Numeri 26 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 26:1-65

Kalembera Wachiwiri

1Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni, 2“Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.” 3Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti, 4“Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.”

Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:

5Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi:

kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki;

kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;

6kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi;

kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.

7Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.

8Mwana wa Palu anali Eliabu, 9ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova. 10Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo. 11Koma ana a Kora sanafe nawo.

12Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele;

kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini;

kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;

13kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera;

kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.

14Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.

15Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi:

kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni;

kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi;

kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;

16kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini;

kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;

17kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi;

kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.

18Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.

19Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.

20Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Sela, fuko la Asera;

kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi;

kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.

21Zidzukulu za Perezi zinali izi:

kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi;

kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.

22Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.

23Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Tola, fuko la Atola;

kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;

24kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu.

Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.

25Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.

26Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi;

kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni;

kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.

27Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.

28Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:

29Zidzukulu za Manase:

kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi);

kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.

30Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi;

kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri;

kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;

31kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli;

kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;

32kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida;

kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.

33(Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)

34Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.

35Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi;

kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela;

kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri;

kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.

36Zidzukulu za Sutela zinali izi:

kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.

37Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500.

Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.

38Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi:

kuchokera mwa Bela, fuko la Abela;

kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli;

kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;

39kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu;

kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;

40Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi:

kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi;

kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;

41Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.

42Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi:

kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu.

Izi zinali zidzukulu za Dani. 43Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.

44Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna;

kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi;

kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;

45ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya:

kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi;

kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;

46(Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)

47Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.

48Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli;

kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;

49kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri;

kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.

50Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.

51Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.

52Yehova anawuza Mose kuti, 53“Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo. 54Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa. 55Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo. 56Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”

57Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa:

kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni;

kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati;

kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.

58Awanso anali mabanja a Alevi:

banja la Alibini,

banja la Ahebroni,

banja la Amali,

banja la Amusi, fuko la Kora

banja la Akohati,

(Kohati anali abambo a Amramu. 59Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo. 60Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara. 61Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).

62Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.

63Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko. 64Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai; 65Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Números 26:1-65

Segundo censo de las tribus de Israel

1Después de la mortandad, el Señor les dijo a Moisés y al sacerdote Eleazar hijo de Aarón: 2«Haced un censo de toda la comunidad israelita por sus familias patriarcales. Alistad a los varones mayores de veinte años que sean aptos para el servicio militar en Israel».

3Moisés y el sacerdote Eleazar hablaron con el pueblo en las llanuras de Moab, cerca del Jordán, a la altura de Jericó, y le ordenaron 4levantar un censo de todos los varones mayores de veinte años, tal como el Señor se lo había mandado a Moisés.

Los israelitas que salieron de Egipto fueron los siguientes:

5-6De Enoc, Falú, Jezrón y Carmí, hijos de Rubén, el primogénito de Israel, proceden los siguientes clanes: los enoquitas, los faluitas, los jezronitas y los carmitas. 7Estos son los clanes de la tribu de Rubén. Su número llegó a cuarenta y tres mil setecientos treinta hombres.

8Eliab fue el único hijo de Falú. 9Los hijos de Eliab fueron Nemuel, Datán y Abirán. Estos son los mismos Datán y Abirán que, no obstante haber sido escogidos por la comunidad como oficiales, se rebelaron contra Moisés y Aarón junto con la facción de Coré cuando este último se rebeló contra el Señor. 10En esa ocasión, la tierra abrió sus fauces y se los tragó junto con Coré, muriendo también sus seguidores. El fuego devoró a doscientos cincuenta hombres, y este hecho los convirtió en una señal de advertencia. 11Sin embargo, los hijos de Coré no perecieron.

12-13De Nemuel, Jamín, Zera y Saúl, hijos de Simeón, proceden los siguientes clanes: los nemuelitas, los jaminitas, los zeraítas y los saulitas. 14Estos son los clanes de la tribu de Simeón. Su número llegó a veintidós mil doscientos hombres.

15-17De Zefón, Jaguí, Suni, Ozni, Erí, Arodí y Arelí, hijos de Gad, proceden los siguientes clanes: los zefonitas, los jaguitas, los sunitas, los oznitas, los eritas, los aroditas y los arelitas. 18Estos son los clanes de la tribu de Gad. Su número llegó a cuarenta mil quinientos hombres.

19-20Er y Onán eran hijos de Judá, pero ambos murieron en Canaán. De sus hijos Selá, Fares y Zera proceden los siguientes clanes: los selaítas, los faresitas y los zeraítas.

21De Jezrón y de Jamul, hijos de Fares, proceden los clanes jezronitas y jamulitas. 22Estos son los clanes de la tribu de Judá. Su número llegó a setenta y seis mil quinientos hombres.

