Numeri 26 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 26:1-65

Kalembera Wachiwiri

1Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni, 2“Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.” 3Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti, 4“Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.”

Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:

5Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi:

kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki;

kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;

6kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi;

kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.

7Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.

8Mwana wa Palu anali Eliabu, 9ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova. 10Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo. 11Koma ana a Kora sanafe nawo.

12Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele;

kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini;

kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;

13kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera;

kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.

14Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.

15Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi:

kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni;

kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi;

kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;

16kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini;

kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;

17kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi;

kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.

18Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.

19Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.

20Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Sela, fuko la Asera;

kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi;

kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.

21Zidzukulu za Perezi zinali izi:

kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi;

kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.

22Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.

23Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Tola, fuko la Atola;

kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;

24kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu.

Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.

25Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.

26Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi;

kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni;

kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.

27Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.

28Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:

29Zidzukulu za Manase:

kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi);

kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.

30Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi;

kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri;

kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;

31kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli;

kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;

32kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida;

kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.

33(Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)

34Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.

35Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi;

kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela;

kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri;

kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.

36Zidzukulu za Sutela zinali izi:

kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.

37Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500.

Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.

38Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi:

kuchokera mwa Bela, fuko la Abela;

kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli;

kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;

39kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu;

kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;

40Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi:

kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi;

kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;

41Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.

42Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi:

kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu.

Izi zinali zidzukulu za Dani. 43Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.

44Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna;

kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi;

kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;

45ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya:

kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi;

kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;

46(Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)

47Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.

48Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli;

kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;

49kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri;

kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.

50Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.

51Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.

52Yehova anawuza Mose kuti, 53“Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo. 54Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa. 55Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo. 56Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”

57Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa:

kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni;

kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati;

kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.

58Awanso anali mabanja a Alevi:

banja la Alibini,

banja la Ahebroni,

banja la Amali,

banja la Amusi, fuko la Kora

banja la Akohati,

(Kohati anali abambo a Amramu. 59Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo. 60Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara. 61Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).

62Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.

63Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko. 64Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai; 65Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.

Bibelen på hverdagsdansk

4. Mosebog 26:1-65

1sagde Herren til Moses og præsten Eleazar, Arons søn: 2„Lav en optælling over samtlige israelitiske mænd over 20 år, så I ved, hvor mange våbenføre mænd hver enkelt stamme og slægt kan bidrage med.” 3-4Så optalte Moses og Eleazar folket, mens de lå i lejr på Moabs sletter ved Jordanfloden over for Jeriko. Her følger resultatet af denne anden mønstring, stamme for stamme, slægt for slægt:

5Først Rubens stamme (Ruben var jo Jakobs førstefødte søn): Stammen bestod af følgende slægter, opkaldt efter Rubens sønner: hanokitterne opkaldt efter Hanok; palluitterne opkaldt efter Pallu; 6hesronitterne opkaldt efter Hesron; karmitterne opkaldt efter Karmi. 7Fra Rubens slægter mønstredes der 43.730 våbenføre mænd.

8Eliab, der var søn af Pallu, 9havde tre sønner: Nemuel, Datan og Abiram. Det var Datan og Abiram, der sammen med Kora gjorde oprør imod Moses og Aron—ja, imod Herren selv. 10Derfor åbnede jorden sit gab og opslugte dem, så de sammen med de 250 mænd, der blev brændt op af Herrens ild, blev til skræk og advarsel for hele folket. 11Koras slægt uddøde dog ikke.

12Dernæst Simeons stamme, som bestod af følgende slægter, opkaldt efter Simeons sønner: nemuelitterne opkaldt efter Nemuel; jaminitterne opkaldt efter Jamin; jakinitterne opkaldt efter Jakin; 13zerahitterne opkaldt efter Zerach; shaulitterne opkaldt efter Shaul. 14Fra Simeons slægter mønstredes i alt 22.200 mand.

15Gads stamme bestod af følgende slægter, opkaldt efter Gads sønner: zefonitterne opkaldt efter Zefon; haggitterne opkaldt efter Haggi; shunitterne opkaldt efter Shuni; 16oznitterne opkaldt efter Ozni; eritterne opkaldt efter Eri; 17aroditterne opkaldt efter Arod; arelitterne opkaldt efter Areli. 18Fra Gads slægter i alt 40.500 mand.

19Dernæst Judas stamme: Judas sønner Er og Onan, der døde i Kana’an, er ikke medregnet. 20Stammens slægter er opkaldt efter Judas øvrige sønner: shelanitterne opkaldt efter Shela; peretzitterne opkaldt efter Peretz; zerahitterne opkaldt efter Zerach. 21Peretzitterne var yderligere opdelt i hesronitterne, opkaldt efter Hesron, og hamulitterne, opkaldt efter Hamul, begge sønner af Peretz. 22Fra Judas slægter i alt 76.500 mand.

23Issakars stamme bestod af følgende slægter, opkaldt efter Issakars sønner: tolaitterne opkaldt efter Tola; punitterne opkaldt efter Pua; 24jashubitterne opkaldt efter Jashub; shimronitterne opkaldt efter Shimron. 25Fra Issakars slægter i alt 64.300 mand.

