Numeri 32 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 32:1-42

Mafuko a ku Tsidya la Yorodani

1Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo. 2Choncho Arubeni ndi Agadi anapita kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa atsogoleri a anthu ndi kunena kuti, 3“Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni, 4dziko lomwe Yehova anagonjetsa pamaso pa Aisraeli, ndiwo malo woyenera ziweto, ndipo atumiki anufe tili ndi ziweto. 5Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’ ”

6Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno? 7Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa? 8Izi ndi zimene makolo anu anachita pamene ndinawatuma kuchokera ku Kadesi kukaona dzikolo. 9Atapita ku chigwa cha Esikolo, ndi kuliona dzikolo, anafowoketsa Aisraeli kuti asalowe mʼdziko limene Yehova anawapatsa. 10Yehova anakwiya tsiku limenelo ndipo analumbira kuti, 11‘Chifukwa sananditsatire ndi mtima wonse, palibe ndi mmodzi yemwe mwa amuna a zaka makumi awiri kapena kuposa pamenepo, amene anachokera ku Igupto, amene adzaone dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo. 12Palibe ndi mmodzi yemwe kupatula Kalebe mwana wa Yefune, Mkeni, ndi Yoswa mwana wa Nuni chifukwa anatsatira Yehova ndi mtima wonse.’ 13Yehova anakwiyira Aisraeli kwambiri ndipo anawachititsa kuyenda mʼchipululu zaka makumi anayi, mpaka mʼbado wonse wa anthu amene anachita choyipa pamaso pake unatha.

14“Ndipo onani tsopano, inu mʼbado wochimwa, mwalowa mʼmalo mwa makolo anu ndipo mwachititsa kuti Yehova akwiyire Israeli kwambiri. 15Ngati muleka kumutsata, Iye adzawasiyiranso anthu onsewa mʼchipululu ndipo mudzawonongetsa anthu onsewa.”

16Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu. 17Koma ndife okonzeka kutenga zida za nkhondo ndi kupita pamodzi ndi Aisraeli mpaka titakawafikitsa ku malo awo. Panopa, akazi ndi ana athu akhala mʼmizinda yotetezedwa, kuwateteza kwa anthu okhala mʼdzikoli. 18Sitidzabwerera ku midzi yathu mpaka Mwisraeli aliyense atalandira cholowa chake. 19Sitidzalandira cholowa chilichonse pamodzi nawo ku tsidya lina la Yorodani, chifukwa cholowa chathu tachipezera ku tsidya lino la kummawa kwa Yorodani.”

20Tsono Mose anati kwa anthuwo, “Ngati inu mudzachita zimenezi, kutenga zida zankhondo pamaso pa Yehova kuti muchite nkhondo, 21ndipo ngati nonsenu mudzapita ndi zida kuwoloka Yorodani pamaso pa Yehova mpaka atachotsa adani ake pamaso pake, 22dzikolo nʼkugonja pamaso pa Yehova, mudzabwera ndi kukhala mfulu pamaso pa Yehova ndi Aisraeli. Ndipo dziko lino lidzakhala lanu pamaso pa Yehova.

23“Koma mukalephera kuchita izi, mudzakhala mukuchimwira Yehova. Ndipo dziwani kuti tchimo lanu lidzakupezani. 24Amangireni akazi ndi ana anu mizinda, mangani makola a ziweto zanu, koma chitani zomwe mwalonjeza.”

25Agadi ndi Arubeni anati kwa Mose, “Ife antchito anu tidzachita monga mbuye wathu mwalamulira. 26Ana ndi akazi athu, ziweto zathu zina ndi ngʼombe zidzatsala kuno ku mizinda ya Giliyadi, 27koma antchito anufe, mwamuna aliyense amene ali ndi chida cha nkhondo, adzawoloka kukamenya nkhondo pamaso pa Yehova monga mbuye wathu wanenera.”

28Choncho Mose anapereka malamulo awa kwa wansembe Eliezara, kwa Yoswa mwana wa Nuni ndi kwa akulu a mafuko a Aisraeli. 29Mose anawawuza kuti, ngati Agadi ndi Arubeni, mwamuna aliyense wokonzekera nkhondo, awoloka Yorodani pamodzi ndi inu pamaso pa Yehova, ndipo dzikolo nʼkugonjetsedwa pamaso panu, mudzawapatse dziko la Giliyadi kukhala lawo. 30Koma ngati sawoloka pamodzi nanu ndi zida zankhondo, ayenera kulandira cholowa chawo pamodzi ndi inu ku Kanaani.

31Agadi ndi Arubeni anayankha kuti, “Antchito anu adzachita zimene Yehova wanena. 32Tidzawoloka pamaso pa Yehova ndipo tidzalowa mu Kanaani ndi zida zankhondo, koma cholowa chathu chidzakhala ku tsidya lino la Yorodani.”

33Choncho Mose anapatsa Agadi, Arubeni ndi theka la fuko la Manase mwana wa Yosefe dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi, mfumu ya ku Basani, dziko lonse, mizinda yake ndi midzi yowazungulira.

34Agadi anamanga Diboni, Ataroti, Aroeri, 35Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha, 36Beti-Nimira ndi Beti-Harani mizinda ya malinga. Anamanganso makola a ziweto zawo. 37Ndipo Arubeni anamanga Hesiboni, Eleali, Kiriataimu, 38Nebo ndi Baala-Meoni (mayina awa anasinthidwa) ndi Sibima. Anapereka mayina ku mizinda ina yomwe anamangayo.

