Numeri 3 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 3:1-51

Alevi

1Iyi ndi mbiri ya banja la Aaroni ndi Mose pa nthawi yomwe Yehova anayankhula ndi Mose pa phiri la Sinai.

2Mayina a ana aamuna a Aaroni anali Nadabu, woyamba kubadwa, Abihu, Eliezara ndi Itamara. 3Amenewa ndi mayina a ana aamuna a Aaroni, ansembe odzozedwa omwe anapatulidwa kuti azitumikira ngati ansembe. 4Koma Nadabu ndi Abihu, anagwa nafa pamaso pa Yehova pamene ankapereka nsembe ndi moto wachilendo pamaso pa Yehova mʼchipululu cha Sinai. Iwowo analibe ana aamuna. Choncho Eliezara ndi Itamara ndiwo amene ankatumikira ngati ansembe nthawi imene Aaroni abambo awo anali moyo.

5Yehova anati kwa Mose, 6“Bweretsa fuko la Levi ndipo ulipereke kwa Aaroni wansembe kuti lizimutumikira. 7Azigwira ntchito yothandiza iyeyo ndi gulu lonse ku tenti ya msonkhano pogwira ntchito ya ku Chihema. 8Azisamalira zipangizo zonse za mu tenti ya msonkhano, ndipo azigwirira ntchito Aisraeli potumikira mu tenti. 9Pereka Alevi kwa Aaroni ndi kwa ana ake aamuna. Amenewa ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwa iye kwathunthu. 10Usankhe Aaroni ndi ana ake aamuna kuti azitumikira pa ntchito ya unsembe. Koma wina aliyense woyandikira malo opatulika aphedwe.”

11Yehova anawuzanso Mose kuti, 12“Pakati pa Aisraeli onse ndatenga Alevi kulowa mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa kwa amayi a Chiisraeli. Alevi ndi anga, 13pakuti ana onse oyamba kubadwa ndi anga. Nditakantha ana onse oyamba kubadwa mu Igupto, ndinadzipatulira ndekha mwana aliyense woyamba kubadwa mu Israeli, wa munthu ndi nyama. Azikhala anga. Ine ndine Yehova.”

14Yehova anawuza Mose mʼchipululu cha Sinai kuti, 15“Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.” 16Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.

17Mayina a ana aamuna a Levi ndi awa:

Geresoni, Kohati ndi Merari.

18Mayina a ana a Geresoni potsata mabanja awo ndi awa:

Libini ndi Simei.

19Ana a Kohati potsata mabanja awo ndi awa:

Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli.

20Ana a Merari potsata mabanja awo ndi awa:

Mali ndi Musi.

Amenewa ndiwo anali mabanja a Alevi monga mwa makolo awo.

21Kwa Geresoni kunali banja la Alibini, banja la Asimei. Amenewa ndiwo anali mabanja a Ageresoni. 22Chiwerengero cha amuna onse amene anawawerenga a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 7,500. 23Mabanja a Ageresoni azimanga misasa yawo kumadzulo, kumbuyo kwa Chihema. 24Mtsogoleri wa mabanja a Ageresoni anali Eliyasafu mwana wa Laeli. 25Ntchito imene Ageresoni anapatsidwa ku tenti ya msonkhano inali yosamalira Chihema ndi tenti, pamodzi ndi zophimbira zake, katani ya pa khomo la ku tenti ya msonkhano, 26ndi makatani wotchinga bwalo, katani ya pa chipata cholowera ku bwalo lozungulira Chihema ndi guwa lansembe, zingwe ndi zonse zokhudzana ndi ntchito yawo.

27Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati. 28Chiwerengero cha amuna onse a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 8,600. Akohati ankagwira ntchito yosamalira malo wopatulika. 29Mabanja a ana a Kohati ankamanga misasa yawo kummwera kwa Chihema. 30Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Kohati anali Elizafani mwana wa Uzieli. 31Iwo ankagwira ntchito yosamalira Bokosi la Chipangano, tebulo, choyikapo nyale, maguwa, zipangizo za kumalo wopatulika zimene ansembe ankagwiritsa ntchito, katani, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito. 32Mtsogoleri wamkulu wa Alevi anali Eliezara mwana wa Aaroni wansembe. Iye anasankhidwa kukhala woyangʼanira omwe ankasamalira malo wopatulika.

33Kwa Merari kunali banja la Mali ndi banja la Musi. Amenewa ndiye anali mabanja a Amerari. 34Chiwerengero cha amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 6,200. 35Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Amerari anali Zuriyeli mwana wa Abihaili. Iwo ankamanga misasa yawo kumpoto kwa Chihema. 36Amerari anapatsidwa ntchito yosamalira mitengo ya chihema, nsichi zake, mizati yake, matsinde ake, ndi zida zake zonse, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito, 37pamodzi ndi mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema ndi zingwe zake.

38Mose ndi Aaroni ndi ana ake aamuna ankamanga misasa yawo kummawa kwa chihema, kuyangʼana kotulukira dzuwa, kutsogolo kwa tenti ya msonkhano. Anali ndi ntchito yosamalira malo wopatulika mʼmalo mwa Aisraeli. Aliyense woyandikira malo wopatulika ankayenera kuphedwa.