26Zebulons stamme bestod af følgende slægter, opkaldt efter Zebulons sønner: sereditterne opkaldt efter Sered; elonitterne opkaldt efter Elon; jale’elitterne opkaldt efter Jale’el. 27Fra Zebulons slægter i alt 60.500 mand.

28To stammer udsprang fra Josefs to sønner: Manasse og Efraim. 29Manasses stamme bestod af makiritterne, opkaldt efter Manasses søn Makir, og gileaditterne, opkaldt efter Makirs søn Gilead. 30Gileaditterne var opdelt i følgende slægter: iezritterne opkaldt efter Iezer; helekitterne opkaldt efter Helek; 31asrielitterne opkaldt efter Asriel; shekemitterne opkaldt efter Shekem; 32shemidaitterne opkaldt efter Shemida; heferitterne opkaldt efter Hefer. 33Hefers søn Zelofhad havde ingen sønner, men fem døtre ved navn Mala, Noa, Hogla, Milka og Tirtza. 34Fra Manasses slægter var der i alt 52.700 mand.

35Efraims stamme bestod af følgende slægter, opkaldt efter Efraims sønner: shutelaitterne opkaldt efter Shutela; bekeritterne opkaldt efter Beker; tahanitterne opkaldt efter Tahan. 36Shutela fik sønnen Eran, hvorfra eranitterne stammer. 37Fra Efraims slægter var der i alt 32.500 mand.

38Benjamins stamme bestod af følgende slægter, opkaldt efter Benjamins sønner: belaitterne opkaldt efter Bela; ashbelitterne opkaldt efter Ashbel; ahiramitterne opkaldt efter Ahiram; 39shufamitterne opkaldt efter Shufam; hufamitterne opkaldt efter Hufam. 40Bela fik sønnerne Ard og Na’aman, hvorfra arditterne og na’amitterne stammer. 41Fra Benjamins slægter var der i alt 45.600 mand.

42-43Dans stamme bestod af shuhamitterne, opkaldt efter Shuham,26,42-43 Også kaldet Hushim, se 1.Mos. 46,23. Dans søn. Fra Dans stamme var der 64.400 mand.

44Ashers stamme bestod af følgende slægter, opkaldt efter Ashers sønner: jimnitterne opkaldt efter Jimna; jishvitterne opkaldt efter Jishvi; beriaitterne opkaldt efter Beria. 45Følgende slægter stammer fra Berias sønner Heber og Malkiel: heberitterne og malkielitterne. 46Asher havde en datter ved navn Sera. 47Fra Ashers slægter var der i alt 53.400 mand.

48Naftalis stamme bestod af følgende slægter, opkaldt efter Naftalis sønner: jahtze’elitterne opkaldt efter Jahtze’el; gunitterne opkaldt efter Guni; 49jetzeritterne opkaldt efter Jetzer; shillemitterne opkaldt efter Shillem. 50Fra Naftalis slægter i alt 45.400 mand.

51Det samlede antal våbenføre israelitiske mænd over 20 år var altså 601.730.

52-54Derefter sagde Herren til Moses: „Du skal fordele landet mellem stammerne i forhold til stammernes størrelse, således at de store stammer vil få et stort landområde, og de mindre stammer vil få et mindre landområde. 55Der skal kastes lod om rækkefølgen af fordelingen mellem stammerne. 56Nogle vil få et stort område, andre et mindre område, alt sammen ved lodkastning.”

57Levis stamme bestod af følgende slægter: gershonitterne opkaldt efter Gershon; kehatitterne opkaldt efter Kehat; meraritterne opkaldt efter Merari. 58-59Under dem hørte følgende slægter: libnitterne, hebronitterne, mahlitterne, mushitterne og koraitterne.

En af Kehats efterkommere hed Amram, som i Egypten blev gift med Jokebed af Levis stamme, hvorefter hun fødte Aron, Moses og Mirjam. 60Aron fik sønnerne Nadab, Abihu, Eleazar og Itamar. 61Nadab og Abihu døde, fordi de bragte et røgelsesoffer, der var i modstrid med Herrens befalinger.

62Det samlede antal levitter af hankøn fra en måned og opefter var 23.000. Levitterne blev imidlertid ikke regnet med i folketællingen, for de fik ikke arvelod i landet sammen med de øvrige stammer.

63Det var så resultatet af den folketælling, som Moses og præsten Eleazar holdt på Moabs sletter ved Jordanfloden over for Jeriko. 64-65Ikke en eneste af alle disse mennesker var med i den første folketælling, som Moses og præsten Aron havde foretaget i Sinaiørkenen; alle, der havde været med i den første optælling, var døde i mellemtiden, sådan som Herren havde sagt: „De skal alle dø i ørkenen.” De eneste, der var tilbage fra dengang, var Kaleb og Josva.