Numeri 28 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 28:1-31

Zopereka za Tsiku ndi Tsiku

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’ 3Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema. 4Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo. 5Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi. 6Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova. 7Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova. 8Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’ ”

Zopereka za pa Sabata

9“ ‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. 10Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’ ”

Zopereka za pa Mwezi

11“Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema. 12Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; 13ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova. 14Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka. 15Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.

Paska

16“ ‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova. 17Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri. 18Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. 19Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema. 20Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse. 21Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja. 22Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu. 23Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa. 24Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa. 25Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.

Madyerero a Masabata

26“ ‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. 27Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova. 28Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri. 29Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi. 30Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu. 31Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.

Bibelen på hverdagsdansk

4. Mosebog 28:1-31

De daglige ofre

1Herren sagde til Moses: 2„Indskærp over for israelitterne, at de skal bringe de forskellige ofre på de fastsatte tidspunkter. Jeg glæder mig over røgen fra disse ofre.

3Det daglige brændoffer består af to etårs vædderlam uden skavanker. 4Det ene lam skal ofres om morgenen og det andet lige før solnedgang. 5Sammen med hvert lam skal der ofres et afgrødeoffer bestående af to liter fintmalet mel blandet med en liter olivenolie. 6Det er det daglige offer, som blev indstiftet på Sinaibjerget, et brændoffer med en liflig duft for Herren. 7Desuden skal I sammen med hvert lam ofre et drikoffer på en liter øl. Drikofferet skal udgydes for Herren i helligdommen. 8Om aftenen skal I ofre det andet lam med et tilsvarende afgrødeoffer og drikoffer. Disse ofre vil frembringe en liflig duft for Herren.

Sabbatsofferet

9-10På sabbatsdagen skal der i tilknytning til de daglige morgen- og aftenbrændofre med tilhørende drikofre bringes et ekstra brændoffer på to etårs vædderlam uden skavanker. Det skal ledsages af et afgrødeoffer på fire liter fint mel blandet med olivenolie med tilhørende drikoffer.

Det månedlige offer

11På den første dag i hver måned skal I ofre et særligt brændoffer til Herren bestående af to unge tyre, en vædder og syv etårs vædderlam, alle uden skavanker. 12Sammen med hvert dyr skal I ofre et afgrødeoffer: seks liter fint mel blandet med olivenolie for hver tyr, fire liter fint mel blandet med olivenolie for hver vædder, 13og to liter fint mel blandet med olivenolie for hvert lam.28,13 På hebraisk henholdsvis 3 tiendedele, 2 tiendedele og en tiendedel efa, hvor en efa er ca. 22 liter. Det samme i vers 20 og 28. Dette er et lifligt brændoffer for Herren. 14Hvert offer skal ledsages af et drikoffer bestående af to liter vin for hver tyr, godt en liter vin for hver vædder og knap en liter vin for hvert lam. Dette brændoffer skal I bringe Herren på den første dag i måneden hele året igennem. 15Desuden skal I ofre en gedebuk som syndoffer for Herren. Alt dette er ud over det daglige brændoffer og drikoffer.

Påskeofferet

16Den 14. dag i den første måned skal I fejre påskehøjtid til ære for Herren. 17Den følgende dag begynder den ugelange fest, og i det tidsrum må I under ingen omstændigheder spise brød, der er bagt med surdej. 18På festens første dag skal I hvile fra jeres daglige arbejde og samles for Herrens ansigt. 19Ved den lejlighed skal I ofre to unge tyre, en vædder og syv etårs vædderlam, alle uden skavanker, som brændofre til Herren. 20-21Med hvert dyr skal der ofres et afgrødeoffer: seks liter fint mel blandet med olivenolie for hver tyr, fire liter fint mel blandet med olivenolie for hver vædder, og to liter fint mel blandet med olivenolie for hvert lam. 22Desuden skal der ofres en gedebuk til soning for jeres synder. 23Disse ofre er ud over de daglige morgenbrændofre. 24Tilsvarende ofre skal I bringe på hver af de syv dage, festen varer, som liflige ofre for Herren. 25På festens syvende dag skal I atter lade det daglige arbejde hvile og samles for Herrens ansigt.

Høstofferet

26Under høstfesten28,26 Dvs. hvedehøsten. Denne fest blev senere kaldt pinsefesten, men er bedst kendt under navnet ugefesten, fordi den blev afholdt syv hele uger efter festen for den første byghøst, der blev holdt dagen efter sabbatten under de usyrnede brøds fest, der fulgte umiddelbart efter påskedagen. Se 3.Mos. 23,15ff. skal I også hvile fra det daglige arbejde og samles for Herrens ansigt. På den dag skal I ofre den første afgrøde til Herren. 27Som brændoffer skal I ofre to unge tyre, en vædder og syv etårs vædderlam. 28Som afgrødeoffer skal I ofre seks liter fint mel blandet med olivenolie for hver tyr, fire liter for hver vædder 29og to liter for hvert lam. 30Ved samme lejlighed skal der ofres en gedebuk som soning for jeres synder. 31På den dag skal I stadig ofre de daglige brændofre, afgrødeofre og drikofre ved siden af de særlige brændofre med tilhørende drikofre. Sørg altid for at ofre dyr uden skavanker.