Numeri 34 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 34:1-29

Malire a Dziko la Kanaani

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:

3“ ‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere. 4Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni, 5kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.

6“ ‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.

7“ ‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori 8ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi, 9ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.

10“ ‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu. 11Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti. 12Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere.

“ ‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’ ”

13Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka, 14chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo. 15Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”

16Yehova anawuza Mose kuti, 17“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni. 18Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo. 19Mayina awo ndi awa:

Kalebe mwana wa Yefune,

wochokera ku fuko la Yuda,

20Semueli mwana wa Amihudi,

wochokera ku fuko la Simeoni;

21Elidadi mwana wa Kisiloni,

wochokera ku fuko la Benjamini;

22Buki mwana wa Yogili,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;

23Hanieli mwana wa Efodi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;

24Kemueli mwana wa Sifitani,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.

25Elizafani mwana wa Parinaki,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;

26Palitieli mwana wa Azani,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,

27Ahihudi mwana wa Selomi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;

28Pedaheli mwana wa Amihudi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”

29Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.

Священное Писание

Числа 34:1-29

Границы Ханаана

1Вечный сказал Мусе:

2– Дай исраильтянам повеление и скажи им: «Когда вы войдёте в Ханаан, то у земли, которая будет дана вам в удел, будут такие границы.

3Южная сторона у вас будет простираться от пустыни Цин вдоль границы Эдома. На востоке ваша южная граница будет начинаться от края Мёртвого моря34:3 Букв.: «Солёного моря», также в ст. 12., 4проходить на юг к Скорпионовой возвышенности34:4 Или: «к возвышенности Акраббим»., тянуться через Цин и идти на юг в направлении Кадеш-Барни. Оттуда она пойдёт к Хацар-Аддару и пройдёт к Ацмоне, 5где повернёт к речке на границе Египта и закончится у Средиземного моря.

6Вашей западной границей будет побережье Средиземного моря34:6 Букв.: «Великого моря», также в ст. 7.. Это ваша граница на западе.

7Для северной границы проведите рубеж от Средиземного моря до горы Ор, 8а от горы Ор до Лево-Хамата34:8 Или: «до перевала в Хамат».. Оттуда граница пойдёт к Цедаду, 9продолжится к Зифрону и закончится в Хацар-Енане. Это ваша граница на севере.

10Для восточной границы проведите рубеж от Хацар-Енана до Шефама. 11Граница пойдёт от Шефама к Ривле на восточной стороне Аина и продолжится по склонам к востоку от Генисаретского озера. 12Затем граница спустится по Иордану и дойдёт до Мёртвого моря.

Это ваша земля – с её границами на каждой стороне».

13Муса повелел исраильтянам:

– Это та земля, которую вы получите в удел по жребию. Вечный повелел отдать её девяти с половиной родам, 14потому что семьи родов Рувима, Гада и половина рода Манассы уже получили надел. 15Эти два с половиной рода получили надел на восточной стороне Иордана, напротив Иерихона.

Ответственные за раздел земли

16Вечный сказал Мусе:

17– Вот имена тех, кто разделит землю вам в удел: священнослужитель Элеазар и Иешуа, сын Нуна. 18Назначьте по одному вождю от каждого рода, чтобы помочь делить землю. 19Вот их имена:

Халев, сын Иефоннии, от рода Иуды;

20Шемуил, сын Аммихуда, от рода Шимона;

21Элидад, сын Кислона, от рода Вениамина;

22Буккий, сын Иогли, вождь от рода Дана;

23Ханниил, сын Эфода, вождь от рода Манассы, сына Юсуфа;

24Кемуил, сын Шифтана, вождь от рода Ефраима, сына Юсуфа;

25Элицафан, сын Парнаха, вождь от рода Завулона;

26Палтиил, сын Аззана, вождь от рода Иссахара;

27Ахиуд, сын Шеломи, вождь от рода Ашира;

28Педаил, сын Аммихуда, вождь от рода Неффалима.

29Это те, кому Вечный велел назначить исраильтянам наделы в земле Ханаана.