Numeri 3 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 3:1-51

Alevi

1Iyi ndi mbiri ya banja la Aaroni ndi Mose pa nthawi yomwe Yehova anayankhula ndi Mose pa phiri la Sinai.

2Mayina a ana aamuna a Aaroni anali Nadabu, woyamba kubadwa, Abihu, Eliezara ndi Itamara. 3Amenewa ndi mayina a ana aamuna a Aaroni, ansembe odzozedwa omwe anapatulidwa kuti azitumikira ngati ansembe. 4Koma Nadabu ndi Abihu, anagwa nafa pamaso pa Yehova pamene ankapereka nsembe ndi moto wachilendo pamaso pa Yehova mʼchipululu cha Sinai. Iwowo analibe ana aamuna. Choncho Eliezara ndi Itamara ndiwo amene ankatumikira ngati ansembe nthawi imene Aaroni abambo awo anali moyo.

5Yehova anati kwa Mose, 6“Bweretsa fuko la Levi ndipo ulipereke kwa Aaroni wansembe kuti lizimutumikira. 7Azigwira ntchito yothandiza iyeyo ndi gulu lonse ku tenti ya msonkhano pogwira ntchito ya ku Chihema. 8Azisamalira zipangizo zonse za mu tenti ya msonkhano, ndipo azigwirira ntchito Aisraeli potumikira mu tenti. 9Pereka Alevi kwa Aaroni ndi kwa ana ake aamuna. Amenewa ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwa iye kwathunthu. 10Usankhe Aaroni ndi ana ake aamuna kuti azitumikira pa ntchito ya unsembe. Koma wina aliyense woyandikira malo opatulika aphedwe.”

11Yehova anawuzanso Mose kuti, 12“Pakati pa Aisraeli onse ndatenga Alevi kulowa mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa kwa amayi a Chiisraeli. Alevi ndi anga, 13pakuti ana onse oyamba kubadwa ndi anga. Nditakantha ana onse oyamba kubadwa mu Igupto, ndinadzipatulira ndekha mwana aliyense woyamba kubadwa mu Israeli, wa munthu ndi nyama. Azikhala anga. Ine ndine Yehova.”

14Yehova anawuza Mose mʼchipululu cha Sinai kuti, 15“Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.” 16Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.

17Mayina a ana aamuna a Levi ndi awa:

Geresoni, Kohati ndi Merari.

18Mayina a ana a Geresoni potsata mabanja awo ndi awa:

Libini ndi Simei.

19Ana a Kohati potsata mabanja awo ndi awa:

Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli.

20Ana a Merari potsata mabanja awo ndi awa:

Mali ndi Musi.

Amenewa ndiwo anali mabanja a Alevi monga mwa makolo awo.

21Kwa Geresoni kunali banja la Alibini, banja la Asimei. Amenewa ndiwo anali mabanja a Ageresoni. 22Chiwerengero cha amuna onse amene anawawerenga a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 7,500. 23Mabanja a Ageresoni azimanga misasa yawo kumadzulo, kumbuyo kwa Chihema. 24Mtsogoleri wa mabanja a Ageresoni anali Eliyasafu mwana wa Laeli. 25Ntchito imene Ageresoni anapatsidwa ku tenti ya msonkhano inali yosamalira Chihema ndi tenti, pamodzi ndi zophimbira zake, katani ya pa khomo la ku tenti ya msonkhano, 26ndi makatani wotchinga bwalo, katani ya pa chipata cholowera ku bwalo lozungulira Chihema ndi guwa lansembe, zingwe ndi zonse zokhudzana ndi ntchito yawo.

27Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati. 28Chiwerengero cha amuna onse a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 8,600. Akohati ankagwira ntchito yosamalira malo wopatulika. 29Mabanja a ana a Kohati ankamanga misasa yawo kummwera kwa Chihema. 30Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Kohati anali Elizafani mwana wa Uzieli. 31Iwo ankagwira ntchito yosamalira Bokosi la Chipangano, tebulo, choyikapo nyale, maguwa, zipangizo za kumalo wopatulika zimene ansembe ankagwiritsa ntchito, katani, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito. 32Mtsogoleri wamkulu wa Alevi anali Eliezara mwana wa Aaroni wansembe. Iye anasankhidwa kukhala woyangʼanira omwe ankasamalira malo wopatulika.

