Numeri 26 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 26:1-65

Kalembera Wachiwiri

1Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni, 2“Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.” 3Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti, 4“Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.”

Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:

5Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi:

kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki;

kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;

6kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi;

kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.

7Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.

8Mwana wa Palu anali Eliabu, 9ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova. 10Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo. 11Koma ana a Kora sanafe nawo.

12Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele;

kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini;

kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;

13kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera;

kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.

14Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.

15Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi:

kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni;

kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi;

kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;

16kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini;

kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;

17kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi;

kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.

18Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.

19Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.

20Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Sela, fuko la Asera;

kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi;

kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.

21Zidzukulu za Perezi zinali izi:

kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi;

kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.

22Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.

23Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Tola, fuko la Atola;

kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;

24kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu.

Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.

25Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.

26Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi;

kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni;

kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.

27Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.

28Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:

29Zidzukulu za Manase:

kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi);

kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.

30Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi;

kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri;

kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;

31kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli;

kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;

32kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida;

kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.

33(Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)

34Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.

35Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi;

kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela;

kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri;

kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.

36Zidzukulu za Sutela zinali izi:

kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.

37Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500.

Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.

38Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi:

kuchokera mwa Bela, fuko la Abela;

kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli;

kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;

39kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu;

kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;

40Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi:

kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi;

kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;

41Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.

42Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi:

kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu.

Izi zinali zidzukulu za Dani. 43Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.

44Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna;

kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi;

kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;

45ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya:

kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi;

kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;

46(Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)

47Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.

48Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli;

kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;

49kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri;

kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.

50Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.

51Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.

52Yehova anawuza Mose kuti, 53“Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo. 54Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa. 55Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo. 56Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”

57Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa:

kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni;

kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati;

kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.

58Awanso anali mabanja a Alevi:

banja la Alibini,

banja la Ahebroni,

banja la Amali,

banja la Amusi, fuko la Kora

banja la Akohati,

(Kohati anali abambo a Amramu. 59Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo. 60Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara. 61Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).

62Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.

63Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko. 64Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai; 65Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.

Thai New Contemporary Bible

กันดารวิถี 26:1-65

สำมะโนประชากรครั้งที่สอง

1หลังจากภัยพิบัติยุติลงแล้ว องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสกับโมเสสและเอเลอาซาร์บุตรปุโรหิตอาโรนว่า 2“จงทำสำมะโนประชากรชายทุกคนในอิสราเอลที่มีอายุยี่สิบปีขึ้นไป เพื่อสำรวจว่าในแต่ละครอบครัวมีใครบ้างที่สามารถออกรบได้” 3ดังนั้นโมเสสและปุโรหิตเอเลอาซาร์จึงแจ้งพวกเขาขณะตั้งค่ายอยู่ในที่ราบโมอับริมแม่น้ำจอร์แดนตรงข้ามเมืองเยรีโค26:3 ภาษาฮีบรูว่าจอร์แดนแห่งเยรีโคอาจจะเป็นชื่อโบราณของแม่น้ำจอร์แดน เช่นเดียวกับข้อ 63ว่า 4“จงทำสำมะโนประชากรชายอายุยี่สิบปีขึ้นไปตามที่องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสสั่งโมเสส”

ชนอิสราเอลที่ออกมาจากอียิปต์ ได้แก่

5วงศ์วานของรูเบนบุตรหัวปีของอิสราเอลได้แก่

ตระกูลฮาโนคจากฮาโนค

ตระกูลปัลลูจากปัลลู

6ตระกูลเฮสโรนจากเฮสโรน

ตระกูลคารมีจากคารมี

7ทั้งหมดนี้คือตระกูลต่างๆ ของรูเบน นับได้ 43,730 คน

8บุตรชายของปัลลูคือเอลีอับ 9และบุตรชายของเอลีอับคือ เนมูเอล ดาธาน และอาบีรัม ดาธานและอาบีรัมนี้เป็นเจ้าหน้าที่ของชุมชนซึ่งได้กบฏต่อโมเสสและต่ออาโรน และเป็นพรรคพวกของโคราห์เมื่อเขากบฏต่อองค์พระผู้เป็นเจ้า 10พื้นธรณีแยกออกและสูบพวกเขาลงไปพร้อมกับโคราห์ และพรรคพวกของเขา 250 คนถูกไฟคลอกตาย และนั่นเป็นเครื่องเตือนเหล่าประชากร 11แต่เชื้อสายโคราห์ไม่ได้สูญสิ้นไป

