Numeri 28 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 28:1-31

Zopereka za Tsiku ndi Tsiku

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’ 3Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema. 4Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo. 5Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi. 6Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova. 7Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova. 8Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’ ”

Zopereka za pa Sabata

9“ ‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. 10Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’ ”

Zopereka za pa Mwezi

11“Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema. 12Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; 13ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova. 14Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka. 15Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.

Paska

16“ ‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova. 17Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri. 18Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. 19Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema. 20Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse. 21Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja. 22Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu. 23Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa. 24Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa. 25Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.

Madyerero a Masabata

26“ ‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. 27Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova. 28Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri. 29Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi. 30Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu. 31Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Числа 28:1-31

Ежедневные жертвоприношения

(Исх. 29:38-42)

1Вечный сказал Мусо:

2– Дай исроильтянам повеление, скажи им: «Следите, чтобы приносили Мне в должное время пищу для Моих огненных жертв, чьё благоухание приятно Мне». 3Скажи им: «Вот огненная жертва, которую вы должны совершать Вечному: два годовалых ягнёнка без изъяна для постоянного всесожжения ежедневно, 4одного утром, а другого вечером, 5вместе с хлебным приношением из полутора килограммов28:5 Букв.: «одна десятая ефы». лучшей муки, смешанной с одним литром28:5 Букв.: «четверть гина», также в ст. 7. оливкового масла. 6Это постоянное всесожжение, принятое у горы Синай, приятное благоухание, огненная жертва Вечному. 7Пусть с каждым ягнёнком совершается жертвенное возлияние из одного литра вина. Выливайте жертвенное возлияние Вечному у святилища. 8Другого ягнёнка приносите вечером с таким же хлебным приношением и жертвенным возлиянием, как и утром. Это огненная жертва, благоухание, приятное Вечному.

Субботние приношения

9В субботу приносите двух годовалых ягнят без изъяна с жертвенными возлияниями при них и хлебным приношением из трёх килограммов28:9 Букв.: «две десятых ефы». лучшей муки, смешанной с маслом. 10Таково всесожжение на каждую субботу, не считая постоянного всесожжения с жертвенным возлиянием при нём.

Ежемесячные приношения

11В первый день каждого месяца приносите Вечному всесожжение из двух молодых быков, одного барана и семи годовалых ягнят без изъяна. 12Хлебное приношение при каждом быке пусть будет из четырёх с половиной килограммов лучшей муки, смешанной с маслом; при баране – из трёх килограммов лучшей муки, смешанной с маслом; 13а при ягнёнке – из полутора килограммов28:12-13 Букв.: «три десятых ефы… две десятых ефы… одна десятая ефы»; также в ст. 28:20-21, 28-29; 29:3-4, 9-10, 14-15. лучшей муки, смешанной с маслом. Это для всесожжения, приятного благоухания, огненной жертвы Вечному. 14Жертвенное возлияние при каждом быке пусть будет из двух литров: при баране – из одного литра с четвертью; а при ягнёнке – из одного литра28:14 Букв.: «полгина… треть гина… четверть гина». вина. Это ежемесячное всесожжение, которое нужно совершать каждое новолуние28:14 Исроильтяне, пользовавшиеся лунным календарём, праздновали начало каждого месяца, которое совпадало с новолунием. круглый год. 15Кроме постоянного всесожжения с положенным жертвенным возлиянием нужно приносить Вечному одного козла в жертву за грех.

Праздник Освобождения и праздник Пресных хлебов

(Исх. 12:14-20; Лев. 23:5-8; Втор. 16:1-8)

16В четырнадцатый день первого месяца (ранней весной) будет жертвенное приношение исроильтян Вечному в память об их освобождении из-под египетского гнёта. 17На следующий день пусть будет праздник; семь дней ешьте пресный хлеб. 18В первый день созывайте священное собрание и не занимайтесь ничем из обычных дел. 19Приносите Вечному огненную жертву, всесожжение из двух молодых быков, одного барана и семи годовалых ягнят без изъяна. 20При каждом быке приносите хлебное приношение из четырёх с половиной килограммов лучшей муки, смешанной с маслом; при баране – из трёх килограммов; 21а при каждом из семи ягнят – из полутора килограммов. 22Прибавляйте одного козла в жертву за грех, для вашего очищения. 23Приносите это, не считая постоянного утреннего всесожжения. 24Так же приносите ежедневно, семь дней, пищу для огненной жертвы, благоухания, приятного Вечному. Его нужно приносить сверх постоянного всесожжения с положенным жертвенным возлиянием. 25На седьмой день созывайте священное собрание и не занимайтесь ничем из обычных дел.

Праздник Жатвы

(Лев. 23:15-22; Втор. 16:9-12)

26В день первых плодов, когда вы совершаете Вечному приношение из нового зерна на празднике Жатвы, созывайте священное собрание и не занимайтесь ничем из обычных дел. 27Приносите всесожжение из двух молодых быков, одного барана и семи годовалых ягнят для благоухания, приятного Вечному. 28Пусть хлебное приношение при каждом быке будет из четырёх с половиной килограммов лучшей муки, смешанной с маслом; при баране – из трёх килограммов; 29а при каждом из семи ягнят – из полутора килограммов. 30Прибавляйте одного козла для вашего очищения. 31Приносите это с положенными жертвенными возлияниями сверх постоянного всесожжения с положенным хлебным приношением. Пусть животные для жертвы будут у вас без изъяна.