Numeri 28 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 28:1-31

Zopereka za Tsiku ndi Tsiku

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’ 3Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema. 4Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo. 5Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi. 6Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova. 7Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova. 8Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’ ”

Zopereka za pa Sabata

9“ ‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. 10Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’ ”

Zopereka za pa Mwezi

11“Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema. 12Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; 13ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova. 14Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka. 15Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.

Paska

16“ ‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova. 17Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri. 18Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. 19Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema. 20Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse. 21Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja. 22Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu. 23Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa. 24Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa. 25Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.

Madyerero a Masabata

26“ ‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. 27Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova. 28Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri. 29Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi. 30Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu. 31Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.

New Serbian Translation

4. Мојсијева 28:1-31

Дневни приноси

1Господ рече Мојсију: 2„Заповеди Израиљцима и реци им: ’Пазите да приносите мој принос, храну за моју паљену жртву, мој угодни мирис, у време које је одређено за њега.’ 3Реци им: ’Ово је паљена жртва коју ћете приносити Господу: дневно два јагњета од годину дана, без мане, као трајну жртву свеспалницу. 4Једно јагње принеси ујутро, а друго принеси увече. 5Уз то, умешај десетину ефе28,5 Око 1,6 kg. брашна с четврт хина28,5 Око 1 l. чистог, свеже исцеђеног уља. 6То је трајна жртва свеспалница установљена на гори Синај, на угодни мирис – паљену жртву Господу. 7Жртва изливница ће бити четврт хина жестоког пића за свако јагње. Нека се жртва изливница Господу излије у Светињи. 8Друго јагње принеси увече. С њим принеси исту житну жртву као ујутро, и жртву изливницу на угодни мирис, паљену жртву Господу.

Суботње жртве

9На суботњи дан принеси два јагњета од годину дана, без мане, две десетине ефе брашна умешеног са уљем за житну жртву, и жртву изливницу која иде уз њу. 10То је жртва свеспалница за сваку суботу, поред свакодневне жртве свеспалнице и жртве изливнице која иде уз њу.

Месечне жртве

11На почетку ваших месеци принесите жртву свеспалницу Господу: два јунца, два овна и седам јагањаца од годину дана без мане. 12Житна жртва уз сваког јунца биће: три десетине ефе брашна умешеног с уљем. Житна жртва уз сваког овна биће: две десетине брашна умешеног с уљем. 13Житна жртва уз свако јагње биће: две десетине брашна умешеног с уљем. То је жртва свеспалница – паљена жртва на угодан мирис Господу. 14Жртва изливница која иде уз њих биће: пола хина28,14 Око 2 l. вина за сваког јунца, једна трећина хина28,14 Око 1,3 l. вина за овна, и једна четвртина хина28,14 Око 1 l. вина за јагње. То је жртва свеспалница за сваки нови месец током месеци у години. 15Уз свакодневну свеспалницу, нека се Господу приноси један јарац као жртва за грех, уз жртву изливницу која иде с њом.

Жртве за Пасху

16Првога месеца, четрнаестог дана у месецу почиње Пасха Господња. 17А петнаестога дана истог месеца је празник. Једите бесквасне хлебове седам дана. 18Првога дана одржавајте свети сабор; не радите никаквог свакодневног посла. 19Као паљену жртву, свеспалницу, принесите Господу два јунца, једног овна и седам јагањаца од годину дана, без мане. 20Житна жртва која иде уз њих биће: три десетине ефе брашна умешеног с уљем за сваког јунца, две десетине за овна, 21а једну десетину принеси за сваког од седам јагањаца. 22Такође, принеси и једног јарца, жртву за грех, да се изврши откупљење за вас. 23Ово приносите поред јутарње жртве свеспалнице која се свакодневно приноси. 24Овако ћете чинити сваки дан за седам дана. То је паљена жртва, угодни мирис Господу. Нека се то приноси уз свакодневну жртву свеспалницу и уз жртву изливницу која иде с њом. 25А седмога дана нека вам буде свети сабор: не радите никакав посао.

Жртве за празник Седмица

26На дан првина, приликом вашег празника Седмица, кад принесете Господу житну жртву од нове жетве, одржавајте свети сабор. Не радите никакав свакодневни посао! 27За жртву свеспалницу на угодан мирис Господу принесите два јунца, једног овна и седам јагањаца од годину дана. 28Житна жртва која иде уз њих биће: три десетине ефе брашна умешеног с уљем за сваког јунца, две десетине за овна, 29а једну десетину за сваког од седам јагањаца; 30и једног јарца, да се изврши откупљење за вас. 31Поред свакодневне жртве свеспалнице, и житне жртве која иде уз њу, принесите уз њу и жртву изливницу. Нека вам буду без мане.