39Alevi onse amene Mose ndi Aaroni anawawerenga potsatira lamulo la Yehova monga mwa magulu a mabanja awo, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo anali 22,000.

40Yehova anawuza Mose kuti, “Werenga ana onse aamuna oyamba kubadwa mu Israeli, omwe ali ndi mwezi umodzi kapena kupitirirapo ndipo ulembe mndandanda wa mayina awo. 41Unditengere Alevi onse mʼmalo mwa ana oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso ziweto zazimuna za Alevi mʼmalo mwa ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa za Aisraeli. Ine ndine Yehova.”

42Choncho Mose anawerenga ana aamuna onse oyamba kubadwa a Aisraeli monga momwe Yehova anamulamulira. 43Chiwerengero chonse cha ana aamuna oyamba kubadwa kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 22, 273.

44Ndipo Yehova anawuzanso Mose kuti, 45“Tenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso zoweta zonse za Alevi mʼmalo mwa zoweta za Aisraeli. Alevi ndi anga. Ine ndine Yehova. 46Pofuna kuwombola ana aamuna 273 oyamba kubadwa a Aisraeli amene anaposa chiwerengero cha aamuna a fuko la Levi, 47utenge masekeli asanu pa munthu aliyense. Masekeliwo akhale ofanana ndi masekeli a ku malo wopatulika, kumene sekeli imodzi imakwanira magera makumi awiri. 48Ndalama zimenezi uzipereke kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kuti ukhale mtengo woombolera Aisraeli woonjezerawo.”

49Choncho Mose anatenga ndalama zowombolera zija kuchokera kwa Aisraeli amene chiwerengero chawo chinaposa chiwerengero cha omwe anawomboledwa ndi Alevi. 50Anatenga masekeli a siliva okwana 1,365 molingana ndi masekeli a ku malo opatulika, kuchokera kwa ana aamuna oyamba kubadwa a Aisraeli. 51Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.

La Bible du Semeur

Nombres 3:1-51

Les prêtres

1Voici la liste des descendants d’Aaron et de Moïse à l’époque où l’Eternel s’adressa à Moïse sur le mont Sinaï.

2Voici les noms des fils d’Aaron : l’aîné s’appelait Nadab, puis vinrent Abihou, Eléazar et Itamar. 3Ils étaient prêtres ayant reçu l’onction pour être investis de la fonction sacerdotale. 4Mais Nadab et Abihou moururent devant l’Eternel, dans le désert du Sinaï, parce qu’ils lui avaient présenté un feu profane ; ils n’avaient pas eu d’enfants. Eléazar et Itamar exercèrent le ministère sacerdotal sous la supervision de leur père Aaron3.4 Voir Lv 10.1-7..

Les lévites, au service des prêtres

5L’Eternel parla à Moïse en ces termes : 6Fais venir la tribu de Lévi et mets ses membres à la disposition du prêtre Aaron pour qu’ils l’assistent3.6 Les lévites sont clairement distingués des prêtres, descendants d’Aaron (qui forment une branche des lévites). Ils seront les assistants, les aides des prêtres, mais n’accompliront pas toutes leurs fonctions.. 7Ils seront à son service et au service de toute la communauté devant la tente de la Rencontre, pour accomplir les tâches relatives au tabernacle. 8Ils prendront soin de tous les ustensiles de la tente de la Rencontre et seront au service des Israélites pour accomplir les tâches relatives au tabernacle. 9Donc, tu mettras les lévites à la disposition d’Aaron et de ses fils ; ils lui3.9 Certains manuscrits du texte hébreu traditionnel, le Pentateuque samaritain et l’ancienne version grecque ont : me. seront attribués comme représentants des Israélites. 10Tu veilleras à ce qu’Aaron et ses fils exercent les fonctions sacerdotales ; celui qui ne serait pas de leur famille et qui s’approcherait du tabernacle sera puni de mort.

11L’Eternel parla encore à Moïse en ces termes : 12Voici : j’ai choisi les lévites du milieu des Israélites à la place de tous les premiers-nés des mères israélites ; ils m’appartiennent donc. 13Tout premier-né m’appartient en effet, depuis le jour où j’ai fait mourir tous les premiers-nés des Egyptiens et où je me suis consacré tout premier-né en Israël, tant ceux des hommes que ceux des animaux. Ils sont à moi. Je suis l’Eternel3.13 Voir Ex 13.1-16..

Le recensement, le campement et les fonctions des lévites

14Là-dessus, l’Eternel commanda à Moïse, au désert du Sinaï : 15Fais le recensement des descendants de Lévi, selon leurs groupes familiaux et leurs familles ; tu compteras tous les lévites de sexe masculin de l’âge d’un mois et plus3.15 Les lévites ne devaient pas faire de service militaire ; c’est pourquoi ils ne sont pas comptés à partir de vingt ans comme les autres Israélites. Ce recensement sert à déterminer le rapport de leur nombre avec celui des premiers-nés (voir v. 40-51)..

