Numeri 33 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 33:1-56

Malo omwe Aisraeli Anayima pa Ulendo Wawo

1Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni. 2Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:

3Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona, 4pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.

5Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.

6Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.

7Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.

8Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.

9Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.

10Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.

11Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.

12Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.

13Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.

14Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.

15Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai

16Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.

17Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.

18Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.

19Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.

20Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.

21Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.

22Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.

23Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.

24Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.

25Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.

26Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.

27Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.

28Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.

29Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.

30Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.

31Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.

32Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.

33Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.

34Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.

35Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.

36Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.

37Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu. 38Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto. 39Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.

40Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.

41Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.

42Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.

43Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.

44Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.

45Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.

46Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.

47Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.

48Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko. 49Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.

50Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti, 51“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani, 52mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo. 53Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo. 54Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.

55“ ‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo. 56Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’ ”

Nueva Versión Internacional

Números 33:1-56

Ruta de Israel por el desierto

1Cuando los israelitas salieron de Egipto bajo la dirección de Moisés y de Aarón, marchaban ordenadamente, como un ejército. 2Por orden del Señor, Moisés anotaba cada uno de los lugares de donde partían y adonde llegaban. Esta es la ruta que siguieron:

3El día quince del mes primero, un día después de la Pascua, los israelitas partieron de Ramsés. Marcharon con aire triunfal a la vista de todos los egipcios, 4mientras estos sepultaban a sus primogénitos, a quienes el Señor había herido de muerte. El Señor también dictó sentencia contra los dioses egipcios.

5Los israelitas partieron de Ramsés y acamparon en Sucot.

6Partieron de Sucot y acamparon en Etam, en los límites del desierto.

7Partieron de Etam, pero volvieron a Pi Hajirot, al este de Baal Zefón, y acamparon cerca de Migdol.

8Partieron de Pi Hajirot y cruzaron el mar hasta llegar al desierto. Después de andar tres días por el desierto de Etam, acamparon en Mara.

9Partieron de Mara con dirección a Elim, donde había doce manantiales y setenta palmeras, y acamparon allí.

10Partieron de Elim y acamparon cerca del mar Rojo.

11Partieron del mar Rojo y acamparon en el desierto de Sin.

12Partieron del desierto de Sin y acamparon en Dofcá.

13Partieron de Dofcá y acamparon en Alús.

14Partieron de Alús y acamparon en Refidín, donde los israelitas no tenían agua para beber.

15Partieron de Refidín y acamparon en el desierto de Sinaí.

16Partieron del desierto de Sinaí y acamparon en Quibrot Hatavá.

17Partieron de Quibrot Hatavá y acamparon en Jazerot.

18Partieron de Jazerot y acamparon en Ritmá.

19Partieron de Ritmá y acamparon en Rimón Peres.

20Partieron de Rimón Peres y acamparon en Libná.

21Partieron de Libná y acamparon en Risá.

22Partieron de Risá y acamparon en Celata.

23Partieron de Celata y acamparon en el monte Séfer.

24Partieron del monte Séfer y acamparon en Jaradá.

25Partieron de Jaradá y acamparon en Maquelot.

26Partieron de Maquelot y acamparon en Tajat.

27Partieron de Tajat y acamparon en Téraj.

28Partieron de Téraj y acamparon en Mitca.

29Partieron de Mitca y acamparon en Jasmoná.

30Partieron de Jasmoná y acamparon en Moserot.

31Partieron de Moserot y acamparon en Bené Yacán.

32Partieron de Bené Yacán y acamparon en Hor de Guidgad.

33Partieron de Hor de Guidgad y acamparon en Jotbata.

34Partieron de Jotbata y acamparon en Abroná.

35Partieron de Abroná y acamparon en Ezión Guéber.

36Partieron de Ezión Guéber y acamparon en Cades, en el desierto de Zin.

37Partieron de Cades y acamparon en el monte Hor, en la frontera con Edom. 38Por orden del Señor, el sacerdote Aarón subió al monte Hor, donde murió el día primero del mes quinto, cuarenta años después de que los israelitas habían salido de Egipto. 39Aarón murió en el monte Hor a la edad de ciento veintitrés años.

40El rey cananeo de Arad, que vivía en el Néguev de Canaán, se enteró de que los israelitas se acercaban.

41Partieron del monte Hor y acamparon en Zalmona.

42Partieron de Zalmona y acamparon en Punón.

43Partieron de Punón y acamparon en Obot.

44Partieron de Obot y acamparon en Iyé Abarín, en la frontera con Moab.

45Partieron de Iyé Abarín y acamparon en Dibón Gad.

46Partieron de Dibón Gad y acamparon en Almón Diblatayin.

47Partieron de Almón Diblatayin y acamparon en los campos de Abarín, cerca de Nebo.

48Partieron de los montes de Abarín y acamparon en las llanuras de Moab, cerca del Jordán, a la altura de Jericó. 49Acamparon a lo largo del Jordán, desde Bet Yesimot hasta Abel Sitín, en las llanuras de Moab.

Instrucciones acerca de la tierra prometida

50Allí en las llanuras de Moab, cerca del Jordán, a la altura de Jericó, el Señor dijo a Moisés: 51«Habla con los israelitas y diles que, una vez que crucen el Jordán y entren en Canaán, 52deberán expulsar del país a todos sus habitantes y destruir todos los ídolos e imágenes fundidas que ellos tienen. Ordénales que arrasen todos sus altares paganos 53y conquisten la tierra y la habiten, porque yo se la he dado a ellos como heredad. 54La tierra deberán repartirla por sorteo, según sus clanes. La tribu más numerosa recibirá la heredad más grande, mientras que la tribu menos numerosa recibirá la heredad más pequeña. Todo lo que les toque en el sorteo será de ellos, y recibirán su heredad según sus familias patriarcales.

55»Pero si no expulsan a los habitantes de la tierra que ustedes van a poseer, sino que los dejan allí, esa gente les causará problemas, como si tuvieran clavadas astillas en los ojos y espinas en los costados. 56Entonces yo haré con ustedes lo que había pensado hacer con ellos».