Numeri 24 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 24:1-25

1Tsopano Balaamu ataona kuti kunakomera Yehova kudalitsa Israeli, sanapitenso ku mawula monga ankachitira kale, koma kuyangʼana ku chipululu. 2Balaamu atayangʼana, anaona Aisraeli atamanga misasa yawo fuko ndi fuko. Pamenepo mzimu wa Mulungu unabwera pa iye 3ndipo ananena uthenga wake:

“Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori,

uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka,

4uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu,

yemwe amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse,

yemwe amagwa chafufumimba, koma maso ake ali chipenyere:

5“Matenti ako ndi okongola kwambiri iwe Yakobo,

misasa yako, iwe Israeli!

6“Monga zigwa zotambalala,

monga minda mʼmbali mwa mtsinje,

monga aloe wodzalidwa ndi Yehova,

monga mikungudza mʼmbali mwa madzi.

7Madzi adzayenderera mʼmitsuko yake;

mbewu zake zidzakhala ndi madzi ambiri.

“Mfumu yake idzakhala yamphamvu kuposa Agagi;

ufumu wake udzakwezedwa.

8“Mulungu womutulutsa mʼdziko la Igupto

ali ndi mphamvu ngati za njati.

Amawononga mitundu yomuwukira

ndi kuphwanya mafupa awo,

amalasa ndi mivi yake.

9Monga mkango waumuna, amabisala nagona pansi,

monga mkango waukazi, adzamuputa ndani?

“Amene adalitsa iwe, adalitsike

ndipo amene atemberera iwe, atembereredwe!”

10Kenaka Balaki anakwiyira Balaamu. Anawomba mʼmanja ndi kunena naye kuti, “Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, koma taona, wawadalitsa katatu konseka. 11Tsopano choka msanga uzipita kwanu! Ndinanena kuti ndidzakulipira bwino kwambiri, koma Yehova sanafune kuti ulandire malipirowo.”

12Balaamu anayankha Balaki kuti, “Kodi sindinawawuze amithenga amene munawatumiza kwa ine, 13kuti ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yake yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingathe kuchita zinthu mwa ine ndekha, zabwino kapena zoyipa, kuposa lamulo la Yehova ndi kuti ndiyenera kunena zokhazo zimene Yehova akunena? 14Tsopano ndikupita kwa anthu anga, koma tabwerani ndikuchenjezeni zimene anthu awa adzachitira anthu anu masiku akubwerawa.”

Uthenga Wachinayi wa Balaamu

15Ndipo iye ananena uthenga wake nati,

“Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori,

uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka.

16Uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu,

amene ali ndi nzeru zochokera kwa Wammwambamwamba,

amene amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse,

amene amagwa chafufumimba koma diso lake lili lotsekuka:

17“Ndikumuona iye koma osati tsopano;

ndikumupenya iye koma osati pafupi.

Nyenyezi idzatuluka mwa Yakobo;

ndodo yaufumu idzatuluka mwa Israeli.

Iye adzagonjetsa Mowabu

ndi kugonjetsa ana onse a Seti.

18Edomu adzagonjetsedwa;

Seiri, mdani wake, adzawonongedwa

koma mphamvu za Israeli zidzachuluka.

19Wolamulira adzachokera mwa Yakobo

ndipo adzawononga otsala a mu mzindamo.”

Uthenga Wachisanu wa Balaamu

20Kenaka Balaamu anaona Aamaleki ndipo ananena uthenga wake uwu:

“Aamaleki anali oyamba mwa mitundu ya anthu

koma potsiriza pake adzawonongeka.”

Uthenga Wachisanu ndi Chimodzi wa Balaamu

21Kenaka anaonanso Akeni ndipo ananena uthenga wake,

“Malo amene mukukhalamo ndi otetezedwa,

chisa chanu chinayikidwa pa thanthwe;

22komabe inu Akeni mudzawonongedwa,

pamene Asuri adzakutengeni ukapolo.”

Uthenga Wachisanu ndi Chiwiri wa Balaamu

23Ndipo ananenanso uthenga wina kuti,

“Aa, ndani adzakhala ndi moyo Mulungu akachita zimenezi?

24Sitima zapamadzi zidzabwera kuchokera ku madooko a Kitimu;

kupondereza Asuri ndi Eberi,

koma iwonso adzawonongeka.”

25Pamenepo Balaamu ananyamuka ndi kubwerera kwawo ndipo Balaki anapitanso njira yake.

