Numeri 26 – CCL & HLGN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 26:1-65

Kalembera Wachiwiri

1Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni, 2“Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.” 3Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti, 4“Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.”

Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:

5Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi:

kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki;

kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;

6kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi;

kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.

7Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.

8Mwana wa Palu anali Eliabu, 9ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova. 10Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo. 11Koma ana a Kora sanafe nawo.

12Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele;

kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini;

kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;

13kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera;

kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.

14Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.

15Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi:

kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni;

kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi;

kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;

16kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini;

kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;

17kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi;

kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.

18Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.

19Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.

20Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Sela, fuko la Asera;

kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi;

kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.

21Zidzukulu za Perezi zinali izi:

kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi;

kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.

22Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.

23Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Tola, fuko la Atola;

kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;

24kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu.

Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.

25Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.

26Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi;

kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni;

kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.

27Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.

28Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:

29Zidzukulu za Manase:

kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi);

kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.

30Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi;

kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri;

kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;

31kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli;

kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;

32kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida;

kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.

33(Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)

34Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.

35Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi;

kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela;

kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri;

kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.

36Zidzukulu za Sutela zinali izi:

kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.

37Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500.

Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.

38Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi:

kuchokera mwa Bela, fuko la Abela;

kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli;

kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;

39kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu;

kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;

40Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi:

kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi;

kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;

41Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.

42Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi:

kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu.

Izi zinali zidzukulu za Dani. 43Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.

44Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna;

kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi;

kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;

45ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya:

kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi;

kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;

46(Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)

47Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.

48Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli;

kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;

49kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri;

kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.

50Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.

51Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.

52Yehova anawuza Mose kuti, 53“Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo. 54Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa. 55Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo. 56Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”

57Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa:

kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni;

kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati;

kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.

58Awanso anali mabanja a Alevi:

banja la Alibini,

banja la Ahebroni,

banja la Amali,

banja la Amusi, fuko la Kora

banja la Akohati,

(Kohati anali abambo a Amramu. 59Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo. 60Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara. 61Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).

62Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.

63Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko. 64Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai; 65Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.

Ang Pulong Sang Dios

Numero 26:1-65

Ang Ikaduha nga Pagsensos

1Pagkatapos sang kalalat-an, nagsiling ang Ginoo kay Moises kag kay Eleazar nga anak ni Aaron nga pari, 2“Isensos ninyo ang bug-os nga katilingban sang Israel suno sa ila pamilya—tanan nga nagaedad sing 20 ka tuig paibabaw nga makasarang sa pag-alagad bilang soldado sang Israel.” 3Gani nagpakighambal si Moises kag si Eleazar nga pari sa mga Israelinhon didto sa kapatagan sang Moab sa higad sang Suba sang Jordan malapit sa Jerico. 4Nagsiling sila sa ila, “Isensos ninyo ang mga tawo nga nagaedad sing 20 ka tuig paibabaw, suno sa ginsugo sang Ginoo kay Moises.”

Amo ini ang mga Israelinhon nga nagguwa sa Egipto:

5Ang mga kaliwat ni Reuben, nga kamagulangan nga anak ni Jacob,26:5 Jacob: sa Hebreo, Israel. amo ang mga pamilya ni Hanoc, Palu, 6Hezron, kag Carmi. 7Sila amo ang mga pamilya nga naghalin kay Reuben; 43,730 sila tanan.

8Ang anak ni Palu amo si Eliab, 9kag ang mga anak ni Eliab amo sila ni Nemuel, Datan kag Abiram. Ining si Datan kag si Abiram amo ang mga pangulo sang katilingban nga nag-upod kay Kora sa pagrebelde sa Ginoo paagi sa pagkontra kay Moises kag kay Aaron. 10Pero ginlamon sila sang duta upod kay Kora, kag ang 250 nila ka sumulunod nasunog sang kalayo. Kag ini nga hitabo nangin paandam sa mga Israelinhon. 11Pero ang mga anak ni Kora wala nagkalamatay.

12Ang mga kaliwat ni Simeon amo ang mga pamilya ni Nemuel, Jamin, Jakin, 13Zera, kag Shaul. 14Sila amo ang mga pamilya nga naghalin kay Simeon; 22,200 sila tanan.

15Ang mga kaliwat ni Gad amo ang mga pamilya ni Zefon, Hagi, Shuni, 16Ozni, Eri, 17Arod, kag Areli. 18Sila amo ang mga pamilya nga naghalin kay Gad; 40,500 sila tanan.

19-20Si Juda may duha ka anak nga lalaki nga si Er kag Onan, nga napatay sa duta sang Canaan. Pero may mga kaliwat gihapon si Juda nga amo ang pamilya ni Shela, Perez, kag Zera. 21Ang mga kaliwat ni Perez amo ang pamilya ni Hezron kag ni Hamul. 22Sila amo ang mga pamilya nga naghalin kay Juda; 76,500 sila tanan.