12วงศ์วานของสิเมโอนแยกตามตระกูล ได้แก่

ตระกูลเนมูเอลจากเนมูเอล

ตระกูลยามีนจากยามีน

ตระกูลยาคีนจากยาคีน

13ตระกูลเศราห์จากเศราห์

และตระกูลชาอูลจากชาอูล

14ทั้งหมดนี้คือตระกูลต่างๆ ของสิเมโอน นับได้ 22,200 คน

15วงศ์วานของกาดแยกตามตระกูล ได้แก่

ตระกูลเศโฟนจากเศโฟน

ตระกูลฮักกีจากฮักกี

ตระกูลชูนีจากชูนี

16ตระกูลโอสนีจากโอสนี

ตระกูลเอรีจากเอรี

17ตระกูลอาโรดี26:17 ฉบับ MT. ว่าอาโรดจากอาโรดี

และตระกูลอาเรลีจากอาเรลี

18ทั้งหมดนี้คือตระกูลต่างๆ ของกาด นับได้ 40,500 คน

19เอร์และโอนันบุตรชายของยูดาห์เสียชีวิตที่คานาอัน

20วงศ์วานของยูดาห์แยกตามตระกูล ได้แก่

ตระกูลเชลาห์จากเชลาห์

ตระกูลเปเรศจากเปเรศ

ตระกูลเศราห์จากเศราห์

21วงศ์วานของเปเรศ ได้แก่

ตระกูลเฮสโรนจากเฮสโรน

และตระกูลฮามูลจากฮามูล

22ทั้งหมดนี้คือตระกูลต่างๆ ของยูดาห์ นับได้ 76,500 คน

23วงศ์วานของอิสสาคาร์แยกตามตระกูล ได้แก่

ตระกูลโทลาจากโทลา

ตระกูลปูวาห์จากปูวาห์

24ตระกูลยาชูบจากยาชูบ

และตระกูลชิมโรนจากชิมโรน

25ทั้งหมดนี้คือตระกูลต่างๆ ของอิสสาคาร์ นับได้ 64,300 คน

26วงศ์วานของเศบูลุน แยกตามตระกูลได้แก่

ตระกูลเสเรดจากเสเรด

ตระกูลเอโลนจากเอโลน

และตระกูลยาเลเอลจากยาเลเอล

27ทั้งหมดนี้คือตระกูลต่างๆ ของเศบูลุน นับได้ 60,500 คน

28วงศ์วานของโยเซฟแยกตามตระกูลนับตามมนัสเสห์และเอฟราอิมคือ

29วงศ์วานของมนัสเสห์ ได้แก่

ตระกูลมาคีร์จากมาคีร์

(มาคีร์เป็นบิดาของกิเลอาด)

ตระกูลกิเลอาดจากกิเลอาด

30วงศ์วานของกิเลอาด ได้แก่

ตระกูลอีเยเซอร์จากอีเยเซอร์

ตระกูลเฮเลคจากเฮเลค

31ตระกูลอัสรีเอลจากอัสรีเอล

ตระกูลเชเคมจากเชเคม

32ตระกูลเชมิดาจากเชมิดา

และตระกูลเฮเฟอร์จากเฮเฟอร์

33(เศโลเฟหัดบุตรเฮเฟอร์ไม่มีบุตรชาย

มีแต่บุตรสาวได้แก่ มาห์ลาห์ โนอาห์ โฮกลาห์ มิลคาห์และทีรซาห์)