33Kwa Merari kunali banja la Mali ndi banja la Musi. Amenewa ndiye anali mabanja a Amerari. 34Chiwerengero cha amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 6,200. 35Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Amerari anali Zuriyeli mwana wa Abihaili. Iwo ankamanga misasa yawo kumpoto kwa Chihema. 36Amerari anapatsidwa ntchito yosamalira mitengo ya chihema, nsichi zake, mizati yake, matsinde ake, ndi zida zake zonse, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito, 37pamodzi ndi mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema ndi zingwe zake.

38Mose ndi Aaroni ndi ana ake aamuna ankamanga misasa yawo kummawa kwa chihema, kuyangʼana kotulukira dzuwa, kutsogolo kwa tenti ya msonkhano. Anali ndi ntchito yosamalira malo wopatulika mʼmalo mwa Aisraeli. Aliyense woyandikira malo wopatulika ankayenera kuphedwa.

39Alevi onse amene Mose ndi Aaroni anawawerenga potsatira lamulo la Yehova monga mwa magulu a mabanja awo, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo anali 22,000.

40Yehova anawuza Mose kuti, “Werenga ana onse aamuna oyamba kubadwa mu Israeli, omwe ali ndi mwezi umodzi kapena kupitirirapo ndipo ulembe mndandanda wa mayina awo. 41Unditengere Alevi onse mʼmalo mwa ana oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso ziweto zazimuna za Alevi mʼmalo mwa ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa za Aisraeli. Ine ndine Yehova.”

42Choncho Mose anawerenga ana aamuna onse oyamba kubadwa a Aisraeli monga momwe Yehova anamulamulira. 43Chiwerengero chonse cha ana aamuna oyamba kubadwa kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 22, 273.

44Ndipo Yehova anawuzanso Mose kuti, 45“Tenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso zoweta zonse za Alevi mʼmalo mwa zoweta za Aisraeli. Alevi ndi anga. Ine ndine Yehova. 46Pofuna kuwombola ana aamuna 273 oyamba kubadwa a Aisraeli amene anaposa chiwerengero cha aamuna a fuko la Levi, 47utenge masekeli asanu pa munthu aliyense. Masekeliwo akhale ofanana ndi masekeli a ku malo wopatulika, kumene sekeli imodzi imakwanira magera makumi awiri. 48Ndalama zimenezi uzipereke kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kuti ukhale mtengo woombolera Aisraeli woonjezerawo.”

49Choncho Mose anatenga ndalama zowombolera zija kuchokera kwa Aisraeli amene chiwerengero chawo chinaposa chiwerengero cha omwe anawomboledwa ndi Alevi. 50Anatenga masekeli a siliva okwana 1,365 molingana ndi masekeli a ku malo opatulika, kuchokera kwa ana aamuna oyamba kubadwa a Aisraeli. 51Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Числа 3:1-51

Служение левитов при шатре

1Вот родословие Хоруна и Мусо к тому времени, когда Вечный говорил с Мусо на горе Синай.

2Имена сыновей Хоруна: Надав, его первенец, и Авиуд, Элеазар и Итамар. 3Это имена сыновей Хоруна, помазанных священнослужителей, которых он посвятил, чтобы они были священнослужителями. 4Но Надав и Авиуд умерли перед Вечным, когда принесли Ему чуждый огонь3:4 См. Лев. 10:1-2. в Синайской пустыне. У них не было сыновей, и лишь Элеазар с Итамаром были священнослужителями при жизни их отца Хоруна.

5Вечный сказал Мусо:

6– Приведи род Леви и представь их священнослужителю Хоруну, чтобы они помогали ему. 7Пусть они исполняют при шатре встречи обязанности за Хоруна и за всё общество, совершая службу при священном шатре. 8Пусть они заботятся о всей утвари шатра встречи и исполняют обязанности за исроильтян, совершая службу при священном шатре. 9Отдай левитов Хоруну и его сыновьям – они должны быть полностью переданы ему из всех родов исроильтян. 10Поставь Хоруна и его сыновей, чтобы они были священнослужителями. Любой посторонний, который приблизится к святилищу, должен быть предан смерти.

11Ещё Вечный сказал Мусо:

12– Я взял левитов из всех родов исроильтян вместо первенцев мужского пола, рождённых от каждой исроильтянки. Левиты – Мои, 13потому что все первенцы – Мои. Когда Я умертвил всех первенцев в Египте, Я освятил Себе всех первенцев в Исроиле – и людей, и животных. Они должны быть Моими. Я – Вечный.

