Numeri 31 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 31:1-54

Aisraeli Agonjetsa Amidiyani

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”

3Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova. 4Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.” 5Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli. 6Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.

7Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense. 8Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori. 9Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense. 10Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse. 11Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe. 12Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.

13Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa. 14Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.

15Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?” 16Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova. 17Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna, 18koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.

19“Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu. 20Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”

21Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili: 22Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu 23ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo. 24Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”

Kugawana Zolanda ku Nkhondo

25Yehova anawuza Mose kuti, 26“Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo. 27Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse. 28Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa. 29Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova. 30Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.” 31Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.

32Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000, 33Ngʼombe 72,000, 34abulu 61,000, 35ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.

36Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali:

nkhosa 337,500, 37mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;

38ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;

39abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;

40anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.

41Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.

42Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja. 43Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500, 44ngʼombe 36,000, 45abulu 30,500, 46anthu 16,000. 47Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.

48Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose, 49iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa. 50Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”

51Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula. 52Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200. 53Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo. 54Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.

King James Version

Numbers 31:1-54

1And the LORD spake unto Moses, saying, 2Avenge the children of Israel of the Midianites: afterward shalt thou be gathered unto thy people. 3And Moses spake unto the people, saying, Arm some of yourselves unto the war, and let them go against the Midianites, and avenge the LORD of Midian. 4Of every tribe a thousand, throughout all the tribes of Israel, shall ye send to the war.31.4 Of…: Heb. A thousand of a tribe, a thousand of a tribe 5So there were delivered out of the thousands of Israel, a thousand of every tribe, twelve thousand armed for war. 6And Moses sent them to the war, a thousand of every tribe, them and Phinehas the son of Eleazar the priest, to the war, with the holy instruments, and the trumpets to blow in his hand.

7And they warred against the Midianites, as the LORD commanded Moses; and they slew all the males. 8And they slew the kings of Midian, beside the rest of them that were slain; namely, Evi, and Rekem, and Zur, and Hur, and Reba, five kings of Midian: Balaam also the son of Beor they slew with the sword. 9And the children of Israel took all the women of Midian captives, and their little ones, and took the spoil of all their cattle, and all their flocks, and all their goods. 10And they burnt all their cities wherein they dwelt, and all their goodly castles, with fire. 11And they took all the spoil, and all the prey, both of men and of beasts. 12And they brought the captives, and the prey, and the spoil, unto Moses, and Eleazar the priest, and unto the congregation of the children of Israel, unto the camp at the plains of Moab, which are by Jordan near Jericho.

13¶ And Moses, and Eleazar the priest, and all the princes of the congregation, went forth to meet them without the camp. 14And Moses was wroth with the officers of the host, with the captains over thousands, and captains over hundreds, which came from the battle.31.14 battle: Heb. host of war 15And Moses said unto them, Have ye saved all the women alive? 16Behold, these caused the children of Israel, through the counsel of Balaam, to commit trespass against the LORD in the matter of Peor, and there was a plague among the congregation of the LORD. 17Now therefore kill every male among the little ones, and kill every woman that hath known man by lying with him.31.17 him: Heb. a male 18But all the women children, that have not known a man by lying with him, keep alive for yourselves. 19And do ye abide without the camp seven days: whosoever hath killed any person, and whosoever hath touched any slain, purify both yourselves and your captives on the third day, and on the seventh day. 20And purify all your raiment, and all that is made of skins, and all work of goats’ hair, and all things made of wood.31.20 that…: Heb. instrument, or, vessel of skins

21¶ And Eleazar the priest said unto the men of war which went to the battle, This is the ordinance of the law which the LORD commanded Moses; 22Only the gold, and the silver, the brass, the iron, the tin, and the lead, 23Every thing that may abide the fire, ye shall make it go through the fire, and it shall be clean: nevertheless it shall be purified with the water of separation: and all that abideth not the fire ye shall make go through the water. 24And ye shall wash your clothes on the seventh day, and ye shall be clean, and afterward ye shall come into the camp.

25¶ And the LORD spake unto Moses, saying, 26Take the sum of the prey that was taken, both of man and of beast, thou, and Eleazar the priest, and the chief fathers of the congregation:31.26 that…: Heb. of the captivity 27And divide the prey into two parts; between them that took the war upon them, who went out to battle, and between all the congregation: 28And levy a tribute unto the LORD of the men of war which went out to battle: one soul of five hundred, both of the persons, and of the beeves, and of the asses, and of the sheep: 29Take it of their half, and give it unto Eleazar the priest, for an heave offering of the LORD. 30And of the children of Israel’s half, thou shalt take one portion of fifty, of the persons, of the beeves, of the asses, and of the flocks, of all manner of beasts, and give them unto the Levites, which keep the charge of the tabernacle of the LORD.31.30 flocks: or, goats 31And Moses and Eleazar the priest did as the LORD commanded Moses. 32And the booty, being the rest of the prey which the men of war had caught, was six hundred thousand and seventy thousand and five thousand sheep, 33And threescore and twelve thousand beeves, 34And threescore and one thousand asses, 35And thirty and two thousand persons in all, of women that had not known man by lying with him. 36And the half, which was the portion of them that went out to war, was in number three hundred thousand and seven and thirty thousand and five hundred sheep: 37And the LORD’s tribute of the sheep was six hundred and threescore and fifteen. 38And the beeves were thirty and six thousand; of which the LORD’s tribute was threescore and twelve. 39And the asses were thirty thousand and five hundred; of which the LORD’s tribute was threescore and one. 40And the persons were sixteen thousand; of which the LORD’s tribute was thirty and two persons. 41And Moses gave the tribute, which was the LORD’s heave offering, unto Eleazar the priest, as the LORD commanded Moses. 42And of the children of Israel’s half, which Moses divided from the men that warred, 43(Now the half that pertained unto the congregation was three hundred thousand and thirty thousand and seven thousand and five hundred sheep, 44And thirty and six thousand beeves, 45And thirty thousand asses and five hundred, 46And sixteen thousand persons;) 47Even of the children of Israel’s half, Moses took one portion of fifty, both of man and of beast, and gave them unto the Levites, which kept the charge of the tabernacle of the LORD; as the LORD commanded Moses.

48¶ And the officers which were over thousands of the host, the captains of thousands, and captains of hundreds, came near unto Moses: 49And they said unto Moses, Thy servants have taken the sum of the men of war which are under our charge, and there lacketh not one man of us.31.49 charge: Heb. hand 50We have therefore brought an oblation for the LORD, what every man hath gotten, of jewels of gold, chains, and bracelets, rings, earrings, and tablets, to make an atonement for our souls before the LORD.31.50 gotten: Heb. found 51And Moses and Eleazar the priest took the gold of them, even all wrought jewels. 52And all the gold of the offering that they offered up to the LORD, of the captains of thousands, and of the captains of hundreds, was sixteen thousand seven hundred and fifty shekels.31.52 offering: Heb. heave offering 53(For the men of war had taken spoil, every man for himself.) 54And Moses and Eleazar the priest took the gold of the captains of thousands and of hundreds, and brought it into the tabernacle of the congregation, for a memorial for the children of Israel before the LORD.