34ทั้งหมดนี้คือตระกูลต่างๆ ของมนัสเสห์ นับได้ 52,700 คน

35วงศ์วานของเอฟราอิมแยกตามตระกูล ได้แก่

ตระกูลชูเธลาห์จากชูเธลาห์

ตระกูลเบเคอร์จากเบเคอร์

ตระกูลทาหานจากทาหาน

36วงศ์วานของชูเธลาห์คือ

ตระกูลเอรานจากเอราน

37ทั้งหมดนี้คือตระกูลต่างๆ ของเอฟราอิมนับได้ 32,500 คน

ทั้งหมดนี้คือวงศ์วานของโยเซฟแยกตามตระกูล

38วงศ์วานของเบนยามินแยกตามตระกูล ได้แก่

ตระกูลเบลาจากเบลา

ตระกูลอัชเบลจากอัชเบล

ตระกูลอาหิรัมจากอาหิรัม

39ตระกูลชูฟาม26:39 สำเนาฉบับ MT.ส่วนมากว่าเชฟูฟามจากชูฟาม

และตระกูลหุฟามจากหุฟาม

40วงศ์วานของเบลาทางอาร์ดและนาอามาน ได้แก่

ตระกูลอาร์ดจากอาร์ด26:40 ฉบับ MT. ไม่มีวลีว่าจากอาร์ด

และตระกูลนาอามานจากนาอามาน

41ทั้งหมดนี้คือตระกูลต่างๆ ของเบนยามิน นับได้ 45,600 คน

42วงศ์วานของดานแยกตามตระกูลคือ

ตระกูลชูฮัมจากชูฮัม

นี่คือตระกูลของดาน 43ทั้งหมดล้วนอยู่ในตระกูลชูฮัม รวม 64,400 คน

44วงศ์วานของอาเชอร์แยกตามตระกูล ได้แก่

ตระกูลอิมนาห์จากอิมนาห์

ตระกูลอิชวีจากอิชวี

ตระกูลเบรียาห์จากเบรียาห์

45และวงศ์วานของตระกูลเบรียาห์ ได้แก่

ตระกูลเฮเบอร์จากเฮเบอร์

ตระกูลมัลคีเอลจากมัลคีเอล

46(อาเชอร์มีบุตรสาวคนหนึ่งชื่อเสราห์)

47ทั้งหมดนี้คือตระกูลต่างๆ ของอาเชอร์นับได้ 53,400 คน

48วงศ์วานของนัฟทาลีแยกตามตระกูล ได้แก่

ตระกูลยาเซเอลจากยาเซเอล

ตระกูลกูนีจากกูนี

49ตระกูลเยเซอร์จากเยเซอร์

ตระกูลชิลเลมจากชิลเลม

50ทั้งหมดนี้คือตระกูลต่างๆ ของนัฟทาลีนับได้ 45,400 คน

51รวมพลอิสราเอลทั้งหมดได้ 601,730 คน

52องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสสั่งโมเสสว่า 53“จงแบ่งดินแดนแก่เผ่าต่างๆ ตามสัดส่วนจำนวนคนที่นับได้ 54เผ่าใหญ่ได้รับที่ดินมาก และเผ่าที่เล็กกว่าได้รับที่ดินน้อยลงตามส่วน และแต่ละกลุ่มจะได้รับมรดกตามจำนวนรายชื่อที่ขึ้นทะเบียนไว้ 55ให้จับฉลากแบ่งดินแดน แต่ละกลุ่มได้ครองกรรมสิทธิ์ตามจำนวนรายชื่อเผ่าบรรพบุรุษ 56แบ่งสรรกรรมสิทธิ์โดยจับฉลากตามส่วนเผ่าใหญ่และเผ่าเล็ก”

57ต่อไปนี้คือเผ่าเลวีนับตามตระกูล ได้แก่

ตระกูลเกอร์โชนจากเกอร์โชน

ตระกูลโคฮาทจากโคฮาท

ตระกูลเมรารีจากเมรารี

58ต่อไปนี้ก็คือตระกูลของเลวีด้วย ได้แก่

ตระกูลลิบนี

ตระกูลเฮโบรน

ตระกูลมาห์ลี

ตระกูลมูชี

ตระกูลโคราห์

(โคฮาทเป็นบรรพบุรุษของอัมราม 59ภรรยาของอัมรามชื่อโยเคเบดผู้เป็นเชื้อสายของเลวี ซึ่งเป็นบุตรสาวของชาวเลวี26:59 หรือโยเคเบดเป็นบุตรสาวของเลวี ที่เกิดในอียิปต์ อัมรามมีบุตรชายคืออาโรนกับโมเสส และบุตรสาวชื่อมิเรียม 60อาโรนมีบุตรชื่อ นาดับ อาบีฮู เอเลอาซาร์ และอิธามาร์ 61แต่นาดับและอาบีฮูสิ้นชีวิตไปเมื่อครั้งจุดไฟที่ไม่ได้รับอนุญาตต่อหน้าองค์พระผู้เป็นเจ้า)

62จำนวนผู้ชายทั้งหมดในตระกูลเลวีอายุหนึ่งเดือนขึ้นไปนับได้ 23,000 คน แต่ไม่ได้นับรวมเข้าในสำมะโนประชากรของอิสราเอล เพราะชาวเลวีไม่ได้รับส่วนแบ่งที่ดินเหมือนตระกูลอื่นๆ

63ทั้งหมดนี้คือสำมะโนประชากรซึ่งโมเสสและปุโรหิตเอเลอาซาร์จัดทำขึ้นในที่ราบโมอับริมแม่น้ำจอร์แดนตรงข้ามเมืองเยรีโค 64ไม่มีสักคนเดียวในสำมะโนประชากรนี้ที่มีชื่ออยู่ในสำมะโนประชากรคราวก่อนซึ่งโมเสสและปุโรหิตอาโรนทำขึ้นในถิ่นกันดารซีนาย 65ตามที่องค์พระผู้เป็นเจ้าได้ตรัสแก่ชาวอิสราเอลเหล่านั้นว่าพวกเขาจะตายในถิ่นกันดารแน่นอน ยกเว้นคาเลบบุตรเยฟุนเนห์และโยชูวาบุตรนูน