Перепись левитов

14Потом Вечный сказал Мусо в Синайской пустыне:

15– Пересчитай левитов по семьям и кланам. Пересчитай всех людей мужского пола возрастом от месяца и старше.

16И Мусо перечислил их так, как велел ему Вечный.

17Вот имена сыновей Леви:

Гершон, Кааф и Мерари.

18Вот имена кланов гершонитов:

Ливни и Шимей.

19Кланы каафитов:

Амрам, Ицхар, Хеврон и Узиил.

20Кланы мераритов:

Махли и Муши.

Вот левитские кланы по их семьям.

21От Гершона произошли кланы ливнитов и шимеитов: это кланы гершонитов. 22Всех перечисленных мужчин возрастом от месяца и старше было семь тысяч пятьсот человек. 23Кланы гершонитов должны были ставить лагерь на западе, позади священного шатра. 24Вождём семей гершонитов был Элиософ, сын Лаила. 25При шатре встречи заботе гершонитов были вверены священный шатёр и его покрытия, завеса к входу в шатёр, 26завесы двора, завеса входа во двор, который вокруг священного шатра и жертвенника, и верёвки её, со всеми их принадлежностями.

27От Каафа произошли кланы амрамитов, ицхаритов, хевронитов и узиилитов: это кланы каафитов. 28Всех мужчин возрастом от месяца и старше было восемь тысяч шестьсот3:28 В некоторых рукописях: «восемь тысяч триста», см. общее количество в ст. 39. человек. Заботе каафитов было вверено святилище. 29Каафитские кланы должны были ставить лагерь с южной стороны священного шатра. 30Вождём семей каафитских кланов был Элицафан, сын Узиила. 31Их заботе были вверены сундук3:31 Сундук – см. пояснительный словарь, а также Исх. 25:10-22., стол, светильник, жертвенники, утварь святилища, которой пользуются при служении, завеса и все принадлежности к ней. 32Главным вождём левитов был Элеазар, сын священнослужителя Хоруна. Он стоял над теми, чьей заботе было вверено святилище.

33От Мерари произошли кланы махлитов и мушитов: это кланы мераритов. 34Всех перечисленных мужчин возрастом от месяца и старше было шесть тысяч двести человек. 35Вождём семей мераритских кланов был Цуриил, сын Авихаила. Они должны были вставать лагерем с северной стороны священного шатра. 36Мераритам было велено заботиться о брусьях священного шатра, его поперечинах, столбах, основаниях, всей его оснастке со всеми принадлежностями 37и о столбах окружающего двора с их основаниями, шатровыми кольями и верёвками.

38Мусо, Хорун и его сыновья ставили лагерь к востоку от священного шатра, к восходу, перед шатром встречи. Они должны были заботиться о святилище за исроильтян. Любого постороннего, который приближался к святилищу, нужно было предать смерти.

39Всего левитов, которых Мусо и Хорун исчислили по повелению Вечного, по их кланам, всех мужчин возрастом от месяца и старше, было двадцать две тысячи человек.

Замена исроильских первенцев левитами

40Вечный сказал Мусо:

– Посчитай всех исроильских первенцев мужского пола от месяца и старше и составь список их имён. 41Я – Вечный, отдели Мне левитов вместо всех исроильских первенцев, а также весь скот левитов вместо всего первородного от скота исроильтян.

42Мусо исчислил всех первенцев других родов исроильтян, как повелел ему Вечный. 43Всего первенцев мужского пола от месяца и старше, перечисленных по именам, было двадцать две тысячи двести семьдесят три человека.

44Ещё Вечный сказал Мусо:

45– Возьми левитов вместо всех первенцев исроильтян и скот левитов вместо их скота. Левиты должны быть Моими. Я – Вечный. 46Чтобы выкупить двести семьдесят три исроильских первенца, которые превышают число левитов, 47собери за каждого по шестьдесят граммов серебра3:47 Букв.: «пять шекелей серебра, шекелей святилища, в одном шекеле двадцать гер». Шекель святилища – стандартная мера веса, которой пользовались священнослужители шатра и храма.. 48Отдай серебро за выкуп Хоруну и его сыновьям.

49Мусо собрал выкуп у тех, кто превысил число выкупленных левитами. 50У первенцев исроильтян он собрал более шестнадцати килограммов серебра3:50 Букв.: «тысяча триста шестьдесят пять шекелей серебра, шекелей святилища».. 51Мусо отдал выкуп Хоруну и его сыновьям, как ему повелел Вечный.