Hoffnung für Alle

4. Mose 24:1-25

Der dritte Segen

1Bileam wusste nun, dass der Herr Israel segnen wollte. Deshalb versuchte er nicht, ihn durch Zauberei zu befragen, wie er es vorher getan hatte. Stattdessen wandte er sich der Steppe zu 2und richtete seinen Blick auf die Israeliten, die dort nach Stämmen geordnet lagerten. Der Geist Gottes kam über ihn, und er begann seine Rede:

3»Dies sagt Bileam, der Sohn von Beor, dies sagt der, dem Gott die Augen öffnet, 4der Gottes Worte hört. Der Allmächtige gibt ihm Visionen, und er fällt zu Boden und sieht verborgene Dinge.

5Wie schön sind eure Zelte, ihr Nachkommen von Jakob! Wie prächtig sind eure Wohnungen, ihr Israeliten!

6Wie weite Täler liegen sie da, wie Gärten am Fluss, sie stehen wie Aloebäume, die der Herr gepflanzt hat, und wie Zedern am Bach.

7Eure Brunnen werden stets voll Wasser sein, eure Saat wird auf fruchtbaren Feldern gedeihen. Euer König wird mächtiger sein als Agag, er herrscht über ein gewaltiges Reich.

8Gott hat euch aus Ägypten hierhergeführt, er macht euch stark wie einen wilden Stier. Ihr verschlingt die Völker, die sich euch entgegenstellen; ihr zerbrecht ihnen die Knochen und tötet sie mit euren Pfeilen.

9Israel liegt da wie ein Löwe, es ruht wie eine Löwin. Wer wagt es, sie zu reizen? Wer euch segnet, wird selbst gesegnet, und wer euch verflucht, wird selbst verflucht.«

10Als er das hörte, geriet Balak außer sich vor Wut. Er ballte die Fäuste und schrie Bileam an: »Ich habe dich hierhergeholt, damit du meine Feinde verfluchst! Und was tust du? Du segnest sie, und das gleich dreimal! 11Verschwinde, mach, dass du nach Hause kommst! Ich hatte versprochen, dich reich zu belohnen. Doch daraus wird nichts. Der Herr hat es nicht gewollt.« 12Bileam erwiderte: »Du weißt, dass ich schon zu deinen Boten gesagt habe: 13›Selbst wenn Balak mir seinen eigenen Palast voller Gold und Silber gibt, kann ich nichts tun, was der Herr mir verbietet. Ich kann nicht eigenmächtig einen Segen oder einen Fluch aussprechen, sondern nur das sagen, was der Herr mir aufträgt.‹ 14So kehre ich jetzt wieder in meine Heimat zurück. Aber vorher will ich dir noch zeigen, was Israel schließlich mit deinem Volk machen wird. Komm und hör zu!«

Die vierte Rede Bileams

15Dann begann Bileam noch einmal:

»Dies sagt Bileam, der Sohn Beors, dies sagt der, dem Gott die Augen öffnet, 16der Gottes Worte hört und den Höchsten kennt. Der Allmächtige gibt ihm Visionen, und er fällt zu Boden und sieht verborgene Dinge:

17Ich sehe jemanden in weiter Ferne. Noch ist er nicht da, aber ich kann ihn schon erkennen. Ein Stern steigt auf bei den Nachkommen von Jakob, ein Zepter erhebt sich in Israel. Es zerschmettert Moab den Schädel und zerschlägt sein wildes Kriegsvolk.

18Es unterwirft seine edomitischen Feinde und nimmt ihr Land Seïr in Besitz, ja, Israel vollbringt Gewaltiges!

19Ein Herrscher steht auf unter den Nachkommen von Jakob und vertreibt den Rest der Edomiter aus ihren Städten.«

20Dann sah Bileam die Amalekiter vor sich und sagte: »Als erstes Volk trat Amalek den Israeliten entgegen, am Ende jedoch wird es für immer untergehen.«

21Nun sah Bileam die Keniter. Über sie sagte er: »Eure Städte sind sicher wie ein Adlernest hoch oben in den Felsen.

22Und doch werdet ihr vernichtet werden, wenn die Assyrer euch gefangen fortschleppen!«

23Zuletzt sagte Bileam: »Lasst euch warnen! Wer wird am Leben bleiben, wenn Gott das alles tut?

24Kriegsschiffe kommen vom Mittelmeer24,24 Wörtlich: von der Küste der Kittäer. – Die Kittäer waren ursprünglich die Bewohner Zyperns und stehen hier für den gesamten Mittelmeerraum., sie unterwerfen die Assyrer und die Nachkommen Ebers und werden dann selbst vernichtet.«

25Nach diesen Worten brach Bileam in seine Heimat auf, und auch Balak ging davon.