39Zidzukulu za Makiri mwana wa Manase zinapita ku Giliyadi kulanda mzindawo ndi kuthamangitsira kunja Aamori omwe anali kumeneko. 40Tsono Mose anapereka Giliyadi kwa Amakiri, ana a Manase, ndipo anakhala kumeneko. 41Yairi, mwana wa Manase analanda midzi yambiri ya Giliyadi ndi kuyitcha kuti Havoti-Yairi. 42Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.

Священное Писание

Числа 32:1-42

Раздел земли к востоку от Иордана

(Втор. 3:12-20)

1Рувимиты и гадиты, у которых были очень большие стада, увидели, что земли Иазера и Галаада хороши для скота. 2Они пришли к Мусе, священнослужителю Элеазару и вождям народа и сказали:

3– Города Атарот, Дивон, Иазер, Нимра, Хешбон, Элеале, Севам, Нево и Беон – 4земля, которую Вечный покорил народу Исраила, хороша для скота, а у твоих рабов есть скот. 5Если мы нашли у тебя расположение, – сказали они, – то пусть эта земля и достанется во владение твоим рабам. Не переводи нас через Иордан.

6Муса сказал гадитам и рувимитам:

– Ваши братья пойдут на войну, а вы будете сидеть здесь? 7Зачем вы отбиваете у исраильтян охоту перейти в землю, которую дал им Вечный? 8Так сделали ваши отцы, когда я посылал их из Кадеш-Барни осмотреть эту землю. 9Придя в долину Эшкол и осмотрев землю, они отбили у исраильтян охоту войти в землю, которую дал им Вечный. 10В тот день Вечный разгневался и поклялся: 11«Никто из покинувших Египет, от двадцати лет и старше, не увидит землю, которую Я клятвенно обещал Ибрахиму, Исхаку и Якубу, потому что они не повиновались Мне от всего сердца – 12никто, кроме Халева, сына кенезеянина Иефоннии, и Иешуа, сына Нуна, которые от всего сердца повиновались Вечному». 13Вечный разгневался на Исраил и заставил народ сорок лет скитаться по пустыне, пока всё то поколение, которое сделало в Его глазах зло, не сгинуло. 14А теперь вы, отродье грешников, встали на место ваших отцов и ещё сильнее разжигаете гнев Вечного на Исраил! 15Если вы откажетесь повиноваться Вечному, то Он снова оставит этот народ в пустыне, а вы будете виновниками их гибели.

16Они подошли к Мусе и сказали:

– Мы построим здесь загоны для скота и города для наших жён и детей, 17а потом будем готовы вооружиться и идти перед исраильтянами, пока не приведём их в их надел. Тем временем наши жёны и дети будут жить в укреплённых городах, в безопасности от жителей этой земли. 18Мы не вернёмся домой, пока каждый исраильтянин не получит свой надел. 19Мы не получим надел с ними на той стороне Иордана, потому что наш надел достался нам на этой, восточной стороне.

20Муса сказал им:

– Если вы сделаете это, если вооружитесь, чтобы воевать для Вечного, 21и каждый из вас, кто вооружён, переправится перед Вечным за Иордан, пока Он не прогонит Своих врагов перед Собой, 22то когда земля будет покорена Вечному, вы можете вернуться. Тогда вы будете свободными от обязательства Вечному и Исраилу, а эта земля будет вашим владением перед Вечным. 23Но если вы не сделаете этого, то вы согрешите против Вечного, и знайте: вам не избежать наказания за грех. 24Стройте города для жён и детей и загоны для отар, но исполните то, что обещали.

25Гадиты и рувимиты сказали Мусе:

– Мы – твои рабы. Мы сделаем, как велит наш господин. 26Наши дети и жёны, отары и весь наш скот останутся здесь, в городах Галаада. 27А твои рабы, все вооружённые для битвы, переправятся, чтобы воевать перед Вечным, как велит наш господин.

28Тогда Муса отдал распоряжение о них священнослужителю Элеазару, Иешуа, сыну Нуна, и главам семейств исраильского народа. 29Он сказал им:

– Если гадиты и рувимиты, все вооружённые для битвы, переправятся с вами за Иордан перед Вечным, то, когда земля покорится вам, отдайте им во владение землю Галаада. 30А если они не переправятся с вами вооружённые, то пусть они примут свой надел с вами в Ханаане.

31Гадиты и рувимиты ответили:

– Мы – твои рабы. Мы сделаем так, как сказал Вечный. 32Мы с оружием переправимся перед Вечным в Ханаан, но пусть удел, который нам достался, останется за нами на этой стороне реки Иордан.

33Тогда Муса отдал родам Гада, Рувима и половине рода Манассы, сына Юсуфа, царство Сигона, царя аморреев, и царство Ога, царя Башана, – всю землю с её городами и их окрестностями.

34Гадиты построили Дивон, Атарот, Ароер, 35Атарот-Шофан, Иазер, Иогбегу, 36Бет-Нимру и Бет-Аран, города-крепости и загоны для скота. 37А рувимиты отстроили города Хешбон, Элеале, Кириатаим, 38Нево и Баал-Меон (их названия были изменены) и Сивму. Они дали отстроенным городам другие имена.

39Потомки Махира, сына Манассы, пришли в Галаад, захватили его и прогнали оттуда аморреев. 40Муса отдал Галаад махиритам, потомкам Манассы, и они поселились там. 41Иаир, потомок Манассы, захватил здесь несколько поселений и назвал их Хаввот-Иаир («селения Иаира»). 42А Нова захватил Кенат с окрестными поселениями и назвал его в свою честь Нова.