23Ang mga kaliwat ni Isacar amo ang mga pamilya ni Tola, Pua, 24Jashub, kag Shimron. 25Sila amo ang mga pamilya nga naghalin kay Isacar; 64,300 sila tanan.

26Ang mga kaliwat ni Zebulun amo ang mga pamilya ni Sered, Elon, kag Jaleel. 27Sila amo ang mga pamilya nga naghalin kay Zebulun; 60,500 sila tanan.

28Ang mga kaliwat ni Jose naghalin sa iya duha ka anak nga si Manase kag si Efraim. 29Ang mga kaliwat ni Manase amo ang mga pamilya ni Makir kag sang iya anak nga si Gilead. 30Ang mga kaliwat ni Gilead amo ang mga pamilya ni Iezer, Helek, 31Asriel, Shekem, 32Shemida, kag Hefer. 33Ang anak ni Hefer nga si Zelofehad wala sing anak nga lalaki, pero may mga anak siya nga babayi nga ang ila mga ngalan amo sila ni Mala, Noa, Hogla, Milca, kag Tirza. 34Sila amo ang mga pamilya nga naghalin kay Manase; 52,700 sila tanan.

35Ang mga kaliwat naman ni Efraim amo ang mga pamilya ni Shutela, Beker, Tahan, 36kag sa anak ni Shutela nga si Eran. 37Sila amo ang mga pamilya nga naghalin kay Efraim; 32,500 sila tanan. Ini nga mga pamilya nga naghalin kay Manase kag Efraim amo ang mga kaliwat ni Jose.

38Ang mga kaliwat ni Benjamin amo ang mga pamilya ni Bela, Ashbel, Ahiram, 39Shufam, kag Hufam. 40Ang mga kaliwat ni Bela amo ang mga pamilya ni Ard kag Naaman. 41Sila amo ang mga pamilya nga naghalin kay Benjamin; 45,600 sila tanan.

42Ang mga kaliwat ni Dan amo ang pamilya ni Shuham. 43Ang tanan nga kaliwat ni Dan mga Shuhamnon; kag 64,400 sila tanan.

44Ang mga kaliwat ni Asher amo ang mga pamilya ni Imna, Ishvi, kag Beria. 45Ang mga kaliwat ni Beria amo ang mga pamilya ni Heber kag ni Malkiel. 46(May anak nga babayi si Asher nga si Sera.) 47Sila amo ang mga pamilya nga naghalin kay Asher; 53,400 sila tanan.

48Ang mga kaliwat ni Naftali amo ang mga pamilya ni Jazeel, Guni, 49Jezer, kag Shilem. 50Sila amo ang mga pamilya nga naghalin kay Naftali; 45,400 sila tanan.

51Gani ang bug-os nga kadamuon sang mga lalaki nga Israelinhon nga ginsensos 601,730.

52Dayon nagsiling ang Ginoo kay Moises, 53“Partihon mo sa ila ang duta bilang ila palanublion suno sa kadamuon sang kada tribo. 54Ang tribo nga madamo, partihi sing dako, kag ang tribo nga diutay partihi sing gamay. 55-56Kinahanglan nga gabot-gabutan kon diin nga parte ang makuha sang madamo kag diutay nga tribo suno sa sensos.”

57Ang mga kaliwat ni Levi amo ang mga pamilya ni Gershon, Kohat kag Merari. 58Kag sa ila naghalin ang mga pamilya ni Libni, Hebron, Mali, Mushi kag Kora.

Si Kohat amo ang katigulangan ni Amram; 59kag ang asawa ni Amram amo si Jokebed nga kaliwat man ni Levi. Natawo si Jokebed sa Egipto. Si Amram kag si Jokebed amo ang mga ginikanan ni Aaron, Moises, kag Miriam. 60Si Aaron amo ang amay nila ni Nadab, Abihu, Eleazar, kag Itamar. 61Pero napatay si Nadab kag si Abihu sang naggamit sila sang kalayo nga indi amo ang dapat nila gamiton sa ila paghalad sa Ginoo.

62Ang kadamuon sang mga lalaki nga kaliwat ni Levi nga nagaedad sing isa ka bulan paibabaw 23,000. Wala sila ginlakip sa kabilugan nga kadamuon sang mga Israelinhon kay wala sila ginpartihan sa duta nga ginpanubli sang mga Israelinhon.

63Amo ato tanan ang mga Israelinhon nga ginsensos ni Moises kag ni Eleazar nga pari didto sa kapatagan sang Moab sa higad sang Jordan malapit sa Jerico. 64Wala na sing may nabilin nga buhi sa mga nalakip sa nahauna nga sensos nga ginhimo ni Moises kag ni Aaron nga pari sa kamingawan sang Sinai. 65Kay nagsiling sadto ang Ginoo sa ila nga sigurado gid nga magkalamatay sila didto sa kamingawan, kag wala sing may makaluwas sa ila luwas lang gid kay Caleb nga anak ni Jefune kag kay Josue nga anak ni Nun.