23-24De Tola, Fuvá, Yasub y Simrón, hijos de Isacar, proceden los siguientes clanes: los tolaítas, los fuvitas, los yasubitas y los simronitas. 25Estos son los clanes de la tribu de Isacar. Su número llegó a sesenta y cuatro mil trescientos hombres.

26De Séred, Elón y Yalel, hijos de Zabulón, proceden los siguientes clanes: los sereditas, los elonitas y los yalelitas. 27Estos son los clanes de la tribu de Zabulón. Su número llegó a sesenta mil quinientos hombres.

28De Manasés y Efraín, hijos de José, proceden los siguientes clanes:

29De Maquir hijo de Manasés y de Galaad hijo de Maquir proceden el clan maquirita y el clan galaadita.

30-32De Jezer, Jélec, Asriel, Siquén, Semidá y Héfer, hijos de Galaad, proceden los siguientes clanes: los jezeritas, los jelequitas, los asrielitas, los siquenitas, los semidaítas y los heferitas. 33Zelofejad hijo de Héfer no tuvo hijos, sino solo hijas, cuyos nombres eran Majlá, Noa, Joglá, Milca y Tirsá. 34Estos son los clanes de la tribu de Manasés. Su número llegó a cincuenta y dos mil setecientos hombres.

35De Sutela, Béquer y Taján, hijos de Efraín, proceden los siguientes clanes: los sutelaítas, los bequeritas y los tajanitas.

36De Erán hijo de Sutela procede el clan de los eranitas. 37Estos son los clanes de la tribu de Efraín. Su número llegó a treinta y dos mil quinientos hombres.

Todos estos clanes descendieron de José.

38-39De Bela, Asbel, Ajirán, Sufán y Jufán, hijos de Benjamín, proceden los siguientes clanes: los belaítas, los asbelitas, los ajiranitas, los sufanitas y los jufanitas.

40De Ard y Naamán, hijos de Bela, proceden los clanes de los arditas y de los naamanitas. 41Estos son los clanes de la tribu de Benjamín. Su número llegó a cuarenta y cinco mil seiscientos hombres.

42De Suján hijo de Dan procede el clan de los sujanitas, que fueron los únicos clanes danitas. 43Su número llegó a sesenta y cuatro mil cuatrocientos hombres.

44De Imná, Isví y Beriá, hijos de Aser, proceden los siguientes clanes: los imnaítas, los isvitas y los beriaítas.

45De Héber y Malquiel, hijos de Beriá, proceden los clanes de los heberitas y de los malquielitas. 46Aser tuvo una hija llamada Sera. 47Estos son los clanes de la tribu de Aser. Su número llegó a cincuenta y tres mil cuatrocientos hombres.

48-49De Yazel, Guní, Jéser y Silén, hijos de Neftalí, proceden los siguientes clanes: los yazelitas, los gunitas, los jeseritas y los silenitas. 50Estos son los clanes de la tribu de Neftalí. Su número llegó a cuarenta y cinco mil cuatrocientos hombres.

51Los hombres de Israel eran en total seiscientos un mil setecientos treinta.

Instrucciones para el reparto de la tierra

52El Señor le dijo a Moisés: 53«Reparte la tierra entre estas tribus para que sea su heredad. Hazlo según el número de nombres registrados. 54A la tribu más numerosa le darás la heredad más grande, y a la tribu menos numerosa le darás la heredad más pequeña. Cada tribu recibirá su heredad en proporción al número de censados. 55La tierra deberá repartirse por sorteo, según el nombre de las tribus patriarcales. 56El sorteo se hará entre todas las tribus, grandes y pequeñas».

Censo de los levitas

57De los levitas Guersón, Coat y Merari proceden los clanes guersonitas, coatitas y meraritas.

58De los levitas proceden también los siguientes clanes: los libnitas, los hebronitas, los majlitas, los musitas y los coreítas. Coat fue el padre de Amirán. 59La esposa de Amirán se llamaba Jocabed hija de Leví, y había nacido en Egipto. Los hijos que ella tuvo de Amirán fueron Aarón y Moisés, y su hermana Miriam. 60Aarón fue el padre de Nadab, Abiú, Eleazar e Itamar, 61pero Nadab y Abiú murieron bajo el juicio del Señor por haberle ofrecido fuego profano.

62Los levitas mayores de un mes de edad fueron en total veintitrés mil. Pero no fueron censados junto con los demás israelitas porque no habrían de recibir heredad entre ellos.

63Estos fueron los israelitas censados por Moisés y el sacerdote Eleazar, cuando los contaron en las llanuras de Moab, cerca del río Jordán, a la altura de Jericó. 64Entre los censados no figuraba ninguno de los registrados en el censo que Moisés y Aarón habían hecho antes en el desierto del Sinaí, 65porque el Señor había dicho que todos morirían en el desierto. Con la excepción de Caleb hijo de Jefone y de Josué hijo de Nun, ninguno de ellos quedó con vida.