16Moïse fit ce recensement sur l’ordre de l’Eternel de la manière qu’il lui avait prescrite.

17Voici les noms des fils de Lévi : Guershôn, Qehath et Merari. 18Guershôn avait pour fils Libni et Shimeï, qui ont donné leurs noms à leurs familles. 19Qehath eut pour fils Amram et Yitsehar, Hébron et Ouzziel qui ont donné leur nom à leur famille. 20Merari eut pour fils Mahli et Moushi qui ont donné leur nom à leur famille. Telles sont les familles des groupes familiaux de Lévi.

21Les descendants de Guershôn comprennent la famille de Libni et celle de Shimeï, qui représentent les familles guershonites. 22Elles comptaient au moment du recensement 7 500 membres de sexe masculin, âgés d’un mois et plus. 23Les familles guershonites campaient derrière le tabernacle, du côté ouest. 24Le chef de leur groupe familial était Eliasaph, fils de Laël. 25Dans la tente de la Rencontre, ils avaient la responsabilité du tabernacle et de la tenture qui le recouvrait, du rideau de l’entrée de la tente, 26des tentures du parvis qui entoure le tabernacle et l’autel, et de sa porte d’entrée ainsi que des cordages. Ils étaient chargés de tous les travaux liés à ces objets.

27De Qehath sont issues les familles des Amramites, des Yitseharites, des Hébronites et des Ouzziélites, qui représentent les familles qehatites. 28Elles comptaient 8 6003.28 L’ancienne version grecque porte 8 300, ce qui s’accorde avec le total donné au v. 39. membres de sexe masculin de plus d’un mois. Ils étaient affectés au service du sanctuaire 29et campaient du côté sud de la Demeure. 30Leur chef était Elitsaphân, fils d’Ouzziel. 31On avait confié à leur responsabilité : le coffre, la table, le chandelier, les autels, les objets sacrés dont on se sert pour officier, et le voile3.31 Séparant le lieu saint du lieu très saint.. Ils étaient chargés de tous les travaux liés à ces objets.

32Le chef suprême des lévites était Eléazar, fils du prêtre Aaron. Il supervisait les lévites préposés au service du sanctuaire. 33De Merari sont issues la famille de Mahli et celle de Moushi. 34Ils étaient 6 200 de sexe masculin âgés de plus d’un mois. 35Le chef du groupe familial et des familles de Merari était Tsouriel, fils d’Abihaïl. Ils campaient du côté nord de la Demeure. 36Les Merarites étaient responsables des planches du tabernacle, de ses traverses, de ses piliers, de leurs socles et de tous les ustensiles, pour accomplir tous les travaux relatifs à ces objets. 37Ils avaient aussi la charge des piliers autour du parvis avec leurs socles, leurs piquets et leurs cordages.

38Moïse, Aaron et ses fils campaient devant le tabernacle, à l’est, devant la tente de la Rencontre. Ils étaient chargés du service du sanctuaire au nom des Israélites. Toute personne profane qui s’en serait approchée comme eux devait être mise à mort.

39Le nombre total des lévites de sexe masculin d’un mois et plus, recensés par Moïse et Aaron sur l’ordre de l’Eternel et par familles, était de 22 000.

Le rachat des fils aînés

40L’Eternel dit à Moïse : Fais à présent le recensement de tous les fils aînés parmi les Israélites depuis l’âge d’un mois et au-dessus, en dressant leur liste nominative. 41A leur place, tu m’attribueras les lévites – je suis l’Eternel. Le bétail des lévites m’appartiendra aussi en échange de tous les premiers-nés du bétail des Israélites.

42Moïse fit le recensement de tous les fils aînés des Israélites selon l’ordre que l’Eternel lui avait donné. 43Le total des fils aînés âgés d’au moins un mois et dont il enregistra les noms était de 22 273.

44L’Eternel parla à Moïse et dit : 45Attribue-moi les lévites en échange de tous les fils aînés des Israélites, et le bétail des lévites à la place du leur, ainsi les lévites seront à moi. Je suis l’Eternel. 46Pour le rachat des 273 fils aînés en surplus par rapport au nombre des lévites, 47tu feras payer cinq pièces d’argent par tête au taux du sicle utilisé au sanctuaire, qui pèse vingt guéras3.47 C’est-à-dire douze grammes. Comme il existait plusieurs systèmes de poids et mesures, il est précisé ici que c’est le système du sanctuaire qui est seul valable pour cette transaction. Le guéra valait environ 0,6 grammes d’argent ; le sicle pesait donc environ 12 grammes. Cette rançon constituera un revenu régulier pour les prêtres (voir 18.16).. 48Tu donneras l’argent à Aaron et à ses fils comme prix du rachat de ceux qui sont en surplus par rapport au nombre des lévites.

49Moïse reçut l’argent du rachat pour ceux qui étaient en excédent sur le nombre des fils aînés rachetés par les lévites ; 50il reçut de la part des fils aînés israélites la somme de 1 365 sicles au taux du sicle en vigueur au sanctuaire. 51Il remit l’argent du rachat à Aaron et à ses fils, selon l’ordre que l’Eternel lui avait donné.