Numeri 26 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 26:1-65

Kalembera Wachiwiri

1Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni, 2“Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.” 3Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti, 4“Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.”

Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:

5Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi:

kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki;

kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;

6kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi;

kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.

7Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.

8Mwana wa Palu anali Eliabu, 9ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova. 10Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo. 11Koma ana a Kora sanafe nawo.

12Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele;

kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini;

kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;

13kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera;

kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.

14Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.

15Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi:

kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni;

kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi;

kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;

16kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini;

kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;

17kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi;

kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.

18Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.

19Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.

20Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Sela, fuko la Asera;

kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi;

kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.

21Zidzukulu za Perezi zinali izi:

kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi;

kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.

22Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.

23Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Tola, fuko la Atola;

kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;

24kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu.

Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.

25Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.

26Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi;

kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni;

kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.

27Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.

28Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:

29Zidzukulu za Manase:

kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi);

kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.

30Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi;

kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri;

kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;

31kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli;

kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;

32kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida;

kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.

33(Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)

34Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.

35Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi;

kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela;

kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri;

kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.

36Zidzukulu za Sutela zinali izi:

kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.

37Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500.

Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.

38Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi:

kuchokera mwa Bela, fuko la Abela;

kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli;

kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;

39kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu;

kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;

40Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi:

kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi;

kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;

41Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.

42Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi:

kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu.

Izi zinali zidzukulu za Dani. 43Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.

44Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna;

kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi;

kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;

45ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya:

kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi;

kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;

46(Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)

47Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.

48Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli;

kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;

49kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri;

kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.

50Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.

51Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.

52Yehova anawuza Mose kuti, 53“Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo. 54Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa. 55Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo. 56Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”

57Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa:

kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni;

kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati;

kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.

58Awanso anali mabanja a Alevi:

banja la Alibini,

banja la Ahebroni,

banja la Amali,

banja la Amusi, fuko la Kora

banja la Akohati,

(Kohati anali abambo a Amramu. 59Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo. 60Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara. 61Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).

62Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.

63Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko. 64Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai; 65Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Числа 26:1-65

Вторая перепись исроильского народа

1После мора Вечный сказал Мусо и Элеазару, сыну священнослужителя Хоруна:

2– Сделайте перепись всего народа Исроила, годных к военной службе, от двадцати лет и старше, по семьям их отцов.

3На равнинах Моава у реки Иордан, напротив города Иерихона, Мусо и священнослужитель Элеазар говорили с ними и сказали:

4– Сделайте перепись исроильтян от двадцати лет и старше, как повелел Мусо Вечный.

Вот исроильтяне, которые вышли из Египта:

5Потомки Рувима, первенца Исроила:

через Ханоха – клан ханохитов;

через Фаллу – клан фаллуитов;

6через Хецрона – клан хецронитов;

через Харми – клан хармитов.

7Это кланы Рувима; исчислено было 43 730 человек.

8Сыном Фаллу был Элиав, 9а сыновьями Элиава – Немуил, Датан и Авирам. Датан и Авирам были знатными людьми. Они восстали против Мусо и Хоруна и оказались среди сообщников Кораха, когда те восстали против Вечного. 10Земля разверзлась и поглотила их вместе с Корахом, сообщники которого погибли, когда огонь сжёг двести пятьдесят человек. Они стали предостережением. 11Но сыновья Кораха не погибли в тот день.

12Потомки Шимона по их кланам:

через Немуила – клан немуилитов;

через Иамина – клан иаминитов;

через Иахина – клан иахинитов;

13через Зераха – клан зерахитов;

через Шаула – клан шаулитов.

14Это кланы Шимона; 22 200 человек.

15Потомки Гада по их кланам:

через Цефона – клан цефонитов;

через Хагги – клан хаггитов;

через Шуни – клан шунитов;

16через Озни – клан ознитов;

через Ери – клан еритов;

17через Ароди – клан ародитов;

через Арели – клан арелитов.

18Это кланы Гада; исчислено было 40 500 человек.

19Сыновьями Иуды были Ир и Онан. Они умерли в Ханоне.

20Потомки Иуды по их кланам:

через Шелу – клан шеланитов;

через Фареца – клан фарецитов;

через Зераха – клан зерахитов;

21Потомки Фареца:

через Хецрона – клан хецронитов;

через Хамула – клан хамулитов.

22Это кланы Иуды; исчислено было 76 500 человек.

23Потомки Иссокора по их кланам:

через Толу – клан толаитов;

через Пуа – клан пуанитов;

24через Иашува – клан иашувитов;

через Шимрона – клан шимронитов.

