Numeri 33 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 33:1-56

Malo omwe Aisraeli Anayima pa Ulendo Wawo

1Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni. 2Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:

3Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona, 4pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.

5Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.

6Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.

7Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.

8Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.

9Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.

10Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.

11Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.

12Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.

13Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.

14Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.

15Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai

16Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.

17Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.

18Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.

19Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.

20Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.

21Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.

22Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.

23Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.

24Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.

25Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.

26Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.

27Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.

28Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.

29Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.

30Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.

31Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.

32Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.

33Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.

34Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.

35Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.

36Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.

37Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu. 38Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto. 39Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.

40Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.

41Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.

42Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.

43Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.

44Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.

45Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.

46Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.

47Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.

48Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko. 49Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.

50Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti, 51“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani, 52mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo. 53Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo. 54Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.

55“ ‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo. 56Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’ ”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Числа 33:1-56

Лагеря исроильтян

1Вот лагеря на пути исроильтян, когда они вышли из Египта по воинствам их, под началом Мусо и Хоруна. 2По повелению Вечного Мусо записал лагеря на их пути. Вот их путь по лагерям.

3Исроильтяне тронулись в путь из Раамсеса в пятнадцатый день первого месяца (ранней весной), в день после праздника Освобождения. Они выступили смело33:3 Букв.: «под высокой рукою», т. е. под защитой Вечного. на виду у египтян, 4хоронивших первенцев, которых умертвил Вечный. Так Вечный совершил суд над их богами.

5Исроильтяне покинули Раамсес и остановились в Суккоте.

6Они покинули Суккот и остановились в Етаме, на краю пустыни.

7Они покинули Етам, повернули к Пи-Хахироту, что на востоке от Баал-Цефона, и остановились рядом с Мигдолом.

8Они покинули Пи-Хахирот, прошли через море в пустыню и, пройдя три дня по пустыне Етам, остановились в Маре.

9Они покинули Мару и пришли в Елим, где были двенадцать источников и семьдесят пальм, и остановились здесь.

10Они покинули Елим и остановились у Тростникового моря.

11Они покинули Тростниковое море и остановились в пустыне Син.

12Они покинули пустыню Син и остановились в Дофке.

13Они покинули Дофку и остановились в Алуше.

14Они покинули Алуш и остановились в Рефидиме, где у народа не было воды, чтобы утолить жажду.

15Они покинули Рефидим и остановились в Синайской пустыне.

16Они покинули Синайскую пустыню и остановились в Киврот-Хатааве.

17Они покинули Киврот-Хатааву и остановились в Хацероте.

18Они покинули Хацерот и остановились в Ритме.

19Они покинули Ритму и остановились в Риммон-Фареце.

20Они покинули Риммон-Фарец и остановились в Ливне.

21Они покинули Ливну и остановились в Риссе.

22Они покинули Риссу и остановились в Кеелате.

23Они покинули Кеелат и остановились у горы Шафер.

24Они покинули гору Шафер и остановились в Хараде.

25Они покинули Хараду и остановились в Макелоте.

26Они покинули Макелот и остановились в Тахате.

27Они покинули Тахат и остановились в Терахе.

28Они покинули Терах и остановились в Митеке.

29Они покинули Митеку и остановились в Хашмоне.

30Они покинули Хашмону и остановились в Мосероте.

31Они покинули Мосерот и остановились в Бене-Яакане.

32Они покинули Бене-Яакан и остановились в Хор-Хаггидгаде.

33Они покинули Хор-Хаггидгад и остановились в Иотвате.

34Они покинули Иотват и остановились в Авроне.

35Они покинули Аврон и остановились в Эцион-Гевере.

36Они покинули Эцион-Гевер и остановились в Кадеше, в пустыне Цин.

37Они покинули Кадеш и остановились у горы Ор, на границе Эдома. 38По повелению Вечного священнослужитель Хорун поднялся на гору Ор и умер там в первый день пятого месяца (в середине лета), в сороковой год после того, как исроильтяне ушли из Египта. 39Хоруну было сто двадцать три года, когда он умер на горе Ор.

40Ханонский царь Арада, расположенного в Негеве ханонском, услышал, что идут исроильтяне.

41Они покинули гору Ор и остановились в Салмоне. 42Они покинули Салмону и остановились в Пуноне.

43Они покинули Пунон и остановились в Овоте.

44Они покинули Овот и остановились в Ийе-Авариме, на землях Моава.

45Они покинули Ийе-Аварим и остановились в Дивон-Гаде.

46Они покинули Дивон-Гад и остановились в Алмон-Дивлатаиме.

47Они покинули Алмон-Дивлатаим и остановились в горах Аварим, рядом с Нево.

48Они покинули горы Аварим и остановились на равнинах Моава у реки Иордан напротив города Иерихона. 49На равнинах Моава они остановились вдоль Иордана от Бет-Иешимота до Авель-Шиттима.

50На равнинах Моава у реки Иордан, напротив города Иерихона, Вечный сказал Мусо:

51– Говори с исроильтянами и скажи им: «Когда вы перейдёте через Иордан в Ханон, 52то прогоните всех жителей этой земли. Сокрушите их каменных и литых идолов и разорите их капища на возвышенностях. 53Завладейте этой землёй и поселитесь в ней, потому что Вечный отдал эту землю вам во владение. 54Разделите землю по жребию между кланами. Большему клану дайте больший надел, а меньшему – меньший. Что выпадет им по жребию, то и будет их. Разделите землю между родами. 55Если вы не прогоните обитателей этой земли, то те, кому вы дадите остаться, станут у вас как шипы в глазах и колючки в боку. Они лишат вас покоя на этой земле, в которой вы будете жить. 56Тогда Я сделаю с вами то, что собираюсь сделать с ними».