaan; (this is the land that shall fall unto you for an inheritance, even the land of Canaan with the coasts thereof:) 3Then your south quarter shall be from the wilderness of Zin along by the coast of Edom, and your south border shall be the outmost coast of the salt sea eastward: 4And your border shall turn from the south to the ascent of Akrabbim, and pass on to Zin: and the going forth thereof shall be from the south to Kadesh-barnea, and shall go on to Hazar-addar, and pass on to Azmon: 5And the border shall fetch a compass from Azmon unto the river of Egypt, and the goings out of it shall be at the sea. 6And as for the western border, ye shall even have the great sea for a border: this shall be your west border. 7And this shall be your north border: from the great sea ye shall point out for you mount Hor: 8From mount Hor ye shall point out your border unto the entrance of Hamath; and the goings forth of the border shall be to Zedad:

9¶ And the border shall go on to Ziphron, and the goings out of it shall be at Hazar-enan: this shall be your north border. 10And ye shall point out your east border from Hazar-enan to Shepham: 11And the coast shall go down from Shepham to Riblah, on the east side of Ain; and the border shall descend, and shall reach unto the side of the sea of Chinnereth eastward:34.11 side of the sea: Heb. shoulder of the sea 12And the border shall go down to Jordan, and the goings out of it shall be at the salt sea: this shall be your land with the coasts thereof round about. 13And Moses commanded the children of Israel, saying, This is the land which ye shall inherit by lot, which the LORD commanded to give unto the nine tribes, and to the half tribe: 14For the tribe of the children of Reuben according to the house of their fathers, and the tribe of the children of Gad according to the house of their fathers, have received their inheritance; and half the tribe of Manasseh have received their inheritance: 15The two tribes and the half tribe have received their inheritance on this side Jordan near Jericho eastward, toward the sunrising.

16And the LORD spake unto Moses, saying, 17These are the names of the men which shall divide the land unto you: Eleazar the priest, and Joshua the son of Nun. 18And ye shall take one prince of every tribe, to divide the land by inheritance. 19And the names of the men are these: Of the tribe of Judah, Caleb the son of Jephunneh. 20And of the tribe of the children of Simeon, Shemuel the son of Ammihud. 21Of the tribe of Benjamin, Elidad the son of Chislon. 22And the prince of the tribe of the children of Dan, Bukki the son of Jogli. 23The prince of the children of Joseph, for the tribe of the children of Manasseh, Hanniel the son of Ephod. 24And the prince of the tribe of the children of Ephraim, Kemuel the son of Shiphtan. 25And the prince of the tribe of the children of Zebulun, Elizaphan the son of Parnach. 26And the prince of the tribe of the children of Issachar, Paltiel the son of Azzan. 27And the prince of the tribe of the children of Asher, Ahihud the son of Shelomi. 28And the prince of the tribe of the children of Naphtali, Pedahel the son of Ammihud. 29These are they whom the LORD commanded to divide the inheritance unto the children of Israel in the land of Canaan.