25Это кланы Иссокора; исчислено было 64 300 человек.

26Потомки Завулона по их кланам:

через Середа – клан середитов;

через Елона – клан елонитов;

через Иахлеила – клан иахлеилитов.

27Это кланы Завулона; исчислено было 60 500 человек.

28Потомки Юсуфа по их кланам через Манассу и Ефраима:

29Потомки Манассы:

через Махира – клан махиритов (Махир был отцом Галаада);

через Галаада – клан галаадитов.

30Вот потомки Галаада:

через Иезера – клан иезеритов;

через Хелека – клан хелекитов;

31через Асриила – клан асриилитов;

через Шахема – клан шахемитов,

32через Шемиду – клан шемидитов;

через Хефера – клан хеферитов.

33(У Целофхада, сына Хефера, не было сыновей; у него были только дочери; их звали Махла, Ноа, Хогла, Милка и Тирца.)

34Это кланы Манассы; исчислено было 52 700 человек.

35Вот потомки Ефраима по их кланам:

через Шутелаха – клан шутелахитов;

через Бехера – клан бехеритов;

через Тахана – клан таханитов.

36Вот потомки Шутелаха:

через Ерана – клан еранитов.

37Это кланы Ефраима; исчислено было 32 500 человек.

Это потомки Юсуфа по их кланам.

38Потомки Вениамина по их кланам:

через Белу – клан белаитов;

через Ашбела – клан ашбелитов;

через Ахирама – клан ахирамитов;

39через Шуфама – клан шуфамитов;

через Хуфама – клан хуфамитов.

40Потомки Белы через Арда и Наамана:

через Арда – клан ардитов;

через Наамана – клан нааманитов.

41Это кланы Вениамина; исчислено было 45 600 человек.

42Вот потомки Дона по их кланам:

через Шухама – клан шухамитов.

Это кланы Дона: 43все они были кланами шухамитов; исчислено было 64 400 человек.

44Потомки Ошера по их кланам:

через Имну – клан имнитов;

через Ишви – клан ишвитов;

через Брию – клан бриитов;

45а через потомков Брии:

через Хевера – клан хеверитов;

через Малкиила – клан малкиилитов.

46(У Ошера была дочь, которую звали Серах.)

47Это кланы Ошера; исчислено было 53 400 человек.

48Потомки Неффалима по их кланам:

через Иахцеила – клан иахцеилитов;

через Гуни – клан гунитов;

49через Иецера – клан иецеритов;

через Шиллема – клан шиллемитов.

50Это кланы Неффалима; исчислено было 45 400 человек.

51Всего исроильтян было 601 730 человек.

52Вечный сказал Мусо:

53– Землю нужно разделить между родами по числу людей. 54Большему роду дай больший удел, а меньшему – меньший. Пусть каждый род получит надел по количеству исчисленных. 55Пусть земля будет распределяться по жребию. Они получат наделы по числу людей в родах. 56Пусть каждый надел распределяется по жребию между более и менее многочисленными.

57Левиты, исчисленные по их кланам:

через Гершона – клан гершонитов;

через Каафа – клан каафитов;

через Мерари – клан мераритов.

58Вот кланы левитов:

клан ливнитов;

клан хевронитов;

клан махлитов;

клан мушитов;

клан корахитов.

(Кааф был предком Амрама. 59Жену Амрама звали Иохеведа, она была из потомков Леви и родилась среди левитов26:59 Или: «Иохеведа, дочь Леви, которая родилась у Леви». в Египте. Амраму она родила Хоруна, Мусо и их сестру Марьям. 60Хорун был отцом Надава и Авиуда, Элеазара и Итамара. 61Но Надав и Авиуд умерли, когда принесли Вечному чуждый огонь26:61 См. Лев. 10:1-2..)

62Всех исчисленных мужчин-левитов от месяца и старше было 23 000 человек. Они не были исчислены с остальными исроильтянами, потому что не получили своего надела.

63Вот те, кого исчислили Мусо и священнослужитель Элеазар, когда они считали исроильтян на равнинах Моава у реки Иордан, напротив города Иерихона. 64Среди них не было никого, кто был исчислен Мусо и священнослужителем Хоруном, когда они считали исроильтян в Синайской пустыне. 65Ведь Вечный сказал им, что они непременно умрут в пустыне, и из них не осталось никого, кроме Халева, сына Иефоннии, и Иешуа, сына Нуна.