Numeri 30 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 30:1-16

Za Kulumbira

1Mose anawuza Aisraeli onse zonse zimene Yehova anamulamula. Iye anati, “Zimene Yehova walamula ndi izi: 2Munthu wamwamuna ngati walonjeza kwa Yehova kapena kulumbira kuti adzachita zimene walumbirazo, asaphwanye mawuwo koma ayenera kuchita chilichonse chimene wanena.

3“Pamene munthu wamkazi amene akukhalabe mʼnyumba ya abambo ake alumbira kwa Yehova kuti adzachita zimene walonjeza pa ubwana wake, 4abambo ake namva kulumbira kwakeko kapena kulonjeza kwake kuti adzachitadi, ndipo abambo akewo wosayankhula kanthu, mkaziyo achitedi zomwe analumbirazo. Ayenera kudzachita zonse zimene walonjeza zija. 5Koma ngati abambo akewo amva kulumbira kwake ndi kumukaniza, palibe lamulo lomukakamiza mkaziyo kuchita zimene walonjeza. Yehova adzamukhululukira chifukwa abambo ake anamukaniza.

6“Ngati akwatiwa atalumbira kale kapena ngati alonjeza mofulumira ndi pakamwa pake, 7mwamuna wake ndi kumva kulumbira kwakeko koma wosanenapo kanthu, mkaziyo achitedi zomwe walumbirazo. Achite ndithu zomwe walonjeza zija. 8Koma ngati mwamuna wake amuletsa atamva kulumbira kwakeko, pamenepo amumasula mayiyo ku zimene analumbira komanso ku zimene analonjeza mosaganiza bwinozo ndipo Yehova adzamukhululukira.

9“Mayi wamasiye kapena wosiyidwa ukwati akalumbira kapena kulonjeza kuti adzachita kanthu kalikonse, ayenera kukachitadi.

10“Koma ngati mayi wokwatiwa alumbira nalonjeza kuti adzachitadi zimene walonjeza, 11mwamuna wake ndi kumva kulumbira kwakeko koma osayankhulapo kanthu, osamuletsa, ayenera kuchitadi zonse zimene walumbira ndi zonse zimene walonjeza. 12Koma ngati mwamuna wake amva ndi kumuletsa kuti asachite zomwe walumbirazo, palibe lamulo lomukakamiza mayiyo kuchita zomwe walumbirazo kapenanso zimene walonjeza. Popeza mwamuna wake wamuletsa, Yehova adzamukhululukira mayiyo. 13Mwamuna wake ali ndi mphamvu zovomereza kapena kukana zimene mayiyo walumbira kapena zimene walonjeza zokhudza kudzilanga yekha. 14Ndipo ngati mmawa mwake ndi masiku otsatira mwamuna wake sanenapo kanthu atamva zimenezi, mayiyo achitedi zimene walumbira kapena zimene walonjeza. Mwamunayo wavomereza zimenezo, chifukwa sanamuwuze kanthu mayiyo pa tsiku limene anamva akulonjeza kapena kulumbira. 15Koma ngati mwamunayo amukaniza patapita kanthawi atazimva kale, iyeyo ndiye wochimwa mʼmalo mwa mayiyo.”

16Awa ndiwo malamulo amene Yehova analamula Mose za mwamuna ndi mkazi wake, ndiponso abambo ndi mwana wawo wamkazi amene akanali mtsikana wokhalabe mʼnyumba ya abambo akewo.

New Serbian Translation

4. Мојсијева 30:1-16

Завети жена

1Мојсије рече главарима племена израиљског народа: „Ово је Господ заповедио: 2’Ако неки човек учини завет Господу, или положи заклетву којом се обавеже, нека не погази своју реч; нека учини оно што изађе из његових уста.

3Ако жена учини завет Господу у својој младости, или се обавеже заклетвом док је у кући свога оца, 4па њен отац сазна за њен завет или заклетву којом се обавезала, али јој не приговори, тада сви њени завети и свака заклетва којом се обавезала остају на снази. 5Али ако јој отац то забрани истог дана кад сазна, сви њени завети и заклетве којима се обавезала више не важе. Господ ће јој опростити, јер јој је отац забранио.

6Ако се уда док је под заветом, или се обавезала непромишљеном изјавом, 7па њен муж сазна за то, али јој не приговори истог дана кад сазна, тада сви њени завети и обећања којима се обавезала остају на снази. 8Ако јој се муж успротиви истог дана кад сазна, он тиме поништава завет, или непромишљену изјаву којом се обавезала. А Господ ће јој опростити.

9Завет удовице или разведене, све чиме се обавезала, и даље је обавезује.

10Ако жена учини завет док је у кући свог мужа, или се обавеже обећањем уз заклетву, 11па њен муж сазна за то, али јој не приговори и не забрани јој, тада сви њени завети и свако обећање којим се обавезала остају на снази. 12Али ако их муж поништи истог дана кад сазна за њих, ништа што је прешло преко њених усана не важи. Пошто их је њен муж поништио, Господ ће јој опростити. 13Сваки завет и сваку заклетву којом се жена обавеже на неко самоодрицање, њен муж може да потврди или поништи. 14Ако дани пролазе, а муж јој не приговара, он потврђује све њене завете, или сва обећања којима се обавезала. Он их је потврдио, јер јој није приговорио истог дана кад је сазнао за њих. 15Али ако их поништи касније, пошто је већ сазнао за њих, сам ће носити њену кривицу.’“

16То су одредбе које је Господ дао Мојсију за мужа и његову жену, и за оца и његову ћерку у њеној младости, док је у кући свога оца.